Masalimo 81 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 81:1-16

Salimo 81

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a gititi. Salimo la Asafu.

1Imbani mwachimwemwe kwa Mulungu mphamvu yathu;

Fuwulani mokweza kwa Mulungu wa Yakobo!

2Yambani nyimbo, imbani tambolini

imbani pangwe wolira bwino ndi zeze.

3Imbani lipenga la nyanga ya nkhosa yayimuna pa mwezi watsopano,

ndi pamene mwezi waoneka wonse, pa tsiku la phwando;

4ili ndi lamulo kwa Israeli,

langizo la Mulungu wa Yakobo.

5Iye anapereka lamulolo kwa zidzukulu za Yosefe

pamene anatuluka kulimbana ndi Igupto,

kumene tinamva chiyankhulo chimene sitinachidziwe.

6Iye akunena kuti, “Ine ndinachotsa zolemetsa pa mapewa awo;

Manja awo anamasulidwa mʼdengu.

7Pa mavuto anu munayitana ndipo ndinakulanditsani,

ndinakuyankhani kuchokera mʼmitambo ya mabingu;

ndinakuyesani pa madzi a ku Meriba.

Sela

8“Imvani anthu anga, ndipo ndidzakuchenjezani

ngati mungathe kumvetsera, Inu Israeli!

9Musadzakhale ndi mulungu wachilendo pakati panu;

musadzagwadire mulungu wina.

10Ine ndine Yehova Mulungu wanu,

amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto.

Yasamani kukamwa kwanu ndipo ndidzakudyetsani.

11“Koma anthu anga sanandimvere;

Israeli sanandigonjere.

12Kotero ndinawasiya ndi mitima yawo yosamverayo

kuti atsate zimene ankafuna.

13“Anthu anga akanangondimvera,

Israeli akanatsatira njira zanga,

14nʼkanafulumira motani kuti ndigonjetse adani awo

ndi kutembenuza mkono wanga kulimbana ndi amaliwongo!

15Iwo amene amadana ndi Yehova akanakhwinyata pamaso pake,

ndipo chilango chawo chinakakhala mpaka kalekale.

16Koma inu mukanadyetsedwa tirigu wabwino kwambiri;

ndikanakukhutitsani ndi uchi wochokera pa thanthwe.”

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

詩篇 81:1-16

第 81 篇

歌頌上帝的恩惠

亞薩的詩,交給樂長,用迦特樂器。

1要歌頌賜我們力量的上帝,

雅各的上帝歡呼。

2要唱詩,擊鼓,彈起琴瑟。

3要在我們過節的朔日和望日81·3 朔日和望日」即每月的初一和十五。吹響號角。

4這是以色列的律例,

雅各的上帝所定的法令。

5上帝攻擊埃及的時候,

約瑟立下此法度。

我在那裡聽見陌生的聲音說:

6「我卸下了你肩上的重擔,

使你的雙手不再做苦工,

7你在苦難中向我呼求,

我就拯救了你,

從雷聲隆隆的密雲中應允了你。

我在米利巴泉邊考驗你。(細拉)

8我的子民啊,

要聽我的警告。

以色列人啊,

但願你們聽從我的話。

9你們斷不可供奉別的神明,

也不可向外族的神明下拜,

10我是你們的上帝耶和華,

曾把你們帶出埃及

張開你們的口吧,

我必使你們飽足。

11我的子民卻不肯聽我的話,

以色列不願意順從我。

12因此我就任憑他們頑固不化,

為所欲為。

13但願我的子民肯聽從我,

以色列人肯遵行我的道。

14那時,我必迅速制伏他們的敵人,

伸手攻擊他們的仇敵。

15憎惡我的人要在我面前屈膝投降,永遠沉淪。

16我要以上好的麥子供養我的子民,

讓他們飽享磐石間的蜂蜜。」