Masalimo 89 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 89:1-52

Salimo 89

Ndakatulo ya Etani, wa banja la Ezara.

1Ndidzayimba za chikondi chachikulu cha Yehova kwamuyaya;

ndi pakamwa panga ndidzachititsa kuti kukhulupirika kwanu kudziwike ku mibado yonse.

2Ndidzalalikira kuti chikondi chanu chidzakhazikika mpaka muyaya,

kuti Inu munakhazikitsa kukhulupirika kwanu kumwamba kwenikweniko.

3Inu munati, “Ndachita pangano ndi wosankhidwa wanga,

ndalumbira kwa Davide mtumiki wanga kuti,

4‘Ndidzakhazikitsa zidzukulu zako mpaka muyaya.

Ndidzachititsa kuti mpando wako waufumu ukhazikike ku mibado yonse,’ ”

Sela.

5Mayiko akumwamba amatamanda zozizwitsa zanu Yehova,

kukhulupirika kwanunso, mu msonkhano wa oyera mtima anu.

6Pakuti ndani mu mlengalenga angalingane ndi Yehova?

Ndani wofanana ndi Yehova pakati pa zolengedwa zakumwamba?

7Mu msonkhano wa oyera mtima Mulungu amaopedwa kwambiri;

Iye ndiye wochititsa mantha kupambana onse amene amuzungulira.

8Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, ndani wofanana nanu?

Yehova ndinu wamphamvu ndipo kukhulupirika kwanu kwakuzungulirani.

9Mumalamula nyanja ya mafunde awukali;

pamene mafunde ake awundana Inu mumawakhalitsa bata.

10Munaphwanya Rahabe monga munthu wophedwa;

ndi dzanja lanu lamphamvu munabalalitsa adani anu.

11Mayiko akumwamba ndi anu ndiponso dziko lapansi ndi lanu;

munapanga dziko lonse ndi zonse zili mʼmenemo.

12Munalenga Kumpoto ndi Kummwera;

Tabori ndi Herimoni akuyimba ndi chimwemwe pa dzina lanu.

13Mkono wanu ndi wamphamvu;

dzanja lanu ndi lamphamvu, dzanja lanu lamanja ndi lopambana.

14Chilungamo ndi chiweruzo cholungama ndiye maziko a mpando wanu waufumu;

chikondi ndi kukhulupirika zimayenda patsogolo panu.

15Ndi odala amene aphunzira kuyamika Inu,

amene amayenda mʼkuwunika kwa nkhope yanu Yehova.

16Amakondwera mʼdzina lanu tsiku lonse lathunthu;

amasangalala koposa mʼchilungamo chanu.

17Pakuti Inu ndiye ulemerero wawo ndi mphamvu yawo

ndipo mwa kukoma mtima kwanu Inu mumakweza nyanga yathu.

18Ndithudi, chishango chathu ndi cha Yehova,

Mfumu yathu kwa Woyerayo wa Israeli.

19Kale munayankhula mʼmasomphenya,

kwa anthu anu okhulupirika munati,

“Ndapatsa mphamvu wankhondo;

ndakweza mnyamata wochokera pakati pa anthu.

20Ndamupeza mtumiki wanga Davide;

ndamudzoza ndi mafuta opatulika.

21Dzanja langa lidzamuchirikiza;

zoonadi, mkono wanga udzamupatsa mphamvu.

22Adani sadzamulamula kuti apereke msonkho;

anthu oyipa sadzamusautsa.

23Ndidzaphwanya adani ake pamaso pake

ndi kukantha otsutsana naye.

24Chikondi changa chokhulupirika chidzakhala naye,

ndipo kudzera mʼdzina langa nyanga yake idzakwezedwa.

25Ndidzayika dzanja lake pa nyanja,

dzanja lake lamanja pa mitsinje.

26Iyeyo adzafuwula kwa Ine kuti, ‘Ndinu Atate anga,

Mulungu wanga, Thanthwe ndi Chipulumutso changa.’

27Ndidzamuyika kuti akhale mwana wanga woyamba kubadwa;

wokwezedwa kwambiri pakati pa mafumu a dziko lapansi.

28Ndidzamusungira chifundo changa kwamuyaya,

ndipo pangano langa ndi iye silidzatha.

