Masalimo 94 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 94:1-23

Salimo 94

1Inu Yehova, ndinu Mulungu wobwezera chilango,

Inu Mulungu amene mumabwezera chilango, wonetsani kuwala kwanu.

2Nyamukani, Inu woweruza wa dziko lapansi;

bwezerani kwa odzikuza zowayenera.

3Kodi mpaka liti anthu oyipa Inu Yehova,

mpaka liti anthu oyipa adzalumpha ndi chimwemwe?

4Amakhuthula mawu onyada;

onse ochita zoyipa ndi odzaza ndi kudzikuza.

5Amaphwanya anthu anu, Inu Yehova;

amapondereza cholowa chanu.

6Amaphanso amayi a masiye ndi alendo okhala nawo mʼdziko;

amapha ana amasiye.

7Iwo amati, “Yehova sakuona;

Mulungu wa Yakobo salabadirako.”

8Samalani, inu anthu opanda nzeru pakati pa anthu;

zitsiru inu, kodi mudzakhala liti anzeru?

9Kodi Iye amene anapanga khutu sangathe kumva?

Kodi Iye amene anapanga diso sangathe kuona?

10Kodi Iye amene amalangiza mitundu ya anthu sangathenso kulanga?

Kodi Iye amene amaphunzitsa munthu angasowe nzeru?

11Yehova amadziwa maganizo a munthu;

Iye amadziwa kuti maganizowo ndi achabechabe.

12Wodala munthu amene Inu Yehova mumamulangiza,

munthu amene mumamuphunzitsa kuchokera mulamulo lanu;

13mumamupumitsa pa nthawi ya mavuto,

mpaka woyipa atakumbiridwa dzenje.

14Pakuti Yehova sadzawakana anthu ake;

Iye sadzasiya cholowa chake.

15Chiweruzo chidzakhazikikanso pa chilungamo,

ndipo onse olungama mtima adzachitsata.

16Ndani adzadzuka chifukwa cha ine kulimbana ndi anthu oyipa?

Ndani adzayimirira mʼmalo mwanga kulimbana ndi anthu ochita zoyipa?

17Yehova akanapanda kundithandiza,

bwenzi nditakakhala msanga ku malo achete a imfa.

18Ndikanena kuti, “Phazi langa likuterereka,”

chikondi chanu, Inu Yehova, chimandichirikiza.

19Pamene nkhawa inakula mʼkati mwanga,

chitonthozo chanu chinabweretsa chimwemwe mʼmoyo mwanga.

20Kodi mpando waufumu woyipa ungathe kugwirizana nanu

umene umabweretsa masautso chifukwa cha malamulo ake?

21Iwo amasonkhana pamodzi kulimbana ndi wolungama

ndi kugamula kuti wosalakwa aphedwe.

22Koma Yehova wakhala linga langa,

ndipo Mulungu ndiye thanthwe limene ndimathawirako.

23Iye adzawabwezera chifukwa cha machimo awo

ndi kuwawononga chifukwa cha kuyipa kwawo;

Yehova Mulungu wathu adzawawononga.

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Salmo 94:1-23

Salmo 94

1Señor, Dios de las venganzas;

Dios de las venganzas, ¡manifiéstate!94:1 ¡manifiéstate! Lit. resplandece.

2Levántate, Juez de la tierra,

y dales su merecido a los soberbios.

3¿Hasta cuándo, Señor, hasta cuándo

habrán de ufanarse los impíos?

4Todos esos malhechores son unos fanfarrones;

a borbotones escupen su arrogancia.

5A tu pueblo, Señor, lo pisotean;

¡oprimen a tu herencia!

6Matan a las viudas y a los extranjeros;

a los huérfanos los asesinan.

7Y hasta dicen: «El Señor no ve;

el Dios de Jacob no se da cuenta».

8Entended esto, gente necia;

¿cuándo, insensatos, lo vais a comprender?

9¿Acaso no oirá el que nos puso las orejas,

ni podrá ver el que nos formó los ojos?

10¿Y no habrá de castigar el que corrige a las naciones

e instruye en el saber a todo el mundo?

11El Señor conoce los pensamientos humanos,

y sabe que son absurdos.

12Dichoso aquel a quien tú, Señor, corriges;

aquel a quien instruyes en tu ley,

13para que enfrente tranquilo los días de aflicción

mientras al impío se le cava una fosa.

14El Señor no rechazará a su pueblo;

no dejará a su herencia en el abandono.

15El juicio volverá a basarse en la justicia,

y todos los rectos de corazón lo seguirán.

16¿Quién se levantó a defenderme de los impíos?

¿Quién se puso de mi parte contra los malhechores?

17Si el Señor no me hubiera brindado su ayuda,

muy pronto me habría quedado en mortal silencio.

18Apenas decía: «Mis pies resbalan»,

cuando ya tu amor, Señor, venía en mi ayuda.

19Cuando en mí la angustia iba en aumento,

tu consuelo llenaba mi alma de alegría.

20¿Podrías ser amigo de reyes corruptos94:20 de reyes corruptos. Lit. del trono corrupto.

que por decreto fraguan la maldad,

21que conspiran contra la gente honrada

y condenan a muerte al inocente?

22Pero el Señor es mi protector,

es mi Dios y la roca en que me refugio.

23Él les hará pagar por sus pecados

y los destruirá por su maldad;

¡el Señor nuestro Dios los destruirá!