Masalimo 95 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 95:1-11

Salimo 95

1Bwerani, tiyeni timuyimbire Yehova mwachimwemwe,

tiyeni tifuwule kwa Thanthwe la chipulumutso chathu

2Tiyeni tibwere pamaso pake ndi chiyamiko

ndipo mupembedzeni Iyeyo ndi zida zoyimbira ndi nyimbo.

3Pakuti Yehova ndi Mulungu wamkulu,

mfumu yayikulu pamwamba pa milungu yonse.

4Mʼmanja mwake muli maziko ozama a dziko lapansi,

ndipo msonga za mapiri ndi zake.

5Nyanja ndi yake, pakuti anayilenga ndi Iye,

ndipo manja ake anawumba mtunda wowuma.

6Bwerani, tiyeni tiwerame pomulambira,

tiyeni tigwade pamaso pa Yehova Mlengi wathu;

7pakuti Iye ndiye Mulungu wathu

ndipo ife ndife anthu a pabusa pake,

ndi nkhosa za mʼdzanja lake.

Lero ngati inu mumva mawu ake,

8musawumitse mitima yanu monga momwe munachitira pa Meriba,

monga munachitira tsiku lija pa Masa mʼchipululu.

9Kumene makolo anu anandiyesa ndi kundiputa,

ngakhale anaona zimene Ine ndinazichita.

10Kwa zaka makumi anayi ndinali wokwiya ndi mʼbado umenewo;

ndipo ndinati, “Iwo ndi anthu amene mitima yawo imasochera

ndipo sanadziwe njira zanga.”

11Choncho ndili chikwiyire, ndinalumbira kuti,

“Iwowa sadzalowa ku malo anga a mpumulo.”

New Russian Translation

Псалтирь 95:1-13

Псалом 95

(1 Пар. 16:23-33)

1Воспойте Господу новую песню;

вся земля, воспой Господу.

2Воспойте Господу, благословляйте Его имя,

говорите о Его спасении каждый день.

3Возвещайте славу Его среди народов,

чудеса Его – среди всех людей,

4потому что велик Господь и достоин беспредельной хвалы;

Он внушает страх более всех богов.

5Все боги народов – идолы,

а Господь сотворил небеса.

6Слава и величие перед Ним,

сила и великолепие в Его святилище.

7Воздайте Господу, народы,

воздайте Ему славу и силу.

8Воздайте Господу славу, присущую Его имени.

Несите дар и идите во дворы Его.

9Прославьте Господа в великолепии Его святости95:9 Или: «в святом облачении прославьте Господа»; или: «прославьте Господа в Его великолепном святилище»..

Трепещи перед Ним, вся земля!

10Скажите среди народов: «Господь правит!»

Прочно мир утвержден и не поколеблется;

Господь будет судить народы справедливо.

11Да возвеселятся небеса и возликует земля;

да восшумит море и все, что в нем.

12Да возрадуется поле и все, что на нем,

и да возликуют все деревья лесные

13перед Господом, потому что идет,

идет Он судить землю.

Он будет судить вселенную справедливо

и народы – по Своей истине.