Masalimo 87 – CCL & NVI

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 87:1-7

Salimo 87

Salimo la Ana a Kora.

1Iye wakhazikitsa maziko ake pa phiri loyera;

2Yehova amakonda zipata za Ziyoni

kupambana malo onse okhalamo a Yakobo.

3Za ulemerero wako zimakambidwa,

Iwe mzinda wa Mulungu:

Sela

4“Ndidzanena za Rahabe ndi Babuloni

pakati pa iwo amene amandidziwa.

Dzikonso la Filisitiya, Turo pamodzi ndi Kusi,

ndipo ndidzati, ‘Uyu anabadwira mʼZiyoni.’ ”

5Ndithudi, za Ziyoni adzanena kuti,

“Uyu ndi uyo anabadwira mwa iye,

ndipo Wammwambamwamba adzakhazikitsa iyeyo.”

6Yehova adzalemba mʼbuku la kawundula wa anthu a mitundu ina:

“Uyu anabadwira mʼZiyoni.”

Sela

7Oyimba ndi ovina omwe adzati,

“Akasupe anga onse ali mwa iwe.”

Nueva Versión Internacional

Salmo 87:1-7

Salmo 87

Salmo de los hijos de Coré. Cántico.

1Los cimientos de la ciudad de Dios87:1 Los … de Dios. Lit. Los cimientos de él. están en el santo monte.

2El Señor ama las entradas de Sión

más que a todas las moradas de Jacob.

3De ti, ciudad de Dios,

se dicen cosas gloriosas: Selah

4«Entre los que me reconocen

puedo contar a Rahab y a Babilonia,

a Filistea y a Tiro, lo mismo que a Cus.

Se dice: “Este nació en Sión”».

5De Sión se dirá, en efecto:

«Este y aquel nacieron en ella.

El Altísimo mismo la ha establecido».

6El Señor anotará en el registro de los pueblos:

«Este nació en Sión». Selah

7Y mientras cantan y bailan, dicen:

«Todas mis fuentes están en ti».87:7 Todas mis fuentes. Alt. Todos mis orígenes.