Masalimo 92 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 92:1-15

Salimo 92

Salimo. Nyimbo ya pa tsiku la Sabata.

1Nʼkwabwino kutamanda Yehova

ndi kuyimbira nyimbo dzina lanu, Inu Wammwambamwamba,

2Kulengeza chikondi chanu mmawa,

ndi kukhulupirika kwanu nthawi ya usiku,

3kuyimbira nyimbo choyimbira cha zingwe khumi

ndi mayimbidwe abwino a zeze.

4Pakuti Inu mumandisangalatsa ndi ntchito zanu, Inu Yehova;

Ine ndikuyimba mwachimwemwe pa ntchito ya manja anu.

5Ndi yayikuludi ntchito yanu Yehova,

maganizo anu ndi ozamadi!

6Munthu wopanda nzeru sadziwa,

zitsiru sizizindikira,

7kuti ngakhale anthu oyipa aphuka ngati udzu

ndipo anthu onse ochita zoyipa apindula,

adzawonongedwa kwamuyaya.

8Koma Inu Yehova, ndinu wokwezedwa kwamuyaya.

9Zoonadi adani anu Yehova,

zoonadi adani anu adzawonongeka;

onse ochita zoyipa adzabalalitsidwa.

10Inu mwakweza nyanga yanga ngati nyanga ya njati;

mafuta abwino akhuthulidwa pamutu wanga.

11Maso anga aona kugonjetsedwa kwa olimbana nane,

makutu anga amva za kugwa kwa amaliwongo anga oyipa.

12Anthu olungama adzaphuka ngati mtengo wa mgwalangwa,

adzakula ngati mkungudza wa ku Lebanoni;

13odzalidwa mʼnyumba ya Yehova,

adzakula bwino mʼmabwalo a Mulungu wathu.

14Iwo adzaberekabe zipatso mu ukalamba wawo,

adzakhala anthete ndi obiriwira,

15kulengeza kuti, “Yehova ndi wolungama;

Iye ndiye Thanthwe langa, ndipo mwa Iye mulibe choyipa.”

Hoffnung für Alle

Psalm 92:1-16

Wie gut ist es, dir, Herr, zu danken!

1Ein Lied zum Sabbat.

2Wie gut ist es, dir, Herr, zu danken

und deinen Namen, du höchster Gott, zu besingen,

3schon früh am Morgen deine Gnade zu loben

und noch in der Nacht deine Treue zu preisen,

4zur Musik der zehnsaitigen Harfe

und zum schönen Spiel auf der Laute!

5Herr, was du tust, macht mich froh,

und ich juble über deine großen Taten.

6Wie machtvoll sind deine Werke,

und wie tief sind deine Gedanken!

7Nur ein unvernünftiger Mensch sieht das nicht ein,

nur ein Narr kann nichts damit anfangen.

8Mag auch ein Gottloser Erfolg haben,

mag er emporwachsen und blühen –

er wird doch für immer vernichtet werden.

9Du aber, Herr,

bist in Ewigkeit erhaben!

10Eines ist sicher: Deine Feinde werden umkommen;

die Menschen, die Unrecht tun, werden in alle Winde zerstreut!

11Doch mir gibst du Kraft, wie ein wilder Stier sie hat;

du schenkst mir Freude und neuen Mut.92,11 Wörtlich: Du erhöhst mein Horn wie das eines Büffels, mit frischem Öl hast du mich überschüttet. – Das Horn steht sinnbildlich für Stärke und Kraft. Vgl. außerdem »salben/Salbung« in den Sacherklärungen.

12Ich werde noch miterleben, wie meine Feinde stürzen;

ich werde hören, wie sie um Gnade wimmern.

13Wer Gott liebt, gleicht einer immergrünen Palme,

er wird mächtig wie eine Zeder auf dem Libanongebirge.

14Er ist wie ein Baum, der im Vorhof des Tempels gepflanzt wurde

und dort wachsen und gedeihen kann.

15Noch im hohen Alter wird er Frucht tragen,

immer ist er kraftvoll und frisch.

16Sein Leben ist ein Beweis dafür, dass der Herr für Recht sorgt.

Bei Gott bin ich sicher und geborgen;

was er tut, ist vollkommen und gerecht!