Masalimo 98 – Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero CCL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 98:1-9

Salimo 98

Salimo.

1Imbirani Yehova nyimbo yatsopano,

pakuti Iyeyo wachita zinthu zodabwitsa;

dzanja lake lamanja ndi mkono wake woyera

zamuchitira chipulumutso.

2Yehova waonetsa chipulumutso chake

ndipo waulula chilungamo chake kwa anthu a mitundu ina.

3Iye wakumbukira chikondi chake

ndi kukhulupirika kwake pa Aisraeli;

malekezero onse a dziko lapansi aona

chipulumutso cha Mulungu wathu.

4Fuwulani mwachimwemwe kwa Yehova, dziko lonse lapansi,

muyimbireni nyimbo mofuwula ndi mokondwera.

5Imbirani Yehova nyimbo ndi zeze,

ndi zeze ndi mawu a kuyimba,

6ndi malipenga ndi kuliza kwa nyanga ya nkhosa yayimuna

fuwulani mwachimwemwe pamaso pa Yehova Mfumu.

7Nyanja ikokome pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo,

dziko lonse ndi onse amene amakhala mʼmenemo.

8Mitsinje iwombe mʼmanja mwawo,

mapiri ayimbe pamodzi mwachimwemwe;

9izo ziyimbe pamaso pa Yehova,

pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi.

Adzaweruza dziko lonse mwachilungamo,

ndi mitundu ya anthu mosakondera.