Masalimo 95 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 95:1-11

Salimo 95

1Bwerani, tiyeni timuyimbire Yehova mwachimwemwe,

tiyeni tifuwule kwa Thanthwe la chipulumutso chathu

2Tiyeni tibwere pamaso pake ndi chiyamiko

ndipo mupembedzeni Iyeyo ndi zida zoyimbira ndi nyimbo.

3Pakuti Yehova ndi Mulungu wamkulu,

mfumu yayikulu pamwamba pa milungu yonse.

4Mʼmanja mwake muli maziko ozama a dziko lapansi,

ndipo msonga za mapiri ndi zake.

5Nyanja ndi yake, pakuti anayilenga ndi Iye,

ndipo manja ake anawumba mtunda wowuma.

6Bwerani, tiyeni tiwerame pomulambira,

tiyeni tigwade pamaso pa Yehova Mlengi wathu;

7pakuti Iye ndiye Mulungu wathu

ndipo ife ndife anthu a pabusa pake,

ndi nkhosa za mʼdzanja lake.

Lero ngati inu mumva mawu ake,

8musawumitse mitima yanu monga momwe munachitira pa Meriba,

monga munachitira tsiku lija pa Masa mʼchipululu.

9Kumene makolo anu anandiyesa ndi kundiputa,

ngakhale anaona zimene Ine ndinazichita.

10Kwa zaka makumi anayi ndinali wokwiya ndi mʼbado umenewo;

ndipo ndinati, “Iwo ndi anthu amene mitima yawo imasochera

ndipo sanadziwe njira zanga.”

11Choncho ndili chikwiyire, ndinalumbira kuti,

“Iwowa sadzalowa ku malo anga a mpumulo.”

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

詩篇 95:1-11

第 95 篇

讚美上帝之歌

1來吧,讓我們向耶和華歌唱,

向拯救我們的磐石歡呼。

2讓我們懷著感恩的心來到祂面前,

向祂高唱讚美詩。

3因為耶和華是偉大的上帝,

是眾神明之上的大君王。

4祂掌管地的深處,

祂擁有山的高峰。

5海洋屬於祂,是祂創造的,

陸地也是祂造的。

6來吧,讓我們俯伏敬拜,

在創造我們的耶和華面前跪下。

7因為祂是我們的上帝,

我們是祂照管的子民,

是祂牧放的羊群。

你們今日若聽見祂的聲音,

8不可像你們祖先在米利巴

在曠野的瑪撒那樣心裡頑固。

9耶和華說:「雖然他們見過我的作為,

卻仍然試探我。

10所以,我憎惡他們四十年之久,

我說,『他們偏離正路,不遵行我的命令。』

11因此我在怒中起誓說,

『他們絕不可進入我的安息!』」