Masalimo 92 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 92:1-15

Salimo 92

Salimo. Nyimbo ya pa tsiku la Sabata.

1Nʼkwabwino kutamanda Yehova

ndi kuyimbira nyimbo dzina lanu, Inu Wammwambamwamba,

2Kulengeza chikondi chanu mmawa,

ndi kukhulupirika kwanu nthawi ya usiku,

3kuyimbira nyimbo choyimbira cha zingwe khumi

ndi mayimbidwe abwino a zeze.

4Pakuti Inu mumandisangalatsa ndi ntchito zanu, Inu Yehova;

Ine ndikuyimba mwachimwemwe pa ntchito ya manja anu.

5Ndi yayikuludi ntchito yanu Yehova,

maganizo anu ndi ozamadi!

6Munthu wopanda nzeru sadziwa,

zitsiru sizizindikira,

7kuti ngakhale anthu oyipa aphuka ngati udzu

ndipo anthu onse ochita zoyipa apindula,

adzawonongedwa kwamuyaya.

8Koma Inu Yehova, ndinu wokwezedwa kwamuyaya.

9Zoonadi adani anu Yehova,

zoonadi adani anu adzawonongeka;

onse ochita zoyipa adzabalalitsidwa.

10Inu mwakweza nyanga yanga ngati nyanga ya njati;

mafuta abwino akhuthulidwa pamutu wanga.

11Maso anga aona kugonjetsedwa kwa olimbana nane,

makutu anga amva za kugwa kwa amaliwongo anga oyipa.

12Anthu olungama adzaphuka ngati mtengo wa mgwalangwa,

adzakula ngati mkungudza wa ku Lebanoni;

13odzalidwa mʼnyumba ya Yehova,

adzakula bwino mʼmabwalo a Mulungu wathu.

14Iwo adzaberekabe zipatso mu ukalamba wawo,

adzakhala anthete ndi obiriwira,

15kulengeza kuti, “Yehova ndi wolungama;

Iye ndiye Thanthwe langa, ndipo mwa Iye mulibe choyipa.”

Bibelen på hverdagsdansk

Salmernes Bog 92:1-16

Lovsang i Guds hus

1En sang til sabbatten.

2Det er godt at takke dig, Herre,

at lovsynge den almægtige Gud,

3at mindes din nåde hver morgen,

at takke dig for din trofasthed hver aften,

4at prise dig til harpeklang,

til toner fra lut og lyre.

5Jeg fryder mig over dine undere,

glæder mig over dine gerninger.

6Du gør utrolige ting, Herre,

dine tanker er ufattelige.

7Der er noget, som tåber ikke kan begribe,

en sandhed, de uvidende ikke kan forstå:

8Selv om de gudløse ser ud til at klare sig godt,

bliver de til sidst udslettet for evigt.

9Men du, Herre, har magten i al evighed,

10du nedkæmper alle dine fjender.

De gudløse vil gå til grunde,

de onde vil blive gjort til intet.

11Du har givet mig styrke som vildoksen,

din støtte giver mig glæde og fremgang.

12Jeg har set mine fjender falde,

hørt om mine angriberes nederlag.

13De retskafne trives som mægtige palmer,

vokser sig store som Libanons cedre.

14De er plantet i Herrens Hus,

dér trives de under hans pleje.

15Selv i alderdommen bærer de frugt,

de bevarer deres friskhed og livskraft.

16De vidner om Herrens beskyttelse,

han er helt igennem god og retfærdig.