Masalimo 98 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 98:1-9

Salimo 98

Salimo.

1Imbirani Yehova nyimbo yatsopano,

pakuti Iyeyo wachita zinthu zodabwitsa;

dzanja lake lamanja ndi mkono wake woyera

zamuchitira chipulumutso.

2Yehova waonetsa chipulumutso chake

ndipo waulula chilungamo chake kwa anthu a mitundu ina.

3Iye wakumbukira chikondi chake

ndi kukhulupirika kwake pa Aisraeli;

malekezero onse a dziko lapansi aona

chipulumutso cha Mulungu wathu.

4Fuwulani mwachimwemwe kwa Yehova, dziko lonse lapansi,

muyimbireni nyimbo mofuwula ndi mokondwera.

5Imbirani Yehova nyimbo ndi zeze,

ndi zeze ndi mawu a kuyimba,

6ndi malipenga ndi kuliza kwa nyanga ya nkhosa yayimuna

fuwulani mwachimwemwe pamaso pa Yehova Mfumu.

7Nyanja ikokome pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo,

dziko lonse ndi onse amene amakhala mʼmenemo.

8Mitsinje iwombe mʼmanja mwawo,

mapiri ayimbe pamodzi mwachimwemwe;

9izo ziyimbe pamaso pa Yehova,

pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi.

Adzaweruza dziko lonse mwachilungamo,

ndi mitundu ya anthu mosakondera.

Hoffnung für Alle

Psalm 98:1-9

Freut euch mit uns – Gott hat uns befreit!

1Ein Lied.

Singt dem Herrn ein neues Lied,

denn er hat Wunder getan!

Der heilige Gott hat den Sieg errungen

durch seine gewaltige Kraft.

2Alle Völker konnten sehen, wie der Herr befreit,

seine Gerechtigkeit hielt er der Welt vor Augen!

3Er erfüllte das Versprechen, seinem Volk gnädig und treu zu sein.

Bis in die fernsten Länder ist die Nachricht gedrungen:

»Gott hat Israel gerettet!«

4Jubelt dem Herrn zu, ihr Menschen auf der Erde!

Preist ihn mit Liedern, singt und jubelt laut vor Freude!

5Lasst für ihn die Saiten der Harfe erklingen

und erfreut den Herrn mit eurem Gesang!

6Trompeten und Hörner sollen für Gott,

euren König, erschallen!

7Das Meer mit allem, was in ihm lebt,

soll zu seiner Ehre brausen und tosen!

Die ganze Welt soll in Jubel ausbrechen!

8Ihr Flüsse, klatscht in die Hände;

ihr Berge, preist unseren Herrn,

9denn er kommt, um die Welt zu richten.

Sein Urteil über die Völker ist unbestechlich und gerecht.