29Ine ndidzakhazikitsa zidzukulu zake mpaka muyaya,

mpando wake waufumu ngati masiku a miyamba.

30“Ngati ana ake adzataya lamulo langa

ndi kusatsatira malangizo anga,

31ngati adzaswa malamulo anga

ndi kulephera kusunga ziphunzitso zanga,

32Ine ndidzalanga tchimo lawo ndi ndodo,

mphulupulu zawo powakwapula.

33Koma sindidzachotsa chikondi changa pa iye,

kapena kukhala wosakhulupirika kwa iyeyo.

34Sindidzaswa pangano langa

kapena kusintha zimene milomo yanga yayankhula.

35Ndinalumbira kamodzi mwa kuyera kwanga

ndipo sindidzanama kwa Davide,

36kuti zidzukulu zake zidzakhale kwamuyaya

ndipo mpando wake waufumu udzakhazikika pamaso panga ngati dzuwa;

37udzakhazikika kwamuyaya monga mwezi,

mboni yokhulupirika mʼmitambo.

Sela

38“Koma tsopano Inu mwamukana, mwamutaya,

mwamukwiyira kwambiri wodzozedwa wanu.

39Mwakana pangano ndi mtumiki wanu

ndipo mwadetsa mʼfumbi chipewa chake chaufumu.

40Inu mwagumula makoma ake onse

ndipo mwasandutsa bwinja malinga ake.

41Onse amene amadutsa amalanda zinthu zake;

iye wakhala chotonzedwa cha anansi ake.

42Mwakweza dzanja lamanja la adani ake;

mwachititsa kuti adani ake akondwere.

43Mwabunthitsa lupanga lake,

simunamuthandize pa nkhondo.

44Inu mwathetsa kukongola kwa ulemerero wake

ndipo mwagwetsa pansi mpando wake waufumu.

45Mwachepetsa masiku a unyamata wake;

mwamuphimba ndi chofunda chochititsa manyazi.

Sela

46“Mpaka liti Yehova? Kodi mudzadzibisa mpaka kalekale?

Mpaka liti ukali wanu udzayaka ngati moto?

47Kumbukirani kuti masiku a moyo wanga ndi ochepa

pakuti munalenga kwachabe anthu onse!

48Kodi ndi munthu uti angakhale ndi moyo ndi kusaona imfa?

Kapena kudzipulumutsa yekha ku mphamvu ya manda?

Sela

49Inu Ambuye kodi chili kuti chikondi chanu chachikulu choyamba chija,

chimene mwa kukhulupirika kwanu munalumbira kwa Davide?

50Kumbukirani, Ambuye momwe mtumiki wanu wanyozedwera,

momwe ndakhalira ndi kusunga mu mtima mwanga mawu a pangano a anthu a mitundu yonse,

51mawu achipongwe amene adani anu akhala akunyoza, Inu Yehova,

ndi mawu amene akhala akunyoza mayendedwe onse a wodzozedwa wanu.

52“Matamando akhale kwa Yehova mpaka muyaya!”

Ameni ndi Ameni.

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Salmo 89:1-52

Salmo 89

Masquil de Etán el ezraíta.

1Oh Señor, por siempre cantaré

la grandeza de tu amor;

por todas las generaciones

proclamará mi boca tu fidelidad.

2Declararé que tu amor permanece firme para siempre,

que has afirmado en el cielo tu fidelidad.

3Dijiste: «He hecho un pacto con mi escogido;

le he jurado a David mi siervo:

4“Estableceré tu dinastía para siempre,

y afirmaré tu trono por todas las generaciones”». Selah

5Los cielos, Señor, celebran tus maravillas,

y tu fidelidad la asamblea de los santos.

6¿Quién en los cielos es comparable al Señor?

¿Quién como él entre los seres celestiales?

7Dios es muy temido en la asamblea de los santos;

grande y portentoso sobre cuantos lo rodean.

8¿Quién como tú, Señor Dios Todopoderoso,

rodeado de poder y de fidelidad?

9Tú gobiernas sobre el mar embravecido;

tú apaciguas sus encrespadas olas.

10Aplastaste a Rahab como a un cadáver;

con tu brazo poderoso dispersaste a tus enemigos.

