Masalimo 87 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 87:1-7

Salimo 87

Salimo la Ana a Kora.

1Iye wakhazikitsa maziko ake pa phiri loyera;

2Yehova amakonda zipata za Ziyoni

kupambana malo onse okhalamo a Yakobo.

3Za ulemerero wako zimakambidwa,

Iwe mzinda wa Mulungu:

Sela

4“Ndidzanena za Rahabe ndi Babuloni

pakati pa iwo amene amandidziwa.

Dzikonso la Filisitiya, Turo pamodzi ndi Kusi,

ndipo ndidzati, ‘Uyu anabadwira mʼZiyoni.’ ”

5Ndithudi, za Ziyoni adzanena kuti,

“Uyu ndi uyo anabadwira mwa iye,

ndipo Wammwambamwamba adzakhazikitsa iyeyo.”

6Yehova adzalemba mʼbuku la kawundula wa anthu a mitundu ina:

“Uyu anabadwira mʼZiyoni.”

Sela

7Oyimba ndi ovina omwe adzati,

“Akasupe anga onse ali mwa iwe.”

Bibelen på hverdagsdansk

Salmernes Bog 87:1-7

Jerusalem—Guds by og hans folks hjem

1En sang af Koras slægt.

Han grundlagde sin by på de hellige høje.

2Ja, Herren elsker Zions stad

langt mere end andre byer i Israel.

3Jerusalem, du er Guds egen by,

der siges mange herlige ting om dig.

4I Egypten og Babylonien,

i filistrenes land, i Tyrus og Kush

er der folk, der kender Gud

og føler, at Jerusalem er deres hjem.

5I Jerusalem siger man til hinanden:

„Vi hører alle til på dette sted,

og den Almægtige tager hånd om sin by.”

6Herren fører regnskab over alle mennesker,

og noterer dem, der hører Jerusalem til.

7De danser af glæde, mens de lovpriser byen:

„Du er alt, hvad vi har brug for.”