Masalimo 79 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 79:1-13

Salimo 79

Salimo la Asafu.

1Inu Mulungu, anthu a mitundu ina alowerera mʼcholowa chanu;

ayipitsa Nyumba yanu yoyera,

asandutsa Yerusalemu kukhala bwinja.

2Iwo anapereka mitembo ya atumiki anu

kwa mbalame zamlengalenga ngati chakudya,

matupi a oyera mtima anu kwa zirombo za dziko lapansi.

3Akhetsa magazi monga madzi

kuzungulira Yerusalemu yense,

ndipo palibe wina woti ayike mʼmanda anthu akufa.

4Ife ndife chinthu chonyozeka kwa anansi athu,

choseketsa ndi cholalatiridwa kwa iwo amene atizungulira.

5Mpaka liti Inu Yehova? Kodi mudzakwiya mpaka muyaya?

Kodi mpaka liti nsanje yanu idzayaka ngati moto?

6Khuthulirani ukali wanu pa anthu a mitundu ina

amene sakudziwani Inu,

pa maufumu

amene sayitana pa dzina lanu;

7pakuti iwo ameza Yakobo

ndi kuwononga dziko lawo.

8Musatilange chifukwa cha machimo a makolo athu

chifundo chanu chibwere msanga kukumana nafe,

pakuti tili ndi chosowa chachikulu.

9Tithandizeni Inu Mulungu Mpulumutsi wathu,

chifukwa cha ulemerero wa dzina lanu;

tipulumutseni ndi kutikhululukira machimo athu

chifukwa cha dzina lanu.

10Chifukwa chiyani anthu a mitundu ina akuti,

“Ali kuti Mulungu wawo?”

Ife tikuona, zidziwike pakati pa anthu a mitundu ina

kuti mumabwezera chilango chifukwa cha magazi amene anakhetsedwa a atumiki anu.

11Kubuwula kwa anthu a mʼndende kufike pamaso panu;

ndi mphamvu ya dzanja lanu

muwasunge amene aweruzidwa kuti aphedwe.

12Mubwezere kwa anansi athu kasanu nʼkawiri

kunyoza kumene ananyoza Inu Ambuye.

13Pamenepo ife anthu anu, nkhosa za pabusa panu,

tidzakutamandani kwamuyaya,

kuchokera mʼbado ndi mʼbado

tidzafotokoza za matamando anu.

New Russian Translation

Псалтирь 79:1-20

Псалом 79

1Дирижеру хора. На мелодию «Лилия свидетельства». Псалом Асафа.

2Услышь нас, Пастырь Израиля,

Ты, Который водит Иосифа, как овец,

восседающий на херувимах, воссияй!

3Пред Ефремом, Вениамином и Манассией

пробуди силу Свою,

приди и спаси нас!

4Боже, восстанови нас!

Да воссияет лицо Твое,

и будем спасены.

5О Господь, Бог Сил,

как долго еще будешь гневаться

на молитвы Своего народа?

6Напитал Ты нас слезами, как хлебом,

напоил нас ими сполна,

7сделал нас причиной раздора соседей,

и враги наши насмехаются над нами.

8Бог Сил, восстанови нас!

Да воссияет лицо Твое,

и будем спасены.

9Из Египта Ты перенес виноградную лозу,

изгнал народы и посадил ее,

10очистил для нее место.

Принялись ее корни,

и она наполнила землю.

11Горы покрылись ее тенью,

и могучие кедры79:11 Могучие кедры – или: «кедры Божии». – ее ветвями.

12Она пустила свои ветви до моря79:12 То есть до Средиземного моря.

и побеги свои – до реки Евфрат.

13Для чего разрушил Ты ее ограды,

так что все проходящие мимо обрывают ее плоды?

14Лесной кабан подрывает ее,

и дикие звери объедают ее.

15Бог Сил, возвратись к нам!

Взгляни с неба и посмотри на нас!

И сохрани этот виноград,

16что посадила правая рука Твоя,

и сына79:16 Возможное значение: «поросль»., которого Ты сделал сильным для Себя.

17Твой виноград пожжен огнем, обсечен,

от Твоего гнева погибает народ Твой.

18Да будет рука Твоя над тем,

кто от Тебя по правую руку,

над сыном человека,

которого Ты сделал сильным для Себя.

19Тогда мы не отступим от Тебя;

возврати нас к жизни,

и мы будем призывать имя Твое.

20О Господь, Бог Сил, восстанови нас!

Да воссияет Твое лицо, и будем спасены.