Masalimo 83 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 83:1-18

Salimo 83

Nyimbo. Salimo la Asafu.

1Inu Mulungu musakhale chete;

musangoti phee, Mulungu musangoti duu.

2Onani adani anu akuchita chiwawa,

amene amadana nanu autsa mitu yawo.

3Mochenjera iwo akukambirana za chiwembu kutsutsana ndi anthu anu;

Iwo akukonzekera kutsutsana ndi omwe mumawakonda.

4Iwo akunena kuti, “Bwerani” akutero, “Tiyeni tiwononge mtundu wonsewu

kuti dzina la Israeli lisakumbukikenso.”

5Ndi mtima umodzi akukonzekera chiwembu;

Iwo achita mgwirizano kutsutsana nanu:

6Matenti a Edomu ndi Aismaeli,

Mowabu ndi Ahagiri,

7Agebala, Aamoni ndi Aamaleki,

Afilisti, pamodzi ndi anthu a ku Turo.

8Ngakhalenso Aasiriya aphatikizana nawo

kupereka mphamvu kwa ana a Loti.

Sela

9Muwachitire zomwe munachitira Amidiyani,

monga munachitira Sisera ndi Yabini ku mtsinje wa Kisoni.

10Amene anawonongedwa ku Endori

ndi kukhala ngati zinyalala.

11Anthu awo otchuka muwachite zomwe munachita Orebu ndi Zeebu

ana a mafumu muwachite zomwe munachita Zeba ndi Zalimuna,

12amene anati, “Tiyeni tilande dziko

la msipu la Mulungu.”

13Muwasandutse fumbi lowuluka, Inu Mulungu wanga,

ngati mankhusu owuluka ndi mphepo.

14Monga moto umatentha nkhalango,

kapena malawi a moto kuyatsa phiri,

15kotero muwathamangitse ndi mphepo yamkuntho,

ndi kuwachititsa mantha ndi namondwe.

16Muphimbe nkhope zawo ndi manyazi

kuti adzafunefune dzina lanu Yehova.

17Achite manyazi ndi mantha nthawi zonse;

awonongeke mwa manyazi.

18Adziwe kuti Inu amene dzina lanu ndi Yehova,

ndinu nokha Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

诗篇 83:1-18

第 83 篇

祈求上帝击败仇敌

亚萨的诗。

1上帝啊,求你不要缄默无声,

一言不发。

2看啊,你的敌人在喧嚷,

恨你的人趾高气扬。

3他们用诡计害你的子民,

他们一起谋害你所疼爱的人。

4他们说:

“来吧,让我们铲除以色列

让他们亡国,被人遗忘。”

5他们串通一气,

勾结起来抵挡你。

6他们是以东人、以实玛利人、摩押人、夏甲人、

7迦巴勒人、亚扪人、亚玛力人、非利士人和泰尔人。

8亚述也跟他们勾结,

要助罗得的后代一臂之力。(细拉)

9求你对付他们,

如同对付米甸人和基顺河边的西西拉耶宾

10他们在隐·多珥灭亡,

成了地上的粪土。

11求你使他们的首领得到俄立西伊伯那样的下场,

使他们的王侯得到西巴撒慕拿那样的下场。

12他们曾说:

“让我们夺取上帝的草场吧。”

13我的上帝啊,求你把他们驱散,

如同狂风吹散尘土和碎秸。

14烈火怎样烧毁森林,

火焰怎样吞没山岭,

15求你也照样用狂风追赶他们,

用暴雨恐吓他们。

16耶和华啊,

求你使他们满面羞愧,

这样他们才会来寻求你。

17愿他们永远羞愧惊恐,

愿他们在耻辱中灭亡。

18让他们知道你是耶和华,

唯有你是普天下的至高者。