Masalimo 89 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 89:1-52

Salimo 89

Ndakatulo ya Etani, wa banja la Ezara.

1Ndidzayimba za chikondi chachikulu cha Yehova kwamuyaya;

ndi pakamwa panga ndidzachititsa kuti kukhulupirika kwanu kudziwike ku mibado yonse.

2Ndidzalalikira kuti chikondi chanu chidzakhazikika mpaka muyaya,

kuti Inu munakhazikitsa kukhulupirika kwanu kumwamba kwenikweniko.

3Inu munati, “Ndachita pangano ndi wosankhidwa wanga,

ndalumbira kwa Davide mtumiki wanga kuti,

4‘Ndidzakhazikitsa zidzukulu zako mpaka muyaya.

Ndidzachititsa kuti mpando wako waufumu ukhazikike ku mibado yonse,’ ”

Sela.

5Mayiko akumwamba amatamanda zozizwitsa zanu Yehova,

kukhulupirika kwanunso, mu msonkhano wa oyera mtima anu.

6Pakuti ndani mu mlengalenga angalingane ndi Yehova?

Ndani wofanana ndi Yehova pakati pa zolengedwa zakumwamba?

7Mu msonkhano wa oyera mtima Mulungu amaopedwa kwambiri;

Iye ndiye wochititsa mantha kupambana onse amene amuzungulira.

8Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, ndani wofanana nanu?

Yehova ndinu wamphamvu ndipo kukhulupirika kwanu kwakuzungulirani.

9Mumalamula nyanja ya mafunde awukali;

pamene mafunde ake awundana Inu mumawakhalitsa bata.

10Munaphwanya Rahabe monga munthu wophedwa;

ndi dzanja lanu lamphamvu munabalalitsa adani anu.

11Mayiko akumwamba ndi anu ndiponso dziko lapansi ndi lanu;

munapanga dziko lonse ndi zonse zili mʼmenemo.

12Munalenga Kumpoto ndi Kummwera;

Tabori ndi Herimoni akuyimba ndi chimwemwe pa dzina lanu.

13Mkono wanu ndi wamphamvu;

dzanja lanu ndi lamphamvu, dzanja lanu lamanja ndi lopambana.

14Chilungamo ndi chiweruzo cholungama ndiye maziko a mpando wanu waufumu;

chikondi ndi kukhulupirika zimayenda patsogolo panu.

15Ndi odala amene aphunzira kuyamika Inu,

amene amayenda mʼkuwunika kwa nkhope yanu Yehova.

16Amakondwera mʼdzina lanu tsiku lonse lathunthu;

amasangalala koposa mʼchilungamo chanu.

17Pakuti Inu ndiye ulemerero wawo ndi mphamvu yawo

ndipo mwa kukoma mtima kwanu Inu mumakweza nyanga yathu.

18Ndithudi, chishango chathu ndi cha Yehova,

Mfumu yathu kwa Woyerayo wa Israeli.

19Kale munayankhula mʼmasomphenya,

kwa anthu anu okhulupirika munati,

“Ndapatsa mphamvu wankhondo;

ndakweza mnyamata wochokera pakati pa anthu.

20Ndamupeza mtumiki wanga Davide;

ndamudzoza ndi mafuta opatulika.

21Dzanja langa lidzamuchirikiza;

zoonadi, mkono wanga udzamupatsa mphamvu.

22Adani sadzamulamula kuti apereke msonkho;

anthu oyipa sadzamusautsa.

23Ndidzaphwanya adani ake pamaso pake

ndi kukantha otsutsana naye.

24Chikondi changa chokhulupirika chidzakhala naye,

ndipo kudzera mʼdzina langa nyanga yake idzakwezedwa.

25Ndidzayika dzanja lake pa nyanja,

dzanja lake lamanja pa mitsinje.

26Iyeyo adzafuwula kwa Ine kuti, ‘Ndinu Atate anga,

Mulungu wanga, Thanthwe ndi Chipulumutso changa.’

