Masalimo 89 – CCL & KLB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 89:1-52

Salimo 89

Ndakatulo ya Etani, wa banja la Ezara.

1Ndidzayimba za chikondi chachikulu cha Yehova kwamuyaya;

ndi pakamwa panga ndidzachititsa kuti kukhulupirika kwanu kudziwike ku mibado yonse.

2Ndidzalalikira kuti chikondi chanu chidzakhazikika mpaka muyaya,

kuti Inu munakhazikitsa kukhulupirika kwanu kumwamba kwenikweniko.

3Inu munati, “Ndachita pangano ndi wosankhidwa wanga,

ndalumbira kwa Davide mtumiki wanga kuti,

4‘Ndidzakhazikitsa zidzukulu zako mpaka muyaya.

Ndidzachititsa kuti mpando wako waufumu ukhazikike ku mibado yonse,’ ”

Sela.

5Mayiko akumwamba amatamanda zozizwitsa zanu Yehova,

kukhulupirika kwanunso, mu msonkhano wa oyera mtima anu.

6Pakuti ndani mu mlengalenga angalingane ndi Yehova?

Ndani wofanana ndi Yehova pakati pa zolengedwa zakumwamba?

7Mu msonkhano wa oyera mtima Mulungu amaopedwa kwambiri;

Iye ndiye wochititsa mantha kupambana onse amene amuzungulira.

8Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, ndani wofanana nanu?

Yehova ndinu wamphamvu ndipo kukhulupirika kwanu kwakuzungulirani.

9Mumalamula nyanja ya mafunde awukali;

pamene mafunde ake awundana Inu mumawakhalitsa bata.

10Munaphwanya Rahabe monga munthu wophedwa;

ndi dzanja lanu lamphamvu munabalalitsa adani anu.

11Mayiko akumwamba ndi anu ndiponso dziko lapansi ndi lanu;

munapanga dziko lonse ndi zonse zili mʼmenemo.

12Munalenga Kumpoto ndi Kummwera;

Tabori ndi Herimoni akuyimba ndi chimwemwe pa dzina lanu.

13Mkono wanu ndi wamphamvu;

dzanja lanu ndi lamphamvu, dzanja lanu lamanja ndi lopambana.

14Chilungamo ndi chiweruzo cholungama ndiye maziko a mpando wanu waufumu;

chikondi ndi kukhulupirika zimayenda patsogolo panu.

15Ndi odala amene aphunzira kuyamika Inu,

amene amayenda mʼkuwunika kwa nkhope yanu Yehova.

16Amakondwera mʼdzina lanu tsiku lonse lathunthu;

amasangalala koposa mʼchilungamo chanu.

17Pakuti Inu ndiye ulemerero wawo ndi mphamvu yawo

ndipo mwa kukoma mtima kwanu Inu mumakweza nyanga yathu.

18Ndithudi, chishango chathu ndi cha Yehova,

Mfumu yathu kwa Woyerayo wa Israeli.

19Kale munayankhula mʼmasomphenya,

kwa anthu anu okhulupirika munati,

“Ndapatsa mphamvu wankhondo;

ndakweza mnyamata wochokera pakati pa anthu.

20Ndamupeza mtumiki wanga Davide;

ndamudzoza ndi mafuta opatulika.

21Dzanja langa lidzamuchirikiza;

zoonadi, mkono wanga udzamupatsa mphamvu.

22Adani sadzamulamula kuti apereke msonkho;

anthu oyipa sadzamusautsa.

23Ndidzaphwanya adani ake pamaso pake

ndi kukantha otsutsana naye.

24Chikondi changa chokhulupirika chidzakhala naye,

ndipo kudzera mʼdzina langa nyanga yake idzakwezedwa.

25Ndidzayika dzanja lake pa nyanja,

dzanja lake lamanja pa mitsinje.

26Iyeyo adzafuwula kwa Ine kuti, ‘Ndinu Atate anga,

Mulungu wanga, Thanthwe ndi Chipulumutso changa.’

27Ndidzamuyika kuti akhale mwana wanga woyamba kubadwa;

wokwezedwa kwambiri pakati pa mafumu a dziko lapansi.

28Ndidzamusungira chifundo changa kwamuyaya,

ndipo pangano langa ndi iye silidzatha.

29Ine ndidzakhazikitsa zidzukulu zake mpaka muyaya,

mpando wake waufumu ngati masiku a miyamba.

30“Ngati ana ake adzataya lamulo langa

ndi kusatsatira malangizo anga,

31ngati adzaswa malamulo anga

ndi kulephera kusunga ziphunzitso zanga,

32Ine ndidzalanga tchimo lawo ndi ndodo,

mphulupulu zawo powakwapula.

