Masalimo 83 – CCL & KLB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 83:1-18

Salimo 83

Nyimbo. Salimo la Asafu.

1Inu Mulungu musakhale chete;

musangoti phee, Mulungu musangoti duu.

2Onani adani anu akuchita chiwawa,

amene amadana nanu autsa mitu yawo.

3Mochenjera iwo akukambirana za chiwembu kutsutsana ndi anthu anu;

Iwo akukonzekera kutsutsana ndi omwe mumawakonda.

4Iwo akunena kuti, “Bwerani” akutero, “Tiyeni tiwononge mtundu wonsewu

kuti dzina la Israeli lisakumbukikenso.”

5Ndi mtima umodzi akukonzekera chiwembu;

Iwo achita mgwirizano kutsutsana nanu:

6Matenti a Edomu ndi Aismaeli,

Mowabu ndi Ahagiri,

7Agebala, Aamoni ndi Aamaleki,

Afilisti, pamodzi ndi anthu a ku Turo.

8Ngakhalenso Aasiriya aphatikizana nawo

kupereka mphamvu kwa ana a Loti.

Sela

9Muwachitire zomwe munachitira Amidiyani,

monga munachitira Sisera ndi Yabini ku mtsinje wa Kisoni.

10Amene anawonongedwa ku Endori

ndi kukhala ngati zinyalala.

11Anthu awo otchuka muwachite zomwe munachita Orebu ndi Zeebu

ana a mafumu muwachite zomwe munachita Zeba ndi Zalimuna,

12amene anati, “Tiyeni tilande dziko

la msipu la Mulungu.”

13Muwasandutse fumbi lowuluka, Inu Mulungu wanga,

ngati mankhusu owuluka ndi mphepo.

14Monga moto umatentha nkhalango,

kapena malawi a moto kuyatsa phiri,

15kotero muwathamangitse ndi mphepo yamkuntho,

ndi kuwachititsa mantha ndi namondwe.

16Muphimbe nkhope zawo ndi manyazi

kuti adzafunefune dzina lanu Yehova.

17Achite manyazi ndi mantha nthawi zonse;

awonongeke mwa manyazi.

18Adziwe kuti Inu amene dzina lanu ndi Yehova,

ndinu nokha Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi.

Korean Living Bible

시편 83:1-18

원수들을 벌해 달라는 기도

(노래로 부른 아삽의 시)

1하나님이시여,

침묵을 지키지 마소서.

하나님이시여,

말없이 조용하게 계시지 마소서.

2보소서.

주의 원수들이 소란을 피우며

주를 미워하는 자들이

우쭐대고 있습니다.

3그들이 주의 백성을 치고자

책략을 꾸미고

주께서 보호하는 자를 치려고

음모를 꾸며 말합니다.

4“자, 저희 나라를 멸망시키고

다시는 이스라엘이란 이름이

기억되지 않게 하자.”

5그들이 함께

주를 대적할 음모를 꾸미고

동맹을 맺었으니

6에돔 사람과 이스마엘 사람,

모압과 하갈 사람,

7그발과 암몬과 아말렉 사람이며

블레셋과 두로 사람입니다.

8앗시리아 사람들도

그들에게 가담하여

롯의 후손을 도왔습니다.

9주는 미디안 사람들에게

행하신 것과 같이

기손 강가에서 시스라와 야빈에게

행하신 것과 같이

그들에게 행하소서.

10그들은 엔돌에서 패망하여

그 시체가

땅의 거름처럼 썩은 자들입니다.

11그들의 귀족들을

오렙과 스엡처럼 되게 하시고

그들의 통치자들은

세바와 살문나처럼 되게 하소서.

12그들은 하나님의 목장을

소유하자고 말한 자들입니다.

13나의 하나님이시여,

그들을 먼지처럼 흩어 버리시고

바람에 날아가는

지푸라기 같게 하소서.

14불이 숲을 태우고

화염이 산을 삼켜 버리듯이

15주께서 광풍으로

그들을 추격하셔서

주의 폭풍으로

그들을 두렵게 하소서.

16여호와여,

그들이 얼굴을 들 수 없을 정도로

수치를 당하게 하여

주의 이름을 찾게 하소서.

17그들이 수치를 당하여

놀라게 하시며

치욕 가운데 패망하게 하셔서

18여호와이신 주께서만

온 세상을 다스리는

가장 높으신 분이심을 알게 하소서.