Masalimo 96 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 96:1-13

Salimo 96

1Imbirani Yehova nyimbo yatsopano;

Imbirani Yehova dziko lonse lapansi.

2Imbirani Yehova, tamandani dzina lake;

lalikirani chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.

3Lengezani ulemerero wake pakati pa mayiko,

ntchito zake zodabwitsa pakati pa mitundu yonse ya anthu.

4Pakuti wamkulu ndi Yehova ndipo ndi woyenera kwambiri kumutamanda;

ayenera kuopedwa kupambana milungu yonse.

5Pakuti milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi mafano,

koma Yehova analenga mayiko akumwamba.

6Ulemu ndi ufumu zili pamaso pake,

mphamvu ndi ulemerero zili mʼmalo ake opatulika.

7Perekani kwa Yehova, inu mabanja a anthu a mitundu ina,

perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.

8Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake;

bweretsani chopereka ndipo mulowe mʼmabwalo ake.

9Lambirani Yehova mu ulemerero wa chiyero chake;

njenjemerani pamaso pake, dziko lonse lapansi.

10Nenani pakati pa mitundu ya anthu, “Yehova akulamulira.”

Dziko lonse lakhazikika molimba, silingasunthidwe;

Iye adzaweruza mitundu ya anthu molungama.

11Mayiko akumwamba asangalale, dziko lapansi likondwere;

nyanja ikokome, ndi zonse zili mʼmenemo;

12minda ikondwere pamodzi ndi chilichonse chili mʼmenemo.

Pamenepo mitengo yonse ya mʼnkhalango idzayimba ndi chimwemwe;

13idzayimba pamaso pa Yehova,

pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi;

adzaweruza dziko lonse mwachilungamo

ndi mitundu ya anthu onse mʼchoonadi.

Hoffnung für Alle

Psalm 96:1-13

Alle sollen es wissen: Der Herr allein ist König!

(1. Chronik 16,23‒33)

1Singt dem Herrn ein neues Lied,

singt dem Herrn, alle Bewohner der Erde!

2Singt dem Herrn und preist seinen Namen!

Verkündet jeden Tag: »Gott ist ein Gott, der rettet!«

3Erzählt den Völkern von seiner Hoheit!

Macht allen Menschen seine Wunder bekannt!

4Denn groß ist der Herr! Jeder soll ihn rühmen!

Von allen Göttern soll man ihn allein fürchten.

5Die Götter der Völker sind machtlose Figuren,

der Herr aber hat den Himmel geschaffen!

6Majestät und Pracht gehen von ihm aus,

seine Stärke und Schönheit erfüllen den Tempel.

7Gebt dem Herrn, was ihm gebührt;

ihr Völker, erkennt seine Ehre und Macht!

8Preist seinen großen Namen, kommt zu seinem Heiligtum,

und bringt ihm eure Opfer dar!

9Werft euch vor ihm nieder in seiner herrlichen Pracht!96,9 Oder: Werft euch vor ihm nieder in heiligem Schmuck!

Die ganze Welt soll vor ihm erzittern!

10Sagt den Völkern: »Der Herr ist König!«

Er hat die Fundamente der Erde gelegt, niemals gerät sie ins Wanken.

Allen Völkern wird er ein gerechter Richter sein!

11Der Himmel soll sich freuen und die Erde in Jubel ausbrechen!

Das Meer mit allem, was in ihm lebt,

soll zu seiner Ehre brausen und tosen!

12Der Acker sei fröhlich mit allem, was auf ihm wächst!

Auch die Bäume im Wald sollen jubeln,

13wenn der Herr kommt.

Ja, er kommt, um die Welt zu richten.

Sein Urteil über die Völker ist unbestechlich und gerecht.