33Koma sindidzachotsa chikondi changa pa iye,

kapena kukhala wosakhulupirika kwa iyeyo.

34Sindidzaswa pangano langa

kapena kusintha zimene milomo yanga yayankhula.

35Ndinalumbira kamodzi mwa kuyera kwanga

ndipo sindidzanama kwa Davide,

36kuti zidzukulu zake zidzakhale kwamuyaya

ndipo mpando wake waufumu udzakhazikika pamaso panga ngati dzuwa;

37udzakhazikika kwamuyaya monga mwezi,

mboni yokhulupirika mʼmitambo.

Sela

38“Koma tsopano Inu mwamukana, mwamutaya,

mwamukwiyira kwambiri wodzozedwa wanu.

39Mwakana pangano ndi mtumiki wanu

ndipo mwadetsa mʼfumbi chipewa chake chaufumu.

40Inu mwagumula makoma ake onse

ndipo mwasandutsa bwinja malinga ake.

41Onse amene amadutsa amalanda zinthu zake;

iye wakhala chotonzedwa cha anansi ake.

42Mwakweza dzanja lamanja la adani ake;

mwachititsa kuti adani ake akondwere.

43Mwabunthitsa lupanga lake,

simunamuthandize pa nkhondo.

44Inu mwathetsa kukongola kwa ulemerero wake

ndipo mwagwetsa pansi mpando wake waufumu.

45Mwachepetsa masiku a unyamata wake;

mwamuphimba ndi chofunda chochititsa manyazi.

Sela

46“Mpaka liti Yehova? Kodi mudzadzibisa mpaka kalekale?

Mpaka liti ukali wanu udzayaka ngati moto?

47Kumbukirani kuti masiku a moyo wanga ndi ochepa

pakuti munalenga kwachabe anthu onse!

48Kodi ndi munthu uti angakhale ndi moyo ndi kusaona imfa?

Kapena kudzipulumutsa yekha ku mphamvu ya manda?

Sela

49Inu Ambuye kodi chili kuti chikondi chanu chachikulu choyamba chija,

chimene mwa kukhulupirika kwanu munalumbira kwa Davide?

50Kumbukirani, Ambuye momwe mtumiki wanu wanyozedwera,

momwe ndakhalira ndi kusunga mu mtima mwanga mawu a pangano a anthu a mitundu yonse,

51mawu achipongwe amene adani anu akhala akunyoza, Inu Yehova,

ndi mawu amene akhala akunyoza mayendedwe onse a wodzozedwa wanu.

52“Matamando akhale kwa Yehova mpaka muyaya!”

Ameni ndi Ameni.

Korean Living Bible

시편 89:1-52

다윗과 맺은 하나님의 계약

(에스라 사람 에단의 교훈시)

1여호와여, 내가 항상

주의 사랑을 노래하며

주의 성실하심을

대대에 전하겠습니다.

2주의 사랑이 영원하며

주의 성실하심이

하늘처럼 영구함을

내가 선포하겠습니다.

3주께서 말씀하셨습니다.

“내가 나의 택한 자와 계약을 맺고

나의 종 다윗에게 이렇게

맹세하였다.

4‘내가 네 자손을

대대로 왕위에 앉혀

네 나라가 영구히

지속되게 하리라.’ ”

5여호와여, 하늘이

주의 놀라운 일을 찬양하며

89:5 또는 ‘거룩한 자의 회중이’수많은 천사들이

주의 성실하심을 찬양합니다.

6하늘에서 여호와와

비교할 자가 누구며

하늘의 존재들 가운데

여호와와 같은 자가 누구입니까?

7거룩한 천사들도

주를 두려워하고 있습니다.

8전능하신 여호와 하나님이시여,

주와 같은 자가 누구입니까?

주는 능력이 많으시고

모든 일에 성실하신 분이십니다.

9주께서는 성난 바다를 다스리시며

파도가 일 때

그것을 잠잠하게 하십니다.

10주는 89:10 히 ‘라합을’이집트를

살해당한 자처럼 박살내고

주의 강한 능력으로

주의 원수들을 흩어 버렸습니다.

11하늘도 주의 것이며

땅도 주의 것입니다.

주께서 세계와

그 가운데 있는 모든 것을

만드셨습니다.

12남북을 주께서 만드셨으므로

다볼산과 헤르몬산이

기뻐서 주께 노래합니다.

13주는 능력이 많으시고

주의 힘은 위대합니다.

