Masalimo 86 – CCL & KLB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 86:1-17

Salimo 86

Pemphero la Davide.

1Ndimvereni Yehova ndipo mundiyankhe,

pakuti ndine wosauka ndi wosowa.

2Yangʼanirani moyo wanga, pakuti ndine wodzipereka kwa Inu.

Inu ndinu Mulungu wanga;

pulumutsani mtumiki wanu amene amadalira Inu.

Inu ndinu Mulungu wanga.

3Mundichitire chifundo, Inu Ambuye,

pakuti ndikuyitana Inu tsiku lonse.

4Bweretsani chimwemwe kwa mtumiki wanu, Ambuye,

pakuti ndimadalira Inu.

5Inu Ambuye, ndinu wokhululuka ndi wabwino,

wodzaza ndi chikondi kwa onse amene amayitana Inu.

6Yehova imvani pemphero langa;

mvetserani kulira kwanga kofuna chifundo.

7Pa tsiku la mavuto anga ndidzayitana Inu,

pakuti Inu mudzandiyankha.

8Pakati pa milungu palibe wina wofanana nanu Ambuye;

palibe ntchito zolingana ndi ntchito zanu.

9Mitundu yonse ya anthu imene munayipanga

idzabwera ndi kudzalambira pamaso panu Ambuye;

iwo adzabweretsa ulemerero pa dzina lanu.

10Pakuti ndinu wamkulu ndipo mumachita zodabwitsa;

Inu nokha ndiye Mulungu.

11Ndiphunzitseni njira yanu Yehova,

ndipo ndidzayenda mʼchoonadi chanu;

patseni mtima wosagawikana

kuti ndilemekeze dzina lanu.

12Ndidzakutamandani Ambuye Mulungu wanga, ndi mtima wanga wonse;

ndidzalemekeza dzina lanu kwamuyaya.

13Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu kwa ine;

mwandipulumutsa ku malo ozama a manda.

14Inu Mulungu wanga, anthu odzikuza akundithira nkhondo;

anthu ankhanza akufuna kundipha,

amene salabadira za Inu.

15Koma Ambuye ndinu Mulungu wachifundo ndi wokoma mtima,

wosakwiya msanga, wodzaza ndi chikondi ndi wokhulupirika.

16Tembenukirani kwa ine ndipo ndichitireni chifundo;

perekani mphamvu zanu kwa mtumiki wanu

ndipo pulumutsani mwana wa mdzakazi wanu.

17Mundionetse chizindikiro cha ubwino wanu

kuti adani achione ndi kuchititsidwa manyazi,

pakuti Yehova mwandithandiza ndi kunditonthoza.

Korean Living Bible

시편 86:1-17

도움을 구하는 기도

(다윗의 기도)

1여호와여,

내가 큰 어려움을

당하고 있습니다.

나에게 귀를 기울이시고

응답하소서.

286:2 또는 ‘나는 경건하오니’나는 주께 헌신한 자입니다.

내 생명을 지키소서.

주는 나의 하나님이십니다.

주를 의지하는

주의 종을 구원하소서.

3여호와여, 나를 불쌍히 여기소서.

내가 하루 종일 주께 부르짖습니다.

4내 영혼이 주를 바라봅니다.

주여, 내 영혼을 기쁘게 하소서.

5주는 선하시고

기꺼이 용서해 주시며

주께 부르짖는 자에게

한없이 사랑을 베푸시는

분이십니다.

6여호와여, 내 기도에

귀를 기울이시고

내가 간절히 부르짖는

소리를 들으소서.

7주는 내 기도에

응답하시는 분이시므로

내가 환난 날에 주께 부르짖습니다.

8여호와여, 주와 같은 신이 없으며

주께서 하신 일을 행한 자가

아무도 없습니다.

9주께서 창조하신 모든 민족이

주 앞에 와서 경배할 것이며

주의 이름을 찬양할 것입니다.

10주는 위대하시고

놀라운 일을 행하시는 분이시므로

주만 하나님이십니다.

11여호와여, 주의 길을

나에게 가르치소서.

내가 주의 진리 가운데

걸어가겠습니다.

나에게 한결같은 마음을 주셔서

내가 주의 이름을

두려워하게 하소서.

12주 나의 하나님이시여,

내가 마음을 다하여 주를 찬양하고

영원히 주의 이름에

영광을 돌리겠습니다.

13주는 나에게 크신 사랑을 베푸셔서

내 영혼을 86:13 또는 ‘음부에서’무덤에서

건져 주셨습니다.

14하나님이시여,

교만한 자들이 와서 나를 치고

잔인한 무리들이

나를 죽이려고 하며

그들이 주를 멸시합니다.

15그러나 여호와여, 주는

자비롭고 은혜로우신 분이시며

쉽게 화를 내지 않으시고

신실하며 사랑이 많으신

하나님이십니다.

16나를 돌아보고

나를 불쌍히 여기소서.

주의 종에게 힘을 주시고

86:16 또는 ‘주의 여종의 아들을’주의 신실한 아들을 구원하소서.

17여호와여, 주의 은혜의 증거를

나에게 주셔서

나를 미워하는 자들이

부끄러움을 당하게 하소서.

주는 나를 돕고

위로하시는 분이십니다.