Masalimo 8 – Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero CCL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 8:1-9

Salimo 8

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa gititi. Salimo la Davide.

1Inu Yehova Ambuye athu,

dzina lanu ndi la lamphamvudi pa dziko lonse lapansi!

Inu mwakhazikitsa ulemerero wanu

mʼmayiko onse akumwamba.

2Kuchokera mʼkamwa mwa ana ndi makanda,

Inu mwakhazikitsa mphamvu

chifukwa cha adani anu,

kukhazikitsa bata adani ndi anthu obwezera zoyipa.

3Pamene ndilingalira za mayiko anu akumwamba,

ntchito ya zala zanu,

mwezi ndi nyenyezi,

zimene mwaziyika pa malo ake,

4munthu ndani kuti Inu mumamukumbukira,

ndi mwana wa munthu kuti inu mumacheza naye?

5Inu munamupanga kukhala wocheperapo kusiyana ndi zolengedwa zakumwamba

ndipo mwamuveka ulemerero ndi ulemu.

6Inu munamuyika wolamulira ntchito ya manja anu;

munayika zinthu zonse pansi pa mapazi ake;

7nkhosa, mbuzi ndi ngʼombe pamodzi

ndi nyama zakuthengo,

8mbalame zamlengalenga

ndi nsomba zamʼnyanja

zonse zimene zimayenda pansi pa nyanja.

9Inu Yehova, Ambuye athu,

dzina lanu ndi lamphamvudi pa dziko lonse lapansi!