Masalimo 92 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 92:1-15

Salimo 92

Salimo. Nyimbo ya pa tsiku la Sabata.

1Nʼkwabwino kutamanda Yehova

ndi kuyimbira nyimbo dzina lanu, Inu Wammwambamwamba,

2Kulengeza chikondi chanu mmawa,

ndi kukhulupirika kwanu nthawi ya usiku,

3kuyimbira nyimbo choyimbira cha zingwe khumi

ndi mayimbidwe abwino a zeze.

4Pakuti Inu mumandisangalatsa ndi ntchito zanu, Inu Yehova;

Ine ndikuyimba mwachimwemwe pa ntchito ya manja anu.

5Ndi yayikuludi ntchito yanu Yehova,

maganizo anu ndi ozamadi!

6Munthu wopanda nzeru sadziwa,

zitsiru sizizindikira,

7kuti ngakhale anthu oyipa aphuka ngati udzu

ndipo anthu onse ochita zoyipa apindula,

adzawonongedwa kwamuyaya.

8Koma Inu Yehova, ndinu wokwezedwa kwamuyaya.

9Zoonadi adani anu Yehova,

zoonadi adani anu adzawonongeka;

onse ochita zoyipa adzabalalitsidwa.

10Inu mwakweza nyanga yanga ngati nyanga ya njati;

mafuta abwino akhuthulidwa pamutu wanga.

11Maso anga aona kugonjetsedwa kwa olimbana nane,

makutu anga amva za kugwa kwa amaliwongo anga oyipa.

12Anthu olungama adzaphuka ngati mtengo wa mgwalangwa,

adzakula ngati mkungudza wa ku Lebanoni;

13odzalidwa mʼnyumba ya Yehova,

adzakula bwino mʼmabwalo a Mulungu wathu.

14Iwo adzaberekabe zipatso mu ukalamba wawo,

adzakhala anthete ndi obiriwira,

15kulengeza kuti, “Yehova ndi wolungama;

Iye ndiye Thanthwe langa, ndipo mwa Iye mulibe choyipa.”

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Salmo 92:1-15

Salmo 92

Salmo para cantarse en sábado.

1¡Cuán bueno, Señor, es darte gracias

y entonar, oh Altísimo, salmos a tu nombre;

2proclamar tu gran amor por la mañana,

y tu fidelidad por la noche,

3al son del decacordio y de la lira;

al son del arpa y del salterio!

4Tú, Señor, me llenas de alegría con tus maravillas;

por eso alabaré jubiloso las obras de tus manos.

5Oh Señor, ¡cuán imponentes son tus obras,

y cuán profundos tus pensamientos!

6Los insensatos no lo saben,

los necios no lo entienden:

7aunque broten como hierba los impíos,

y florezcan todos los malhechores,

para siempre serán destruidos.

8Solo tú, Señor, serás exaltado para siempre.

9Ciertamente tus enemigos, Señor,

ciertamente tus enemigos perecerán;

¡dispersados por todas partes

serán todos los malhechores!

10Me has dado las fuerzas de un toro;

me has ungido con el mejor perfume.

11Me has hecho ver la caída de mis adversarios

y oír la derrota de mis malvados enemigos.

12Como palmeras florecen los justos;

como cedros del Líbano crecen.

13Plantados en la casa del Señor,

florecen en los atrios de nuestro Dios.

14Aun en su vejez, darán fruto;

siempre estarán vigorosos y lozanos,

15para proclamar: «El Señor es justo;

él es mi Roca, y en él no hay injusticia».