27Ndidzamuyika kuti akhale mwana wanga woyamba kubadwa;

wokwezedwa kwambiri pakati pa mafumu a dziko lapansi.

28Ndidzamusungira chifundo changa kwamuyaya,

ndipo pangano langa ndi iye silidzatha.

29Ine ndidzakhazikitsa zidzukulu zake mpaka muyaya,

mpando wake waufumu ngati masiku a miyamba.

30“Ngati ana ake adzataya lamulo langa

ndi kusatsatira malangizo anga,

31ngati adzaswa malamulo anga

ndi kulephera kusunga ziphunzitso zanga,

32Ine ndidzalanga tchimo lawo ndi ndodo,

mphulupulu zawo powakwapula.

33Koma sindidzachotsa chikondi changa pa iye,

kapena kukhala wosakhulupirika kwa iyeyo.

34Sindidzaswa pangano langa

kapena kusintha zimene milomo yanga yayankhula.

35Ndinalumbira kamodzi mwa kuyera kwanga

ndipo sindidzanama kwa Davide,

36kuti zidzukulu zake zidzakhale kwamuyaya

ndipo mpando wake waufumu udzakhazikika pamaso panga ngati dzuwa;

37udzakhazikika kwamuyaya monga mwezi,

mboni yokhulupirika mʼmitambo.

Sela

38“Koma tsopano Inu mwamukana, mwamutaya,

mwamukwiyira kwambiri wodzozedwa wanu.

39Mwakana pangano ndi mtumiki wanu

ndipo mwadetsa mʼfumbi chipewa chake chaufumu.

40Inu mwagumula makoma ake onse

ndipo mwasandutsa bwinja malinga ake.

41Onse amene amadutsa amalanda zinthu zake;

iye wakhala chotonzedwa cha anansi ake.

42Mwakweza dzanja lamanja la adani ake;

mwachititsa kuti adani ake akondwere.

43Mwabunthitsa lupanga lake,

simunamuthandize pa nkhondo.

44Inu mwathetsa kukongola kwa ulemerero wake

ndipo mwagwetsa pansi mpando wake waufumu.

45Mwachepetsa masiku a unyamata wake;

mwamuphimba ndi chofunda chochititsa manyazi.

Sela

46“Mpaka liti Yehova? Kodi mudzadzibisa mpaka kalekale?

Mpaka liti ukali wanu udzayaka ngati moto?

47Kumbukirani kuti masiku a moyo wanga ndi ochepa

pakuti munalenga kwachabe anthu onse!

48Kodi ndi munthu uti angakhale ndi moyo ndi kusaona imfa?

Kapena kudzipulumutsa yekha ku mphamvu ya manda?

Sela

49Inu Ambuye kodi chili kuti chikondi chanu chachikulu choyamba chija,

chimene mwa kukhulupirika kwanu munalumbira kwa Davide?

50Kumbukirani, Ambuye momwe mtumiki wanu wanyozedwera,

momwe ndakhalira ndi kusunga mu mtima mwanga mawu a pangano a anthu a mitundu yonse,

51mawu achipongwe amene adani anu akhala akunyoza, Inu Yehova,

ndi mawu amene akhala akunyoza mayendedwe onse a wodzozedwa wanu.

52“Matamando akhale kwa Yehova mpaka muyaya!”

Ameni ndi Ameni.

New Serbian Translation

Псалми 89:1-52

Псалам 89

Поучна песма Етан Езраита.

1О милости Господњој ја довека певам;

устима својим верност твоју разглашавам

нараштају сваком!

2Јер рекао сам: „Довека је милост чврста,

верност ти је постављена у небеса.“

3А ти: „Савез сам склопио са изабраником својим,

заклео се свом слузи Давиду:

4’Потомство ћу твоје довека да учврстим,

твој ће престо да потраје кроз поколење свако!’“ Села

5О, Господе, небеса славе чудеса твоја

и твоју верност у збору светих!

