Masalimo 89 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 89:1-52

Salimo 89

Ndakatulo ya Etani, wa banja la Ezara.

1Ndidzayimba za chikondi chachikulu cha Yehova kwamuyaya;

ndi pakamwa panga ndidzachititsa kuti kukhulupirika kwanu kudziwike ku mibado yonse.

2Ndidzalalikira kuti chikondi chanu chidzakhazikika mpaka muyaya,

kuti Inu munakhazikitsa kukhulupirika kwanu kumwamba kwenikweniko.

3Inu munati, “Ndachita pangano ndi wosankhidwa wanga,

ndalumbira kwa Davide mtumiki wanga kuti,

4‘Ndidzakhazikitsa zidzukulu zako mpaka muyaya.

Ndidzachititsa kuti mpando wako waufumu ukhazikike ku mibado yonse,’ ”

Sela.

5Mayiko akumwamba amatamanda zozizwitsa zanu Yehova,

kukhulupirika kwanunso, mu msonkhano wa oyera mtima anu.

6Pakuti ndani mu mlengalenga angalingane ndi Yehova?

Ndani wofanana ndi Yehova pakati pa zolengedwa zakumwamba?

7Mu msonkhano wa oyera mtima Mulungu amaopedwa kwambiri;

Iye ndiye wochititsa mantha kupambana onse amene amuzungulira.

8Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, ndani wofanana nanu?

Yehova ndinu wamphamvu ndipo kukhulupirika kwanu kwakuzungulirani.

9Mumalamula nyanja ya mafunde awukali;

pamene mafunde ake awundana Inu mumawakhalitsa bata.

10Munaphwanya Rahabe monga munthu wophedwa;

ndi dzanja lanu lamphamvu munabalalitsa adani anu.

11Mayiko akumwamba ndi anu ndiponso dziko lapansi ndi lanu;

munapanga dziko lonse ndi zonse zili mʼmenemo.

12Munalenga Kumpoto ndi Kummwera;

Tabori ndi Herimoni akuyimba ndi chimwemwe pa dzina lanu.

13Mkono wanu ndi wamphamvu;

dzanja lanu ndi lamphamvu, dzanja lanu lamanja ndi lopambana.

14Chilungamo ndi chiweruzo cholungama ndiye maziko a mpando wanu waufumu;

chikondi ndi kukhulupirika zimayenda patsogolo panu.

15Ndi odala amene aphunzira kuyamika Inu,

amene amayenda mʼkuwunika kwa nkhope yanu Yehova.

16Amakondwera mʼdzina lanu tsiku lonse lathunthu;

amasangalala koposa mʼchilungamo chanu.

17Pakuti Inu ndiye ulemerero wawo ndi mphamvu yawo

ndipo mwa kukoma mtima kwanu Inu mumakweza nyanga yathu.

18Ndithudi, chishango chathu ndi cha Yehova,

Mfumu yathu kwa Woyerayo wa Israeli.

19Kale munayankhula mʼmasomphenya,

kwa anthu anu okhulupirika munati,

“Ndapatsa mphamvu wankhondo;

ndakweza mnyamata wochokera pakati pa anthu.

20Ndamupeza mtumiki wanga Davide;

ndamudzoza ndi mafuta opatulika.

21Dzanja langa lidzamuchirikiza;

zoonadi, mkono wanga udzamupatsa mphamvu.

22Adani sadzamulamula kuti apereke msonkho;

anthu oyipa sadzamusautsa.

23Ndidzaphwanya adani ake pamaso pake

ndi kukantha otsutsana naye.

24Chikondi changa chokhulupirika chidzakhala naye,

ndipo kudzera mʼdzina langa nyanga yake idzakwezedwa.

25Ndidzayika dzanja lake pa nyanja,

dzanja lake lamanja pa mitsinje.

26Iyeyo adzafuwula kwa Ine kuti, ‘Ndinu Atate anga,

Mulungu wanga, Thanthwe ndi Chipulumutso changa.’

27Ndidzamuyika kuti akhale mwana wanga woyamba kubadwa;

wokwezedwa kwambiri pakati pa mafumu a dziko lapansi.

28Ndidzamusungira chifundo changa kwamuyaya,

ndipo pangano langa ndi iye silidzatha.

29Ine ndidzakhazikitsa zidzukulu zake mpaka muyaya,

mpando wake waufumu ngati masiku a miyamba.

30“Ngati ana ake adzataya lamulo langa

ndi kusatsatira malangizo anga,

31ngati adzaswa malamulo anga

ndi kulephera kusunga ziphunzitso zanga,

32Ine ndidzalanga tchimo lawo ndi ndodo,

mphulupulu zawo powakwapula.

33Koma sindidzachotsa chikondi changa pa iye,

kapena kukhala wosakhulupirika kwa iyeyo.

34Sindidzaswa pangano langa

kapena kusintha zimene milomo yanga yayankhula.

