Salimo 87
Salimo la Ana a Kora.
1Iye wakhazikitsa maziko ake pa phiri loyera;
2Yehova amakonda zipata za Ziyoni
kupambana malo onse okhalamo a Yakobo.
3Za ulemerero wako zimakambidwa,
Iwe mzinda wa Mulungu:
Sela
4“Ndidzanena za Rahabe ndi Babuloni
pakati pa iwo amene amandidziwa.
Dzikonso la Filisitiya, Turo pamodzi ndi Kusi,
ndipo ndidzati, ‘Uyu anabadwira mʼZiyoni.’ ”
5Ndithudi, za Ziyoni adzanena kuti,
“Uyu ndi uyo anabadwira mwa iye,
ndipo Wammwambamwamba adzakhazikitsa iyeyo.”
6Yehova adzalemba mʼbuku la kawundula wa anthu a mitundu ina:
“Uyu anabadwira mʼZiyoni.”
Sela
7Oyimba ndi ovina omwe adzati,
“Akasupe anga onse ali mwa iwe.”
Psalm 87
A psalm of the Sons of Korah. A song.
1The Lord has built his city
on the holy mountain.
2He loves the city of Zion
more than all the other places
where the people of Jacob live.
3City of God,
the Lord says glorious things about you.
4He says, “I will include Egypt and Babylon
in a list of nations who recognize me as king.
I will also include Philistia and Tyre, along with Cush.
I will say about them, ‘They were born in Zion.’ ”
5Certainly it will be said about Zion,
“This nation and that nation were born in it.
The Most High God himself will make it secure.”
6Here is what the Lord will write in his list of the nations.
“Each of them was born in Zion.”
7As they make music they will sing,
“Zion, all our blessings come from you.”