Masalimo 88 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 88:1-18

Salimo 88

Salimo la ana a Kora. Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a nyimbo yoti: “Pa Matenda ndi pa Mazunzo.” Ndakatulo ya Hemani, wa banja la Ezara.

1Inu Yehova, Mulungu amene mumandipulumutsa,

usana ndi usiku ndimalira pamaso panu.

2Pemphero langa lifike pamaso panu;

tcherani khutu lanu kuti mumve kulira kwanga.

3Pakuti ndili ndi mavuto ambiri

ndipo moyo wanga ukuyandikira ku manda.

4Ndikuwerengedwa pamodzi ndi iwo amene akutsikira ku dzenje;

ndine munthu wopanda mphamvu.

5Ndayikidwa pambali pamodzi ndi anthu akufa,

monga ophedwa amene agona mʼmanda,

amene Inu simuwakumbukiranso,

amene achotsedwa pa chisamaliro chanu.

6Mwandiyika pansi pa dzenje penipeni,

mʼmalo akuya a mdima waukulu.

7Ukali wanu ukundipsinja kwambiri,

mwandiopseza kwambiri ndi mafunde anu onse.

Sela

8Mwandichotsa pakati pa abwenzi anga enieni

ndipo mwachititsa kuti ndikhale chonyansa kwa iwo.

Ndatsekerezedwa ndipo sindingathe kuthawa;

9maso anga ada ndi chisoni.

Ndimayitana Inu Yehova tsiku lililonse;

ndimakweza manja anga kwa Inu.

10Kodi mumaonetsa zozizwitsa zanu kwa anthu akufa?

Kodi iwo amene afa amaukanso ndi kutamanda Inu?

Sela

11Kodi chikondi chanu chimalalikidwa mʼmanda,

za kukhulupirika kwanu ku malo a chiwonongeko?

12Kodi zozizwitsa zanu zimadziwika ku malo a mdima,

kapena ntchito zanu zolungama ku dziko la anthu oyiwalika?

13Inu Yehova, Ine ndimalirira thandizo;

mmawa mapemphero anga amafika pamaso panu.

14Inu Yehova nʼchifukwa chiyani mukundikana

ndi kundibisira nkhope yanu?

15Kuyambira ubwana wanga ndakhala ndikuzunzika pafupi kufa;

ndakhala ndikuchita mantha ndipo ndine wothedwa nzeru.

16Ukali wanu wandimiza;

zoopsa zanu zandiwononga.

17Tsiku lonse zimandizungulira ngati chigumula;

zandimiza kwathunthu.

18Inu mwatenga anzanga ndi okondedwa anga kuwachotsa pamaso panga;

mdima ndiye bwenzi langa lenileni.

La Bible du Semeur

Psaumes 88:1-19

Prière d’un homme près de la mort

1Un psaume des Qoréites88.1 Voir note 42.1.. Cantique à chanter avec accompagnement de flûtes88.1 Sens incertain.. Au chef de chœur. Une méditation88.1 Sens incertain. d’Hémân88.1 Voir 1 Ch 6.18-22 ; 25.1, 4. l’Ezrahite.

2Eternel Dieu, toi qui me sauves,

je crie à toi, ╵pendant le jour, pendant la nuit, ╵en ta présence.

3Que ma prière ╵parvienne jusqu’à toi !

Veuille prêter attention à mes cris !

4Car je suis rassasié de maux,

et je suis tout près de la mort.

5Déjà je suis compté ╵parmi ceux qui s’en vont ╵dans le tombeau.

Je ressemble à un homme

qui a perdu ses forces.

6C’est au milieu des morts ╵que j’ai ma place,

comme ceux qui, ╵mortellement blessés, ╵sont couchés dans la tombe,

que tu as oubliés

et dont tu ne t’occupes plus.

7Tu m’as jeté ╵dans un gouffre sans fond,

dans les fonds ténébreux.

8Ta fureur me tenaille,

les flots de ta colère ╵ont déferlé sur moi.

Pause

9Tu as fait s’éloigner de moi mes proches,

tu as fait de moi un objet d’horreur pour eux.

Je suis emprisonné, ╵je ne peux m’en sortir.

10Mes yeux sont épuisés ╵à force d’affliction.

Je t’invoque, Eternel, ╵tout au long de mes jours,

je tends les mains vers toi.

11Feras-tu des prodiges ╵pour ceux qui ne sont plus ?

Verra-t-on se lever ╵les morts pour te louer ?

Pause

12Parle-t-on dans la tombe ╵de ton amour ?

De ta fidélité ╵dans le séjour des morts ?

13Connaît-on tes prodiges ╵là où sont les ténèbres,

et ta justice ╵au pays de l’oubli ?

14Pour moi, ô Eternel, ╵je crie à toi,

je te présente ma prière ╵chaque matin.

15Pourquoi, ô Eternel, ╵me rejeter,

me refuser ton attention ?

16Car je suis affligé, ╵près de la mort ╵depuis que je suis jeune ;

j’endure les terreurs ╵que tu m’imposes. ╵Je suis désemparé.

17Les flots de ta colère ╵ont déferlé sur moi,

je suis anéanti ╵par les angoisses ╵qui me viennent de toi.

18Comme des eaux qui me submergent,

de toutes parts, ╵elles m’assaillent tous les jours.

19Tu as fait s’éloigner de moi ╵tous mes amis, mes compagnons !

Ma seule compagnie ╵est celle des ténèbres.