35Ndinalumbira kamodzi mwa kuyera kwanga

ndipo sindidzanama kwa Davide,

36kuti zidzukulu zake zidzakhale kwamuyaya

ndipo mpando wake waufumu udzakhazikika pamaso panga ngati dzuwa;

37udzakhazikika kwamuyaya monga mwezi,

mboni yokhulupirika mʼmitambo.

Sela

38“Koma tsopano Inu mwamukana, mwamutaya,

mwamukwiyira kwambiri wodzozedwa wanu.

39Mwakana pangano ndi mtumiki wanu

ndipo mwadetsa mʼfumbi chipewa chake chaufumu.

40Inu mwagumula makoma ake onse

ndipo mwasandutsa bwinja malinga ake.

41Onse amene amadutsa amalanda zinthu zake;

iye wakhala chotonzedwa cha anansi ake.

42Mwakweza dzanja lamanja la adani ake;

mwachititsa kuti adani ake akondwere.

43Mwabunthitsa lupanga lake,

simunamuthandize pa nkhondo.

44Inu mwathetsa kukongola kwa ulemerero wake

ndipo mwagwetsa pansi mpando wake waufumu.

45Mwachepetsa masiku a unyamata wake;

mwamuphimba ndi chofunda chochititsa manyazi.

Sela

46“Mpaka liti Yehova? Kodi mudzadzibisa mpaka kalekale?

Mpaka liti ukali wanu udzayaka ngati moto?

47Kumbukirani kuti masiku a moyo wanga ndi ochepa

pakuti munalenga kwachabe anthu onse!

48Kodi ndi munthu uti angakhale ndi moyo ndi kusaona imfa?

Kapena kudzipulumutsa yekha ku mphamvu ya manda?

Sela

49Inu Ambuye kodi chili kuti chikondi chanu chachikulu choyamba chija,

chimene mwa kukhulupirika kwanu munalumbira kwa Davide?

50Kumbukirani, Ambuye momwe mtumiki wanu wanyozedwera,

momwe ndakhalira ndi kusunga mu mtima mwanga mawu a pangano a anthu a mitundu yonse,

51mawu achipongwe amene adani anu akhala akunyoza, Inu Yehova,

ndi mawu amene akhala akunyoza mayendedwe onse a wodzozedwa wanu.

52“Matamando akhale kwa Yehova mpaka muyaya!”

Ameni ndi Ameni.

La Bible du Semeur

Psaumes 89:1-53

Où sont les grâces d’autrefois ?

1Méditation89.1 Sens incertain. d’Etân89.1 Voir 1 R 5.11 ; 1 Ch 6.16-29 ; 15.16-19. l’Ezrahite.

2Je veux chanter à jamais ╵les bontés de l’Eternel

et proclamer d’âge en âge ╵sa fidélité.

3En effet, je peux le dire : ╵ta bonté est établie ╵pour l’éternité.

Dans les cieux tu as ancré ╵ta fidélité.

4Tu as déclaré : ╵« J’ai contracté une alliance ╵avec mon élu ;

à David, mon serviteur, ╵j’ai fait un serment :

5J’affermis ta descendance ╵pour l’éternité,

et j’établirai ton trône ╵aux siècles des siècles89.5 Voir 2 S 7.12-16 ; 1 Ch 17.11-14 ; Ps 132.11-12.. »

Pause

6O Eternel, les cieux chantent ╵tes prodiges.

L’assemblée des saints célèbre ╵ta fidélité.

7Qui dans les nuées ╵est égal à l’Eternel ?

Qui est comparable à l’Eternel ╵parmi les êtres célestes ?

8Car c’est un Dieu redoutable ╵au conseil des saints89.8 Très certainement les anges.,

il est grand, impressionnant ╵au-dessus de tous ceux qui l’entourent.

9Qui, ô Eternel, ╵ô Dieu des armées célestes, ╵qui est puissant comme toi ? ╵Qui, ô Eternel ?

Ta fidélité rayonne ╵tout autour de toi.

10Oui, c’est toi seul qui maîtrises ╵l’orgueil de la mer.

Quand ses vagues se déchaînent, ╵toi, tu les apaises.

11C’est toi qui as écrasé Rahav, ╵le dragon d’Egypte, ╵le blessant à mort89.11 Voir Ps 87.4 et la note..

Par ton bras puissant ╵tu as dispersé tes ennemis.

12A toi appartient le ciel ╵et à toi la terre,

le monde avec tout ce qui s’y trouve, ╵c’est toi qui les as fondés.

13Le nord et le sud, ╵tu les as créés.

Le mont Thabor et l’Hermon89.13 Sommets imposants du nord d’Israël., ╵avec joie, t’acclament.

14Ton bras est armé de force,

ta main est puissante, ╵tu as levé ta main droite89.14 Signe de puissance (le dieu Baal était souvent représenté avec la main droite levée)..

15Les assises de ton trône ╵sont justice et droit.

L’amour et la vérité ╵marchent devant toi.

16Oh ! qu’il est heureux, le peuple ╵qui sait t’acclamer.

Eternel, à ta lumière, ╵il chemine.

17Grâce à toi, ╵il se réjouit sans cesse,

grâce à ta justice, ╵il s’élève !

