Masalimo 87 – CCL & NAV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 87:1-7

Salimo 87

Salimo la Ana a Kora.

1Iye wakhazikitsa maziko ake pa phiri loyera;

2Yehova amakonda zipata za Ziyoni

kupambana malo onse okhalamo a Yakobo.

3Za ulemerero wako zimakambidwa,

Iwe mzinda wa Mulungu:

Sela

4“Ndidzanena za Rahabe ndi Babuloni

pakati pa iwo amene amandidziwa.

Dzikonso la Filisitiya, Turo pamodzi ndi Kusi,

ndipo ndidzati, ‘Uyu anabadwira mʼZiyoni.’ ”

5Ndithudi, za Ziyoni adzanena kuti,

“Uyu ndi uyo anabadwira mwa iye,

ndipo Wammwambamwamba adzakhazikitsa iyeyo.”

6Yehova adzalemba mʼbuku la kawundula wa anthu a mitundu ina:

“Uyu anabadwira mʼZiyoni.”

Sela

7Oyimba ndi ovina omwe adzati,

“Akasupe anga onse ali mwa iwe.”

Ketab El Hayat

مزمور 87:1-7

الْمَزْمُورُ السَّابِعُ وَالثَّمَانُونَ

مَزْمُورٌ لِبَنِي قُورَحَ. تَسْبِيحَةٌ

1أَسَّسَ اللهُ الْمَدِينَةَ عَلَى الْجِبَالِ الْمُقَدَّسَةِ. 2أَحَبَّ الرَّبُّ أَبْوَابَ صِهْيَوْنَ أَكْثَرَ مِنْ جَمِيعِ مَسَاكِنِ بَنِي يَعْقُوبَ. 3يَتَحَدَّثُونَ عَنْكِ بِأُمُورٍ مَجِيدَةٍ يَا مَدِينَةَ اللهِ.

4أَذْكُرُ مِصْرَ وَبَابِلَ بَيْنَ الَّذِينَ يَعْرِفُونَنِي، وَكَذَلِكَ فَلَسْطِينَ وَصُورَ مَعَ الْحَبَشَةِ، فَيَقُولُونَ: هَذَا وُلِدَ فِي صِهْيَوْنَ. 5حَقّاً عَنْ صِهْيَوْنَ يَقُولُونَ: «هَذَا الإِنْسَانُ وَهَذَا الإِنْسَانُ وُلِدَ فِيهَا، وَالْعَلِيُّ يُثَبِّتُهَا». 6يُدَوِّنُ الرَّبُّ فِي سِجِلِّ إِحْصَاءِ الشُّعُوبِ أَنَّ هَذَا وُلِدَ هُنَاكَ. 7الْمُرَنِّمُونَ وَالْعَازِفُونَ عَلَى السَّوَاءِ يَقُولُونَ: «فِيكِ كُلُّ يَنَابِيعِ سُرُورِي».