1489:14 또는 ‘의와 공의가’의와 심판이

주의 보좌의 기초가 되었으며

사랑과 성실이 주 앞에 있습니다.

15즐거운 노래로 주를 찬양하며

주의 빛 가운데 사는 자는

복이 있습니다.

16그들은 하루 종일

주의 이름과 의 때문에

기뻐하고 즐거워합니다.

17주는 그들의 영광과 힘이시며

사랑으로 우리의 힘을

북돋아 주는 분이십니다.

18여호와여, 주는

우리의 방패이십니다.

이스라엘의 거룩한 하나님이시여,

주께서 우리에게 왕을 주셨습니다.

19주는 한때 환상으로

주의 신실한 종들에게

이렇게 말씀하셨습니다.

“내가 용사에게 힘을 주고

백성 중에서 택한 자를 높였으니

20내 종 다윗을 찾아

거룩한 기름을 부어

그를 왕으로 삼은 것이라.

21내 손이 그를 붙들어 주고

내 팔이 그를 힘 있게 할 것이니

22원수가 그를 착취하지 못하고

악인이 그를 괴롭히지 못하리라.

23내가 그의 원수들을 박멸하고

그를 미워하는 자들을

모조리 죽이겠다.

24내가 성실과 사랑으로

그와 함께할 것이니

그가 내 이름으로

89:24 또는 ‘그 뿔이 높아지리로다’위대하게 되리라.

2589:25 문장 전체를 의역하였음.내가 그에게

지중해에서 유프라테스강까지

세력을 떨치게 할 것이니

26그가 나를 불러

‘주는 나의 아버지이며

나의 하나님이시요,

내 구원의 반석이십니다’ 하리라.

27내가 또 그를 내 맏아들로 삼고

세상에서 가장 위대한

왕이 되게 할 것이며

28그를 항상 사랑할 것이니

그와 맺은 계약이

영원히 변치 않을 것이다.

29내가 그 후손을

대대로 왕위에 앉혀

그의 나라가

끝없이 지속되게 하리라.

30“만일 그의 자손이 내 법을 어기고

내 지시에 순종하지 않으며

31내 교훈을 무시하고

내 명령을 지키지 않으면

32내가 막대기로 그들의 죄를 벌하고

채찍으로 그들의 죄를

다스릴 것이다.

33그러나 내가 그에게서

내 사랑과 신실함을 거두지 않고

34그와 맺은 계약을 어기거나

그에게 한 약속을

변경하지 않을 것이다.

35“내가 일단 나의 거룩함으로

맹세하였으니

절대로 다윗에게

거짓말을 하지 않으리라.

36그에게는 후손이 끊어지지 않고

그의 왕위는

해처럼 항상 내 앞에 있을 것이며

37하늘의 충실한 증인인 달처럼

영구할 것이다.”

38그러나 주께서는

기름 부어 택하신 왕에게 노하셔서

그를 거절하고 물리치셨으며

39주의 종과 맺은 계약을 깨뜨리시고 그의 왕관을 땅에 던져 더럽혔으며

40그의 모든 성벽을 헐고

그의 요새를 파괴해 버렸습니다.

41그러므로 지나가는 사람들이

그의 물건을 약탈하고

그의 이웃이 다 그를

비웃고 있습니다.

42주께서는 89:42 또는 ‘저의 대적의 오른손을 높이시고’그의 원수들에게

승리를 주셔서

그들이 기뻐하도록 하셨으며

43그의 칼날을 쓸모없게 하시고

그를 전쟁에서

패하게 하셨습니다.

44또 주는 그의 영광을 뺏으시고

그의 왕위를 땅에 엎으셨으며

45그의 젊은 시절을 단축하시고

그를 수치로 덮어 버렸습니다.

46여호와여, 이런 일이

언제까지 계속되겠습니까?

주는 영원히

자신을 숨기시겠습니까?

언제까지 주의 분노가

불처럼 타오르겠습니까?

47내 생명이 얼마나 짧은지

기억하소서.

주는 모든 인생을

정말 허무하게 창조하셨습니다.

48죽지 않고

영원히 살 자가 어디 있으며

무덤에 들어가지 않을 자가

어디 있습니까?

49여호와여,

이전의 주의 사랑은

어디 있으며

주께서 다윗에게 하신 약속은

어디 있습니까?

50여호와여, 주의 종이 당하는

모욕을 기억하소서.

모든 민족이 나를

멸시하고 있습니다.

51여호와여,

주의 원수들이

주께서 택하신 왕을 조롱하며

그의 거동까지 비웃고 있습니다.

52여호와를 영원히 찬양하라!

아멘! 아멘!