6Јер ко је тај на небу да је Господу налик,

да је као Господ међу синовима Божијим?

7Бог је величанствен на сабору светих,

страшнији је од свих што га окружују.

8Господе, Боже над војскама,

ко је попут тебе моћан Господ?

Верношћу си својом обавијен.

9Ти управљаш морем поноситим,

ти му спушташ таласе немирне.

10Скршио си Раву као да је заклан,

душмане си своје растерао силом руке своје.

11Твоја су небеса, баш као и земља;

свет и оно што га чини ти си поставио.

12Југ и север ти си начинио,

и Тавор и Ермон твом имену кличу.

13Мишица је твоја јака, рука ти је моћна,

десница је твоја подигнута.

14Твог престола темељи су праведност и правда;

милост и истина иду испред твога лица.

15Благо народу коме је клицање знано,

који живи у светлости лица твога, о, Господе!

16Имену се твоме они поваздан радују,

праведношћу твојом они се уздижу.

17Јер ти си слава њихове јакости,

наклоношћу твојом наш се рог89,17 Рог је симбол, метафора војне снаге, достојанства. уздиже.

18Јер наш је штит од Господа,

наш је цар од Светитеља Израиљевог.

19Тада си у виђењу говорио

свом верном народу и рекао:

„Своју помоћ дао сам јунаку,

изабраног из народа дигох.

20Нашао сам Давида, слугу свога,

уљем својим светим помазао сам га.

21На њему ће моја рука да почива,

мишица ће моја да га јача.

22Неће га варати непријатељ,

неће му наудити неправедник.

23Изломићу пред њим душмане његове,

и потући оне што га мрзе.

24Моја верност и милост моја биће са њим,

у моје ће се име подићи рог његов.

25Његову ћу руку дигнути на море

и на реке десницу његову.

26А он ће ме звати: ’Оче мој, Боже мој,

Стено мог спасења!’

27А ја ћу га поставити за прворођеног,

за најузвишенијег међу царевима земље.

28Довека ћу му очувати милост своју

и свој ћу савез да учврстим са њим.

29Довека ћу да учврстим потомство његово,

престо његов биће док је дана небу.

30А ако синови његови мој Закон напусте

и не живе по мојим уредбама;

31ако прекрше одредбе моје

и заповести моје не држе;

32казнићу им преступе шибом

и кривицу ударцима.

33Али милост своју никад нећу да им узмем,

верност своју нећу да порекнем.

34Нећу да погазим свој савез,

нећу да порекнем оно што устима обећао сам.

35Једном сам се заклео Давиду светошћу својом

и порећи нећу!

36Потомство ће његово довека да траје

и преда мном попут сунца престо његов;

37као месец заувек ће потрајати,

попут неба сведок верни.“ Села

38А сада си га свргнуо, згрозио се

и разјарио на свог помазаника;

39Порекао си савез са слугом својим,

у прашини му круну оскрнавио.

40Зарушио си му све зидине

и утврђења му у руине претворио.

41Харају га сви што путем прођу,

комшијама својим постао је ругло.

42Дигао си десницу душмана његових,

крвника његовог ти чиниш веселим.

43Још си му оштрицу мача отупио,

у боју му помогао ниси.

44Његов сјај си окончао,

срушио му престо у прашину.

45Скратио си дане младости његове

и загрнуо га срамотом. Села

46О, Господе, докле ћеш се крити?

Довека ти срџба као ватра букти?

47Присети се дужине мог живота.

Зар узалуд створио си све потомке људи?

48Ко је човек који је живео, а да смрти угледао није?

Из руку Света мртвих ко је живот избавио? Села

49О, Господе, где су твоја милосрђа давна

којима си се у верности својој заклео Давиду?

50Сети се, о, Господе, срамоћења својих слугу,

која носим у недрима од народа многих!

51Господе, њима су нас срамотили противници твоји;

њима су срамотили кораке твог помазаника.

52Благословен довека да је Господ!

Амин! Амин!