Masalimo 85 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 85:1-13

Salimo 85

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora.

1Yehova munakomera mtima dziko lanu;

munabwezeretsa ulemerero wa Yakobo.

2Munakhululukira mphulupulu za anthu anu

ndi kuphimba machimo awo onse.

Sela

3Munayika pambali ukali wanu wonse

ndi kutembenuka kuchoka ku mkwiyo wanu woopsa.

4Tibwezeretseninso mwakale Inu Mulungu Mpulumutsi wathu,

ndipo mutichotsere mkwiyo wanu.

5Kodi mudzatikwiyira mpaka liti?

Kodi mudzapitiriza kukwiya pa mibado yathu yonse?

6Kodi simudzatitsitsimutsanso,

kuti anthu anu asangalale mwa Inu?

7Tionetseni chikondi chanu chosatha, Inu Yehova,

ndipo tipatseni chipulumutso chanu.

8Ndidzamvetsera zimene Yehova Mulungu adzanena;

Iye amalonjeza mtendere kwa anthu ake, oyera mtima ake,

koma musawalole kuti abwerere ku zopusa.

9Ndithu chipulumutso chake chili pafupi ndi iwo amene amaopa Iye,

kuti ulemerero wake ukhale mʼdziko lathu.

10Chikondi ndi kukhulupirika zimakumana pamodzi;

chilungamo ndi mtendere zimapsompsonana.

11Kukhulupirika kumatumphuka kuchokera ku dziko lapansi,

ndipo chilungamo chimayangʼana pansi kuchokera kumwamba.

12Ndithu Yehova adzapereka chimene chili chabwino,

ndipo dziko lathu lidzapereka zokolola zake.

13Wolungama amapita patsogolo pake

ndi kukonza njira za mapazi ake.

La Bible du Semeur

Psaumes 85:1-14

L’Eternel nous rend le bonheur

1Au chef de chœur. Psaume des Qoréites85.1 Voir note 42.1..

2Eternel, tu as montré ╵ta faveur à ton pays.

Tu as rétabli Jacob85.2 Autre traduction : tu as ramené ceux de Jacob qui étaient en captivité..

3Tu as pardonné ╵les fautes commises par ton peuple,

tu as effacé tous ses péchés.

Pause

4Tu as retenu ╵toute ta fureur,

tu es revenu ╵de ton ardente colère.

5Oh, rétablis-nous85.5 Autre traduction : reviens à nous, ou bien, en répartissant les consonnes du verbe hébreu en deux mots : change donc de dispositions., ╵Dieu, notre Sauveur !

Mets un terme ╵à ta colère envers nous !

6Vas-tu, éternellement, ╵être irrité contre nous ?

Ton ressentiment ╵durera-t-il d’âge en âge ?

7Ne voudrais-tu pas ╵nous rendre à la vie

afin que ton peuple ╵se réjouisse en toi ?

8Fais-nous contempler, ╵ton amour, ô Eternel !

Accorde-nous ton salut !

9Je veux écouter ╵ce que dit Dieu, l’Eternel :

c’est de bien-être qu’il parle ╵à son peuple ╵et à ceux qui lui sont attachés.

Mais qu’ils ne retournent pas ╵à leur fol égarement.

10Oui, il va bientôt ╵œuvrer au salut ╵de ceux qui le craignent,

afin que sa gloire ╵puisse demeurer ╵dans notre pays.

11L’amour, la fidélité ╵vont se rencontrer,

et la justice et la paix ╵se donneront l’accolade.

12La vérité germera ╵du sein de la terre,

et la justice regardera ╵depuis les hauteurs célestes.

13L’Eternel lui-même ╵nous donnera le bonheur

et notre pays ╵produira ses fruits.

14La justice le précédera,

elle tracera ╵un chemin devant ses pas85.14 Autre traduction : et elle imprimera ses traces de pas sur le chemin..