Masalimo 82 – Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero CCL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 82:1-8

Salimo 82

Salimo la Asafu.

1Mulungu akutsogolera msonkhano waukulu;

Iye akuweruza pakati pa “milungu.”

2“Mudzateteza osalungama mpaka liti,

ndi kukondera anthu oyipa?

3Tetezani anthu ofowoka ndi amasiye;

mukhazikitse ufulu wa anthu osauka ndi ozunzika.

4Landitsani anthu ofowoka ndi osowa;

apulumutseni mʼdzanja la anthu oyipa.

5“Iwo sadziwa kanthu, sazindikira kalikonse.

Amayendayenda mu mdima;

maziko onse a dziko lapansi agwedezeka.

6“Ndinati, ‘Inu ndinu Mulungu,

nonsenu ndinu ana a Wammwambamwamba.’

7Koma mudzafa ngati anthu wamba;

mudzagwa ngati wolamula wina aliyense.”

8Dzukani Inu Mulungu, weruzani dziko lapansi,

pakuti mayiko onse ndi cholowa chanu.