Masalimo 91 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 91:1-16

Salimo 91

1Iye amene amakhala mu mthunzi wa Wammwambamwamba

adzapuma mu mthunzi wa Wamphamvuzonse.

2Ndidzanena za Yehova, “Iye ndiye pothawira panga ndi linga langa,

Mulungu wanga amene ndimadalira.”

3Ndithu, Iye adzakupulumutsa ku msampha wa mlenje

ndi ku mliri woopsa;

4Adzakuphimba ndi nthenga zake,

ndipo udzapeza malo othawira mʼmapikomo;

kukhulupirika kwake kudzakhala chishango chako ndi lihawo.

5Sudzachita mantha ndi zoopsa za usiku,

kapena muvi wowuluka masana,

6kapena mliri umene umayenda mu mdima,

kapena zowononga za pa nthawi ya masana.

7Anthu 1,000 atha kufa pambali pako,

anthu 10,000 kudzanja lako lamanja,

koma zoopsazo sizidzafika pafupi ndi iwe.

8Udzapenya ndi maso ako

ndipo udzaona mmene anthu oyipa amalangidwira.

9Pakuti wasankha Wammwambamwamba kukhala malo ako okhalamo;

wavomera Yehova kukhala kothawira kwako.

10Choncho palibe choyipa chimene chidzakugwera,

zoopsa sizidzafika pafupi ndi tenti yako.

11Pakuti adzalamulira angelo ake za iwe,

kuti akutchinjirize mosamala pa njira zako zonse;

12ndipo adzakunyamula ndi manja awo,

kuti phazi lako lisagunde pa mwala.

13Udzapondaponda mkango ndi njoka,

udzapondereza mkango wamphamvu ndiponso chinjoka.

14“Chifukwa iye amandikonda,” akutero Yehova, “Ndidzamulanditsa;

ndidzamuteteza pakuti wavomereza dzina langa.

15Adzandiyitana, ndipo ndidzamuyankha;

ndidzakhala naye pa mavuto,

ndidzamupulumutsa ndi kumulemekeza.

16Ndidzamupatsa moyo wautali

ndi kumupulumutsa.”

New Russian Translation

Псалтирь 91:1-16

Псалом 91

1Псалом. Песнь на празднование субботы.

2Хорошо славить Господа

и воспевать имя Твое, Всевышний,

3возглашать милость Твою утром

и верность Твою вечером,

4играть на десятиструнной лире

и на мелодичной арфе.

5Ведь Ты, Господи, обрадовал меня Своими деяниями;

я ликую о делах Твоих рук.

6Господи, как велики Твои дела,

и как глубоки Твои помышления!

7Глупый человек не знает,

и невежда не понимает их.

8Хотя нечестивые возникают, как трава,

и злодеи процветают,

они исчезнут навеки.

9Ты же, Господи, навеки превознесен!

10Подлинно враги Твои, Господи,

подлинно враги Твои погибнут;

все злодеи будут рассеяны.

11А мой рог91:11 Рог – олицетворение могущества, власти и силы. Ты вознесешь, подобно рогу быка,

и умастишь меня свежим маслом.

12Глаза мои видели поражение врагов моих,

и уши мои слышали падение злодеев, восстающих на меня.

13А праведник цветет, словно пальма,

возвышается, как кедр на Ливане.

14Посаженные в доме Господнем,

они зацветут во дворах храма нашего Бога.

15Они и в старости будут плодовиты,

сочны и свежи,

16чтобы возвещать, что праведен Господь, скала моя,

и нет в Нем неправды.