Masalimo 93 – Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero CCL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 93:1-5

Salimo 93

1Yehova akulamulira, wavala ulemerero;

Yehova wavala ulemerero ndipo wadzimangirira mphamvu,

dziko lonse lakhazikika kolimba; silingasunthidwe.

2Mpando wanu waufumu unakhazikika kalekale;

Inu ndinu wamuyaya.

3Nyanja zakweza Inu Yehova,

nyanja zakweza mawu ake;

nyanja zakweza mafunde ake ochita mkokomo.

4Yehova ndi wamphamvu kupambana mkokomo wa madzi ambiri,

ndi wamphamvu kupambana mafunde a nyanja,

Yehova mmwamba ndi wamphamvu.

5Malamulo anu Yehova ndi osasinthika;

chiyero chimakongoletsa nyumba yanu

mpaka muyaya.