18Car c’est toi qui fais ╵sa gloire et sa force,

et c’est grâce à ta faveur ╵que nous triomphons.

19Oui, de l’Eternel dépend ╵notre protecteur,

notre roi est dans la main ╵du Saint d’Israël.

20Autrefois, tu as parlé ╵dans une révélation ╵à ceux qui sont attachés à toi. ╵Tu as dit :

« J’ai prêté secours ╵à un homme valeureux ;

au milieu du peuple, ╵j’ai élevé un jeune homme ╵à une haute fonction :

21j’ai trouvé mon serviteur David89.21 Voir 1 S 13.14 et Ac 13.22. ;

de mon huile sainte, ╵je lui ai donné l’onction89.21 Voir 1 S 16.12-13..

22Je le soutiendrai ╵de ma forte main,

et mon bras le rendra fort.

23Ses ennemis ne pourront ╵jamais le surprendre,

aucun homme inique ╵ne pourra le maltraiter.

24J’écraserai devant lui ╵tous ses adversaires,

et je frapperai ╵ceux qui le haïssent.

25Toujours mon fidèle amour ╵l’accompagnera.

Grâce à moi, ╵il relèvera le front.

26J’étendrai jusqu’à la mer ╵sa domination.

J’établirai son empire ╵jusque sur les fleuves89.26 La mer est la Méditerranée, les fleuves l’Euphrate et ses divers bras ou canaux ; c’étaient les limites des domaines promis à David et à Salomon..

27Il m’invoquera ╵par ces mots : ╵“Toi, tu es mon Père,

et mon Dieu, ╵le rocher ╵où je trouve le salut.”

28Et moi, je ferai de lui ╵mon fils premier-né,

le plus élevé ╵des rois de la terre89.28 Voir Col 1.15..

29Je lui garderai toujours ╵toute ma faveur,

et maintiendrai fermement ╵mon alliance avec lui.

30Je ferai subsister pour toujours ╵sa postérité,

et son trône durera ╵autant que les cieux.

31S’il arrivait que ses fils ╵délaissent ma Loi,

s’ils ne se conduisaient plus ╵selon mes décrets,

32s’ils venaient à transgresser ╵mes commandements,

et s’ils n’obéissaient plus ╵à mes ordonnances,

33je châtierais leur péché ╵avec le bâton,

et leur faute par des coups.

34Mais je ne renierai pas ╵mon amour pour lui.

Je ne démentirai pas ╵ma fidélité ;

35non, car je ne trahirai ╵jamais mon alliance

et je ne reviendrai pas ╵sur ce que j’ai dit.

36Un jour, j’ai fait le serment ╵par ma sainteté :

Non, je ne pourrai jamais ╵mentir à David.

37Sa lignée subsistera ╵éternellement,

et son trône devant moi ╵sera comme le soleil.

38Comme la lune, à toujours, ╵il se maintiendra.

Là-haut, le témoin céleste ╵en est le garant. »

Pause

39Pourtant, tu l’as délaissé, ╵tu l’as rejeté,

et tu t’es mis en colère ╵contre celui qui avait reçu ╵l’onction de ta part.

40Tu as dédaigné l’alliance ╵faite avec ton serviteur,

et tu as profané sa couronne, ╵la jetant à terre.

41Tu as fait de larges brèches ╵dans tous ses remparts,

et ses fortifications, ╵tu les as détruites.

42Tous les passants l’ont pillé,

ses voisins le raillent.

43Tu as affermi ses adversaires

et tu as rempli de joie ╵tous ses ennemis.

44Tu as même fait dévier ╵les coups de son glaive.

Tu ne l’as pas soutenu ╵pendant le combat.

45Tu as éteint sa splendeur,

jeté bas son trône,

46tu as abrégé ╵sa jeunesse,

et tu l’as couvert de honte.

Pause

47Jusques à quand, Eternel, ╵te cacheras-tu sans cesse

et laisseras-tu flamber ╵ta fureur ?

48Veuille tenir compte ╵de la brièveté de ma vie,

as-tu donc créé ╵pour le néant tous les hommes ?

49Quel homme vivra ╵sans voir le trépas ?

Qui échappera ╵au séjour des morts ?

Pause

50Seigneur, où donc sont restées ╵tes faveurs d’antan

que, dans ta fidélité, ╵tu avais promises ╵par un serment à David ?

51Pense, Seigneur, à l’opprobre ╵de tes serviteurs89.51 Plusieurs manuscrits hébreux, l’ancienne version grecque et la version syriaque ont : ton serviteur.,

et pense à ces nombreux peuples ╵dont je suis chargé89.51 Autre traduction : Considère, Seigneur, de quel opprobre tes serviteurs sont affligés par de nombreux peuples et quelle souffrance il me cause..

52Pense, Eternel, aux outrages ╵de tes ennemis,

aux outrages qu’ils déversent ╵sur les pas de l’homme ╵qui a reçu l’onction de ta part.

53Béni soit l’Eternel pour l’éternité !

Amen et amen !