Masalimo 88 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 88:1-18

Salimo 88

Salimo la ana a Kora. Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a nyimbo yoti: “Pa Matenda ndi pa Mazunzo.” Ndakatulo ya Hemani, wa banja la Ezara.

1Inu Yehova, Mulungu amene mumandipulumutsa,

usana ndi usiku ndimalira pamaso panu.

2Pemphero langa lifike pamaso panu;

tcherani khutu lanu kuti mumve kulira kwanga.

3Pakuti ndili ndi mavuto ambiri

ndipo moyo wanga ukuyandikira ku manda.

4Ndikuwerengedwa pamodzi ndi iwo amene akutsikira ku dzenje;

ndine munthu wopanda mphamvu.

5Ndayikidwa pambali pamodzi ndi anthu akufa,

monga ophedwa amene agona mʼmanda,

amene Inu simuwakumbukiranso,

amene achotsedwa pa chisamaliro chanu.

6Mwandiyika pansi pa dzenje penipeni,

mʼmalo akuya a mdima waukulu.

7Ukali wanu ukundipsinja kwambiri,

mwandiopseza kwambiri ndi mafunde anu onse.

Sela

8Mwandichotsa pakati pa abwenzi anga enieni

ndipo mwachititsa kuti ndikhale chonyansa kwa iwo.

Ndatsekerezedwa ndipo sindingathe kuthawa;

9maso anga ada ndi chisoni.

Ndimayitana Inu Yehova tsiku lililonse;

ndimakweza manja anga kwa Inu.

10Kodi mumaonetsa zozizwitsa zanu kwa anthu akufa?

Kodi iwo amene afa amaukanso ndi kutamanda Inu?

Sela

11Kodi chikondi chanu chimalalikidwa mʼmanda,

za kukhulupirika kwanu ku malo a chiwonongeko?

12Kodi zozizwitsa zanu zimadziwika ku malo a mdima,

kapena ntchito zanu zolungama ku dziko la anthu oyiwalika?

13Inu Yehova, Ine ndimalirira thandizo;

mmawa mapemphero anga amafika pamaso panu.

14Inu Yehova nʼchifukwa chiyani mukundikana

ndi kundibisira nkhope yanu?

15Kuyambira ubwana wanga ndakhala ndikuzunzika pafupi kufa;

ndakhala ndikuchita mantha ndipo ndine wothedwa nzeru.

16Ukali wanu wandimiza;

zoopsa zanu zandiwononga.

17Tsiku lonse zimandizungulira ngati chigumula;

zandimiza kwathunthu.

18Inu mwatenga anzanga ndi okondedwa anga kuwachotsa pamaso panga;

mdima ndiye bwenzi langa lenileni.

Hoffnung für Alle

Psalm 88:1-19

Am Rande des Todes – völlig allein!

1Ein Lied von den Nachkommen Korachs. Der Esrachiter Heman verfasste es zum Nachdenken. Auf eine traurige Weise zu singen.

2Herr, mein Gott, du allein kannst mir noch helfen!

Tag und Nacht schreie ich zu dir!

3Lass mein Gebet zu dir dringen,

verschließ deine Ohren nicht vor meinem Flehen!

4Schweres Leid drückt mich nieder,

ich bin dem Tod schon näher als dem Leben.

5Jeder rechnet damit, dass ich bald sterbe,

denn alle Kraft hat mich verlassen.

6Es geht mir wie den Toten, die du vergessen hast,

fern von deiner Hilfe liegen sie in ihrem Grab.

7Du hast mich in den tiefsten Abgrund gestoßen,

in nichts als unergründliche Finsternis.

8Dein Zorn lastet schwer auf mir,

wie hohe Brandungswellen wirft er mich um.

9Alle meine Freunde hast du mir genommen,

voller Abscheu wandten sie sich von mir ab.

Ich bin gefangen und weiß keinen Ausweg mehr.

10Meine Augen sind vom Weinen ganz verquollen.

Jeden Tag rufe ich, Herr, zu dir

und strecke meine Hände nach dir aus.

11Wirst du an den Toten noch ein Wunder tun?

Kommen sie etwa aus ihren Gräbern, um dich zu loben?

12Erzählt man im Totenreich von deiner Gnade

oder in der Gruft von deiner Treue?

13Sind deine Wunder wohl am Ort der Finsternis bekannt?

Wissen die längst vergessenen Toten von deiner Gerechtigkeit?

14Herr, ich schreie zu dir um Hilfe.

Schon früh am Morgen klage ich dir mein Leid.

15Warum hast du mich verstoßen, Herr?

Warum verbirgst du dich vor mir?

16Seit meiner Jugend bin ich elend und vom Tod gezeichnet.

Du hast mir dieses furchtbare Leid auferlegt –

und jetzt bin ich am Ende!

17Dein glühender Zorn hat mich zu Boden geschmettert,

deine schreckliche Strafe hat mich vernichtet!

18Die Angst bedrängt mich von allen Seiten,

vor dieser tödlichen Flut gibt es kein Entrinnen.

19Du hast erreicht, dass mir alle den Rücken kehren,

Freunde und Nachbarn gehen mir aus dem Weg.

Mein einziger Begleiter ist die Finsternis.