Masalimo 8 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 8:1-9

Salimo 8

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa gititi. Salimo la Davide.

1Inu Yehova Ambuye athu,

dzina lanu ndi la lamphamvudi pa dziko lonse lapansi!

Inu mwakhazikitsa ulemerero wanu

mʼmayiko onse akumwamba.

2Kuchokera mʼkamwa mwa ana ndi makanda,

Inu mwakhazikitsa mphamvu

chifukwa cha adani anu,

kukhazikitsa bata adani ndi anthu obwezera zoyipa.

3Pamene ndilingalira za mayiko anu akumwamba,

ntchito ya zala zanu,

mwezi ndi nyenyezi,

zimene mwaziyika pa malo ake,

4munthu ndani kuti Inu mumamukumbukira,

ndi mwana wa munthu kuti inu mumacheza naye?

5Inu munamupanga kukhala wocheperapo kusiyana ndi zolengedwa zakumwamba

ndipo mwamuveka ulemerero ndi ulemu.

6Inu munamuyika wolamulira ntchito ya manja anu;

munayika zinthu zonse pansi pa mapazi ake;

7nkhosa, mbuzi ndi ngʼombe pamodzi

ndi nyama zakuthengo,

8mbalame zamlengalenga

ndi nsomba zamʼnyanja

zonse zimene zimayenda pansi pa nyanja.

9Inu Yehova, Ambuye athu,

dzina lanu ndi lamphamvudi pa dziko lonse lapansi!

Hoffnung für Alle

Psalm 8:1-10

Die Krone der Schöpfung

1Ein Lied von David, zum Spiel auf der Gittit8,1 Gemeint ist ein unbekanntes Musikinstrument oder eine Melodie (so auch in Psalm 81,1; 84,1)..

2Herr, unser Herrscher!

Die ganze Welt spiegelt deine Herrlichkeit wider,

der Himmel ist Zeichen deiner Hoheit und Macht.

3Aus dem Mund der Kinder und Säuglinge lässt du dein Lob erklingen8,3 So nach der griechischen Übersetzung. Der hebräische Text lautet: hast du dir Macht bereitet..

Es ist stärker als das Fluchen deiner Feinde.

Erlahmen muss da ihre Rachsucht, beschämt müssen sie verstummen.

4Ich blicke zum Himmel und sehe, was deine Hände geschaffen haben:

den Mond und die Sterne – allen hast du ihren Platz zugewiesen.

5Was ist da schon der Mensch, dass du an ihn denkst?

Wie klein und unbedeutend ist er,

und doch kümmerst du dich um ihn.8,5 Wörtlich: und was ist der Menschensohn, dass du dich um ihn kümmerst? – Vgl. »Menschensohn« in den Sacherklärungen.

6Du hast ihn nur wenig geringer gemacht als die Engel8,6 Oder: als Gott.,

ja, mit Ruhm und Ehre hast du ihn gekrönt.

7Du hast ihm den Auftrag gegeben,

über deine Geschöpfe zu herrschen.

Alles hast du ihm zu Füßen gelegt:

8die Schafe und Rinder,

die wilden Tiere,

9die Vögel am Himmel, die Fische im Wasser

und alles, was die Meere durchzieht.

10Herr, unser Herrscher!

Die ganze Welt spiegelt deine Herrlichkeit wider.