Masalimo 97 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 97:1-12

Salimo 97

1Yehova akulamulira, dziko lapansi lisangalale;

magombe akutali akondwere.

2Mitambo ndi mdima waukulu zamuzungulira;

chilungamo ndi kuweruza molungama ndiwo maziko a mpando wake waufumu.

3Moto umapita patsogolo pake

ndi kunyeketsa amaliwongo kumbali zonse.

4Zingʼaningʼani zake zimawalitsa dziko lonse;

dziko lapansi limaona ndipo limanjenjemera.

5Mapiri amasungunuka ngati phula pamaso pa Yehova,

pamaso pa Ambuye a dziko lonse lapansi.

6Mayiko akumwamba amalengeza za chilungamo chake,

ndipo mitundu yonse ya anthu imaona ulemerero wake.

7Onse amene amalambira mafano osema amachititsidwa manyazi,

iwo amene amanyadira mafano;

mulambireni, inu milungu yonse!

8Ziyoni akumva ndipo akukondwera,

midzi ya Yuda ikusangalala

chifukwa cha maweruzo anu Yehova.

9Pakuti Inu Yehova ndi Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi;

ndinu wokwezeka kupambana milungu yonse.

10Iwo amene amakonda Yehova adane ndi zoyipa

pakuti Iye amayangʼanira miyoyo ya amene amamukhulupirira

ndipo amawapulumutsa mʼdzanja la anthu oyipa

11Kuwala kumafika pa anthu olungama,

ndi chimwemwe kwa olungama mtima.

12Kondwerani mwa Yehova Inu olungama

ndipo tamandani dzina lake loyera.

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Salmo 97:1-12

Salmo 97

1¡El Señor es rey!

¡Regocíjese la tierra!

¡Alégrense las costas más remotas!

2Oscuros nubarrones lo rodean;

la rectitud y la justicia son la base de su trono.

3El fuego va delante de él

y consume a los adversarios que lo rodean.

4Sus relámpagos iluminan el mundo;

al verlos, la tierra se estremece.

5Ante el Señor, dueño de toda la tierra,

las montañas se derriten como cera.

6Los cielos proclaman su justicia,

y todos los pueblos contemplan su gloria.

7Sean avergonzados todos los idólatras,

los que se jactan de sus ídolos inútiles.

¡Póstrense ante él todos los dioses!

8Señor, a causa de tus juicios

Sión escucha esto y se alegra,

y las ciudades de Judá se regocijan.

9Porque tú eres el Señor Altísimo,

por encima de toda la tierra.

¡Tú estás muy por encima de todos los dioses!

10El Señor ama97:10 El Señor ama (lectura probable); Los que aman al Señor (TM). a los que odian97:10 a los que odian (Siríaca y algunos mss. hebreos); vosotros odiáis (TM). el mal;

él protege la vida de sus fieles,

y los libra de manos de los impíos.

11La luz se esparce sobre los justos,

y la alegría sobre los rectos de corazón.

12Alegraos en el Señor, vosotros los justos,

y alabad su santo nombre.