Masalimo 96 – CCL & OL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 96:1-13

Salimo 96

1Imbirani Yehova nyimbo yatsopano;

Imbirani Yehova dziko lonse lapansi.

2Imbirani Yehova, tamandani dzina lake;

lalikirani chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.

3Lengezani ulemerero wake pakati pa mayiko,

ntchito zake zodabwitsa pakati pa mitundu yonse ya anthu.

4Pakuti wamkulu ndi Yehova ndipo ndi woyenera kwambiri kumutamanda;

ayenera kuopedwa kupambana milungu yonse.

5Pakuti milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi mafano,

koma Yehova analenga mayiko akumwamba.

6Ulemu ndi ufumu zili pamaso pake,

mphamvu ndi ulemerero zili mʼmalo ake opatulika.

7Perekani kwa Yehova, inu mabanja a anthu a mitundu ina,

perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.

8Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake;

bweretsani chopereka ndipo mulowe mʼmabwalo ake.

9Lambirani Yehova mu ulemerero wa chiyero chake;

njenjemerani pamaso pake, dziko lonse lapansi.

10Nenani pakati pa mitundu ya anthu, “Yehova akulamulira.”

Dziko lonse lakhazikika molimba, silingasunthidwe;

Iye adzaweruza mitundu ya anthu molungama.

11Mayiko akumwamba asangalale, dziko lapansi likondwere;

nyanja ikokome, ndi zonse zili mʼmenemo;

12minda ikondwere pamodzi ndi chilichonse chili mʼmenemo.

Pamenepo mitengo yonse ya mʼnkhalango idzayimba ndi chimwemwe;

13idzayimba pamaso pa Yehova,

pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi;

adzaweruza dziko lonse mwachilungamo

ndi mitundu ya anthu onse mʼchoonadi.

O Livro

Salmos 96:1-13

Salmo 96

(1 Cr 16.23-33)

1Cantem ao Senhor um cântico novo;

cantem-lhe em toda a Terra!

2Cantem ao Senhor;

deem louvores à força do seu nome!

Anunciem a sua salvação dia após dia!

3Deem a conhecer entre todos os povos da Terra,

como é excelsa a sua glória!

Contem a todas as gentes as suas maravilhas!

4Porque o Senhor é grande

e digno de todo o louvor;

é muitíssimo superior a todos os chamados deuses.

5Esses pretensos deuses são apenas ídolos,

mas o Senhor, esse é o Criador dos céus.

6À sua volta só há glória e majestade;

a força e a beleza encontram-se no seu santuário.

7Ó povos de todas a nações, louvem o Senhor;

reconheçam a sua grande força e glória!

8Sim, deem ao Senhor a glória que é devida ao seu nome!

Tragam ofertas e venham aos seus átrios!

9Adorem o Senhor revestido de santidade!

Que a Terra inteira trema na sua presença!

10Digam às nações:

“O Senhor governa o mundo,

o mundo permanece inabalável!

Ele julgará os povos com perfeita justiça.”

11Alegrem-se os céus, regozije-se a Terra!

Que os vastos mares exultem!

12Que tudo o que os campos produzem

seja um motivo para se louvar o Senhor,

pois é uma prova do seu poder.

Que as árvores das florestas exaltem o Criador,

13porque o Senhor virá.

Ele há de vir para julgar a Terra com justiça

e os povos com a sua verdade.