Salimo 96
1Imbirani Yehova nyimbo yatsopano;
Imbirani Yehova dziko lonse lapansi.
2Imbirani Yehova, tamandani dzina lake;
lalikirani chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.
3Lengezani ulemerero wake pakati pa mayiko,
ntchito zake zodabwitsa pakati pa mitundu yonse ya anthu.
4Pakuti wamkulu ndi Yehova ndipo ndi woyenera kwambiri kumutamanda;
ayenera kuopedwa kupambana milungu yonse.
5Pakuti milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi mafano,
koma Yehova analenga mayiko akumwamba.
6Ulemu ndi ufumu zili pamaso pake,
mphamvu ndi ulemerero zili mʼmalo ake opatulika.
7Perekani kwa Yehova, inu mabanja a anthu a mitundu ina,
perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
8Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake;
bweretsani chopereka ndipo mulowe mʼmabwalo ake.
9Lambirani Yehova mu ulemerero wa chiyero chake;
njenjemerani pamaso pake, dziko lonse lapansi.
10Nenani pakati pa mitundu ya anthu, “Yehova akulamulira.”
Dziko lonse lakhazikika molimba, silingasunthidwe;
Iye adzaweruza mitundu ya anthu molungama.
11Mayiko akumwamba asangalale, dziko lapansi likondwere;
nyanja ikokome, ndi zonse zili mʼmenemo;
12minda ikondwere pamodzi ndi chilichonse chili mʼmenemo.
Pamenepo mitengo yonse ya mʼnkhalango idzayimba ndi chimwemwe;
13idzayimba pamaso pa Yehova,
pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi;
adzaweruza dziko lonse mwachilungamo
ndi mitundu ya anthu onse mʼchoonadi.
Salmo 96
(1 Cr 16.23-33)
1Cantem ao Senhor um cântico novo;
cantem-lhe em toda a Terra!
2Cantem ao Senhor;
deem louvores à força do seu nome!
Anunciem a sua salvação dia após dia!
3Deem a conhecer entre todos os povos da Terra,
como é excelsa a sua glória!
Contem a todas as gentes as suas maravilhas!
4Porque o Senhor é grande
e digno de todo o louvor;
é muitíssimo superior a todos os chamados deuses.
5Esses pretensos deuses são apenas ídolos,
mas o Senhor, esse é o Criador dos céus.
6À sua volta só há glória e majestade;
a força e a beleza encontram-se no seu santuário.
7Ó povos de todas a nações, louvem o Senhor;
reconheçam a sua grande força e glória!
8Sim, deem ao Senhor a glória que é devida ao seu nome!
Tragam ofertas e venham aos seus átrios!
9Adorem o Senhor revestido de santidade!
Que a Terra inteira trema na sua presença!
10Digam às nações:
“O Senhor governa o mundo,
o mundo permanece inabalável!
Ele julgará os povos com perfeita justiça.”
11Alegrem-se os céus, regozije-se a Terra!
Que os vastos mares exultem!
12Que tudo o que os campos produzem
seja um motivo para se louvar o Senhor,
pois é uma prova do seu poder.
Que as árvores das florestas exaltem o Criador,
13porque o Senhor virá.
Ele há de vir para julgar a Terra com justiça
e os povos com a sua verdade.