Masalimo 86 – CCL & APSD-CEB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 86:1-17

Salimo 86

Pemphero la Davide.

1Ndimvereni Yehova ndipo mundiyankhe,

pakuti ndine wosauka ndi wosowa.

2Yangʼanirani moyo wanga, pakuti ndine wodzipereka kwa Inu.

Inu ndinu Mulungu wanga;

pulumutsani mtumiki wanu amene amadalira Inu.

Inu ndinu Mulungu wanga.

3Mundichitire chifundo, Inu Ambuye,

pakuti ndikuyitana Inu tsiku lonse.

4Bweretsani chimwemwe kwa mtumiki wanu, Ambuye,

pakuti ndimadalira Inu.

5Inu Ambuye, ndinu wokhululuka ndi wabwino,

wodzaza ndi chikondi kwa onse amene amayitana Inu.

6Yehova imvani pemphero langa;

mvetserani kulira kwanga kofuna chifundo.

7Pa tsiku la mavuto anga ndidzayitana Inu,

pakuti Inu mudzandiyankha.

8Pakati pa milungu palibe wina wofanana nanu Ambuye;

palibe ntchito zolingana ndi ntchito zanu.

9Mitundu yonse ya anthu imene munayipanga

idzabwera ndi kudzalambira pamaso panu Ambuye;

iwo adzabweretsa ulemerero pa dzina lanu.

10Pakuti ndinu wamkulu ndipo mumachita zodabwitsa;

Inu nokha ndiye Mulungu.

11Ndiphunzitseni njira yanu Yehova,

ndipo ndidzayenda mʼchoonadi chanu;

patseni mtima wosagawikana

kuti ndilemekeze dzina lanu.

12Ndidzakutamandani Ambuye Mulungu wanga, ndi mtima wanga wonse;

ndidzalemekeza dzina lanu kwamuyaya.

13Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu kwa ine;

mwandipulumutsa ku malo ozama a manda.

14Inu Mulungu wanga, anthu odzikuza akundithira nkhondo;

anthu ankhanza akufuna kundipha,

amene salabadira za Inu.

15Koma Ambuye ndinu Mulungu wachifundo ndi wokoma mtima,

wosakwiya msanga, wodzaza ndi chikondi ndi wokhulupirika.

16Tembenukirani kwa ine ndipo ndichitireni chifundo;

perekani mphamvu zanu kwa mtumiki wanu

ndipo pulumutsani mwana wa mdzakazi wanu.

17Mundionetse chizindikiro cha ubwino wanu

kuti adani achione ndi kuchititsidwa manyazi,

pakuti Yehova mwandithandiza ndi kunditonthoza.

Ang Pulong Sa Dios

Salmo 86:1-17

Salmo 8686:0 Salmo 86 Ang ulohan sa Hebreo: Ang pag-ampo ni David.

Pag-ampo alang sa Tabang sa Dios

1Ginoo, pamatia ug tubaga ang akong pag-ampo kay ako kabos ug timawa.

2Tipigi ang akong kinabuhi kay ako diosnon.

Ikaw ang akong Dios;

luwasa ako nga imong alagad nga nagasalig kanimo.

3Kaloy-i ako, Ginoo,

kay tibuok adlaw akong nagapanawag kanimo.

4Lipaya ako nga imong alagad, Ginoo,

kay kanimo ako nagaampo.

5Tinuod nga ikaw maayo ug mapinasayloon,

ug puno ka sa paghigugma sa tanang nagapanawag kanimo.

6Pamatia ang akong pag-ampo, Ginoo;

pamatia ang akong pagpakilooy kanimo.

7Nagatawag ako kanimo sa panahon sa kalisod kay tubagon mo man ako.

8Walay dios nga sama kanimo, Ginoo;

walay bisan kinsa nga makahimo sa imong gipanghimo.

9Ang tanang nasod nga imong gihimo mosimba kanimo,

ug dayegon ka nila.

10Kay ikaw gamhanan, ug katingalahan ang imong mga buhat;

ikaw lang ang Dios.

11Tudloi ako, Ginoo, sa imong pamaagi,

ug tumanon ko kini nga matinud-anon kanimo.86:11 kini nga matinud-anon kanimo: o, ang imong kamatuoran.

Tabangi ako nga mahimong matinud-anon sa akong pagtahod kanimo.

12Ginoo nga akong Dios,

dayegon ko ikaw sa tibuok kong kasingkasing.

Dayegon ko ikaw sa walay kataposan.

13Kay dako ang imong gugma kanako;

giluwas mo ako sa kamatayon.

14O Dios, gisulong ako sa grupo sa garboso nga mga tawo aron sa pagpatay kanako.

Mga bangis sila ug wala makaila kanimo.

15Apan ikaw, Ginoo, may kahangawa ug maloloy-on nga Dios.

Mahigugmaon ikaw ug matinud-anon, ug dili daling masuko.

16Tagda ako ug kaloy-i;

hatagi ako sa imong kusog ug luwasa ako nga imong alagad.

17Hatagi ako ug timailhan sa imong kaayo aron makita kini sa akong mga kaaway ug maulawan sila.

Kay ikaw, Ginoo, ang nagatabang ug nagalipay kanako.