Masalimo 90 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 90:1-17

BUKU LACHINAYI

Masalimo 90–106

Salimo 90

Pemphero la Mose munthu wa Mulungu.

1Ambuye, mwakhala muli malo athu okhalamo

pa mibado yonse.

2Mapiri asanabadwe,

musanalenge nʼkomwe dziko lapansi ndi dziko lonse,

kuyambira muyaya mpaka muyaya Inu ndinu Mulungu.

3Inu mumabwezera anthu ku fumbi,

mumati, “Bwerera ku fumbi iwe mwana wa munthu.”

4Pakuti zaka 1,000 pamaso panu

zili ngati tsiku limene lapita

kapena ngati kamphindi ka usiku.

5Inu mumasesa anthu mʼtulo ta imfa,

iwo ali ngati udzu watsopano wa mmawa,

6ngakhale kuti mmawa umaphuka watsopano,

pofika madzulo wauma ndi kufota.

7Ife tathedwa ndi mkwiyo wanu;

ndipo taopsezedwa ndi kuyipidwa kwanu.

8Mwayika mphulupulu zathu pamaso panu,

machimo athu obisika poonekera pamaso panu.

9Masiku athu onse amatha ali pansi pa ukali wanu;

timatsiriza zaka zathu ndi kubuwula.

10Kuchuluka kwa masiku athu ndi 70,

kapena 80 ngati tili ndi mphamvu;

komabe zaka zonsezi ndi za mavuto ndi nkhawa,

zimatha mofulumira ndipo ife timawulukira kutali.

11Kodi ndani amadziwa mphamvu ya mkwiyo wanu?

Pakuti ukali wanu ndi waukulu ngati ulemu umene uyenera Inu.

12Tiphunzitseni kuwerenga masiku athu molondola,

kuti tikhale ndi mtima wanzeru.

13Lezani mtima Inu Yehova! Kodi mudzatikwiyira mpaka liti?

Achitireni chifundo atumiki anu.

14Mutikhutitse mmawa ndi chikondi chanu chosatha,

kuti tiyimbe ndi chimwemwe ndi kukhala okondwa masiku athu onse.

15Tisangalatseni masiku ambiri monga masiku amene mwatisautsa,

kwa zaka zambiri monga momwe tinaonera mavuto.

16Ntchito zanu zionetsedwe kwa atumiki anu,

kukongola kwanu kwa ana awo.

17Kukoma mtima kwa Ambuye Mulungu wathu kukhale pa ife;

tikhazikitsireni ntchito ya manja athu;

inde, khazikitsani ntchito ya manja athu.

New International Reader’s Version

Psalm 90:1-17

Book IV

Psalms 90–106

Psalm 90

A prayer of Moses, the man of God.

1Lord, from the very beginning

you have been like a home to us.

2Before you created the whole world and the mountains were made,

from the beginning to the end you are God.

3You turn human beings back to dust.

You say to them, “Return to dust.”

4To you a thousand years

are like a day that has just gone by.

They are like a few hours of the night.

5Yet you sweep people away, and they die.

They are like new grass that grows in the morning.

6In the morning it springs up new,

but by evening it’s all dried up.

7Your anger destroys us.

Your burning anger terrifies us.

8You have put our sins right in front of you.

You have placed our secret sins where you can see them clearly.

9You have been angry with us all of our days.

We groan as we come to the end of our lives.

10We live to be about 70.

Or we may live to be 80, if we stay healthy.

But even our best days are filled with trouble and sorrow.

The years quickly pass, and we are gone.

11If only we knew the power of your anger!

It’s as great as the respect we should have for you.

12Teach us to realize how short our lives are.

Then our hearts will become wise.

13Lord, please stop punishing us!

How long will you keep it up?

Be kind to us.

14Satisfy us with your faithful love every morning.

Then we can sing for joy and be glad all our days.

15Make us glad for as many days as you have made us suffer.

Give us joy for as many years as we’ve had trouble.

16Show us your mighty acts.

Let our children see your glorious power.

17May the Lord our God always be pleased with us.

Lord, make what we do succeed.

Please make what we do succeed.