Masalimo 87 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 87:1-7

Salimo 87

Salimo la Ana a Kora.

1Iye wakhazikitsa maziko ake pa phiri loyera;

2Yehova amakonda zipata za Ziyoni

kupambana malo onse okhalamo a Yakobo.

3Za ulemerero wako zimakambidwa,

Iwe mzinda wa Mulungu:

Sela

4“Ndidzanena za Rahabe ndi Babuloni

pakati pa iwo amene amandidziwa.

Dzikonso la Filisitiya, Turo pamodzi ndi Kusi,

ndipo ndidzati, ‘Uyu anabadwira mʼZiyoni.’ ”

5Ndithudi, za Ziyoni adzanena kuti,

“Uyu ndi uyo anabadwira mwa iye,

ndipo Wammwambamwamba adzakhazikitsa iyeyo.”

6Yehova adzalemba mʼbuku la kawundula wa anthu a mitundu ina:

“Uyu anabadwira mʼZiyoni.”

Sela

7Oyimba ndi ovina omwe adzati,

“Akasupe anga onse ali mwa iwe.”

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

詩篇 87:1-7

第 87 篇

頌讚錫安

可拉後裔的詩。

1耶和華的城座落在聖山上。

2雅各的住處中,

祂最喜愛錫安的門。

3上帝的城啊,

人們傳揚你的榮耀。(細拉)

4「我要把埃及87·4 埃及人」希伯來文是「拉哈伯」,埃及的別名。巴比倫人、非利士人、泰爾人和古實人列為認識我的民族,

視他們為錫安人。」

5至於錫安,必有人說:

「萬族必成為城中的居民,

至高者必親自堅立這城。」

6耶和華將萬民登記入冊的時候,

必把他們列為錫安的居民。(細拉)

7他們跳舞歌唱說:

「我們蒙福的泉源在錫安。」