Masalimo 85 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 85:1-13

Salimo 85

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora.

1Yehova munakomera mtima dziko lanu;

munabwezeretsa ulemerero wa Yakobo.

2Munakhululukira mphulupulu za anthu anu

ndi kuphimba machimo awo onse.

Sela

3Munayika pambali ukali wanu wonse

ndi kutembenuka kuchoka ku mkwiyo wanu woopsa.

4Tibwezeretseninso mwakale Inu Mulungu Mpulumutsi wathu,

ndipo mutichotsere mkwiyo wanu.

5Kodi mudzatikwiyira mpaka liti?

Kodi mudzapitiriza kukwiya pa mibado yathu yonse?

6Kodi simudzatitsitsimutsanso,

kuti anthu anu asangalale mwa Inu?

7Tionetseni chikondi chanu chosatha, Inu Yehova,

ndipo tipatseni chipulumutso chanu.

8Ndidzamvetsera zimene Yehova Mulungu adzanena;

Iye amalonjeza mtendere kwa anthu ake, oyera mtima ake,

koma musawalole kuti abwerere ku zopusa.

9Ndithu chipulumutso chake chili pafupi ndi iwo amene amaopa Iye,

kuti ulemerero wake ukhale mʼdziko lathu.

10Chikondi ndi kukhulupirika zimakumana pamodzi;

chilungamo ndi mtendere zimapsompsonana.

11Kukhulupirika kumatumphuka kuchokera ku dziko lapansi,

ndipo chilungamo chimayangʼana pansi kuchokera kumwamba.

12Ndithu Yehova adzapereka chimene chili chabwino,

ndipo dziko lathu lidzapereka zokolola zake.

13Wolungama amapita patsogolo pake

ndi kukonza njira za mapazi ake.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

詩篇 85:1-13

第 85 篇

為國家求福

可拉後裔的詩,交給樂長。

1耶和華啊,你賜福了你的土地,

使雅各的子孫重返家園。

2你赦免了你子民的罪過,

遮蓋了他們所有的過犯。(細拉)

3你收回自己的怒氣,

不發烈怒。

4拯救我們的上帝啊,

求你復興我們,

止息你對我們的怒氣。

5你要向我們永遠發怒嗎?

你的怒氣要延續到萬代嗎?

6你不再復興我們,

使你的子民靠你歡喜嗎?

7耶和華啊,求你向我們施慈愛,拯救我們。

8我要聽耶和華上帝所說的話,

因為祂應許賜平安給祂忠心的子民。

但我們不可再犯罪。

9祂拯救敬畏祂的人,

好讓祂的榮耀常駐在我們的地上。

10慈愛和忠信同行,

公義與平安相親。

11忠信從地而生,

公義從天而現。

12耶和華賜下祝福,

我們的土地就出產豐富。

13公義要行在祂面前,為祂開路。