11Tuyo es el cielo, y tuya la tierra;

tú fundaste el mundo y todo lo que contiene.

12Por ti fueron creados el norte y el sur;

el Tabor y el Hermón cantan alegres a tu nombre.

13Tu brazo es capaz de grandes proezas;

fuerte es tu mano, exaltada tu diestra.

14La justicia y el derecho son el fundamento de tu trono,

y tus heraldos, el amor y la verdad.

15Dichosos los que saben aclamarte, Señor,

y caminan a la luz de tu presencia;

16los que todo el día se alegran en tu nombre

y se regocijan en tu justicia.

17Porque tú eres su gloria y su poder;

por tu buena voluntad aumentas nuestra fuerza.89:17 aumentas nuestra fuerza. Lit. levantas nuestro cuerno.

18Tú, Señor, eres nuestro escudo;

tú, Santo de Israel, eres nuestro rey.

19Una vez hablaste en una visión,

y le dijiste a tu pueblo fiel:

«Le he brindado mi ayuda a un valiente;

al mejor hombre del pueblo lo he exaltado.

20He encontrado a David, mi siervo,

y lo he ungido con mi aceite santo.

21Mi mano siempre lo sostendrá;

mi brazo lo fortalecerá.

22Ningún enemigo lo someterá a tributo;

ningún inicuo lo oprimirá.

23Aplastaré a quienes se le enfrenten

y derribaré a quienes lo aborrezcan.

24La fidelidad de mi amor lo acompañará,

y por mi nombre será exaltada su fuerza.89:24 su fuerza. Lit. su cuerno.

25Le daré poder sobre el mar89:25 el mar. Probable referencia al mar Mediterráneo.

y dominio sobre los ríos.89:25 los ríos. Probable referencia a Mesopotamia.

26Él me dirá: “Tú eres mi Padre,

mi Dios, la roca de mi salvación”.

27Yo le daré los derechos de primogenitura,

la primacía sobre los reyes de la tierra.

28Mi amor por él será siempre constante,

y mi pacto con él se mantendrá fiel.

29Afirmaré su dinastía y su trono

para siempre, mientras el cielo exista.

30»Pero, si sus hijos se apartan de mi ley

y no viven según mis decretos,

31si violan mis estatutos

y no observan mis mandamientos,

32con vara castigaré sus transgresiones

y con azotes su iniquidad.

33Con todo, jamás le negaré mi amor,

ni mi fidelidad le faltará.

34No violaré mi pacto

ni me retractaré de mis palabras.

35Una sola vez he jurado por mi santidad,

y no voy a mentirle a David:

36Su descendencia vivirá para siempre;

su trono durará como el sol en mi presencia.

37Como la luna, fiel testigo en el cielo,

será establecido para siempre». Selah

38Pero tú has desechado, has rechazado a tu ungido;

te has enfurecido contra él en gran manera.

39Has revocado el pacto con tu siervo;

has arrastrado por los suelos su corona.

40Has derribado todas sus murallas

y dejado en ruinas sus fortalezas.

41Todos los que pasan lo saquean;

¡es motivo de burla para sus vecinos!

42Has exaltado el poder de sus adversarios

y llenado de gozo a sus enemigos.

43Le has quitado el filo a su espada,

y no lo has apoyado en la batalla.

44Has puesto fin a su esplendor

al derribar por tierra su trono.

45Has acortado los días de su juventud;

lo has cubierto con un manto de vergüenza. Selah

46¿Hasta cuándo, Señor, te seguirás escondiendo?

¿Va a arder tu ira para siempre, como el fuego?

47¡Recuerda cuán efímera es mi vida!89:47 Véase 39:4.

Al fin y al cabo, ¿para qué creaste a los mortales?

48¿Quién hay que viva y no muera jamás,

o que pueda escapar del poder del sepulcro? Selah

49¿Dónde está, Señor, tu amor de antaño,

que en tu fidelidad juraste a David?

50Recuerda, Señor, que se burlan de tus siervos;

que llevo en mi pecho los insultos de muchos pueblos.

51Tus enemigos, Señor, nos ultrajan;

a cada paso ofenden a tu ungido.

52¡Bendito sea el Señor por siempre!

Amén y amén.