Masalimo 78 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 78:1-72

Salimo 78

Ndakatulo ya Asafu.

1Inu anthu anga imvani chiphunzitso changa;

mvetserani mawu a pakamwa panga.

2Ndidzatsekula pakamwa panga mʼmafanizo,

ndidzayankhula zinthu zobisika, zinthu zakalekale

3zimene tinazimva ndi kuzidziwa,

zimene makolo athu anatiwuza.

4Sitidzabisira ana awo,

tidzafotokozera mʼbado wotsatira

ntchito zotamandika za Yehova,

mphamvu zake, ndi zozizwitsa zimene Iye wachita.

5Iye anapereka mawu wodzichitira umboni kwa Yakobo

ndi kukhazikitsa lamulo mu Israeli,

zimene analamulira makolo athu

kuphunzitsa ana awo,

6kotero kuti mʼbado wotsatira uthe kuzidziwa,

ngakhale ana amene sanabadwe,

ndi kuti iwo akafotokozere ana awonso.

7Choncho iwo adzakhulupirira Mulungu

ndipo sadzayiwala ntchito zake

koma adzasunga malamulo ake.

8Iwo asadzakhale monga makolo awo,

mʼbado wosamvera ndi wowukira,

umene mitima yake inali yosamvera Mulungu,

umene mizimu yake inali yosakhulupirika kwa Iye.

9Anthu a ku Efereimu, ngakhale ananyamula mauta,

anathawabe pa nthawi ya nkhondo;

10iwo sanasunge pangano la Mulungu

ndipo anakana kukhala mʼmoyo wotsatira lamulo lake.

11Anayiwala zimene Iye anachita,

zozizwitsa zimene anawaonetsa.

12Iyeyo anachita zodabwitsa makolo athu akuona,

mʼdziko la Igupto, mʼchigawo cha Zowani.

13Anagawa nyanja pakati ndi kudutsitsapo iwowo,

Iye anachititsa madzi kuyima chilili ngati khoma.

14Anawatsogolera ndi mtambo masana

ndi kuwala kwa moto usiku wonse.

15Iye anangʼamba miyala mʼchipululu

ndi kuwapatsa madzi ochuluka ngati a mʼnyanja zambiri;

16Anatulutsa mitsinje kuchokera mʼmingʼalu ya miyala

ndi kuyenda madzi ngati mitsinje.

17Komabe iwowo anapitiriza kumuchimwira Iye,

kuwukira Wammwambamwamba mʼchipululu.

18Ananyoza Mulungu mwadala

pomuwumiriza kuti awapatse chakudya chimene anachilakalaka.

19Iwo anayankhula motsutsana naye ponena kuti,

“Kodi Mulungu angatipatse chakudya mʼchipululu?

20Iye atamenya thanthwe

madzi anatuluka,

ndipo mitsinje inadzaza ndi madzi.

Koma iye angatipatsenso ife chakudya?

Kodi angapereke nyama kwa anthu akewa?”

21Yehova atawamva anakwiya kwambiri;

moto wake unayaka kutsutsana ndi Yakobo,

ndipo mkwiyo wake unauka kutsutsana ndi Israeli,

22pakuti iwo sanakhulupirire Mulungu

kapena kudalira chipulumutso chake.

23Komabe Iye anapereka lamulo kwa mitambo mmwamba

ndi kutsekula makomo a mayiko akumwamba;

24anagwetsa mana kuti anthu adye,

anawapatsa tirigu wakumwamba.

25Anthu anadya buledi wa angelo,

Iye anawatumizira chakudya chonse chimene akanatha kudya.

26Anamasula mphepo ya kummwera kuchokera kumwamba,

ndi kutsogolera mphepo ya kummwera mwa mphamvu zake.

27Iye anawagwetsera nyama ngati fumbi,

mbalame zowuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.

28Anazibweretsa kwa iwo mʼkati mwa misasa yawo,

kuzungulira matenti awo onse.

29Iwo anadya mpaka anatsala nazo zochuluka

pakuti Iye anawapatsa zimene anazilakalaka.

30Koma iwowo anasiya kudya chakudya anachilakalakacho,

chakudya chili mʼkamwa mwawobe,

31mkwiyo wa Mulungu unawayakira;

Iye anapha amphamvu onse pakati pawo,

kugwetsa anyamata abwino kwambiri mu Israeli.

32Ngakhale zinali chomwechi, iwo anapitirira kuchimwa;

ngakhale anaona zozizwitsa zakezo iwowo sanakhulupirirebe.

33Kotero Mulungu anachepetsa masiku awo kuti azimirire ngati mpweya.

Iye anachepetsa zaka zawo kuti zithere mʼmasautso.

34Mulungu atawapha, iwo amamufunafuna Iyeyo;

iwo ankatembenukiranso kwa Iye mwachangu.

35Ankakumbukira kuti Mulungu ndiye Thanthwe lawo,

kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye Mpulumutsi wawo.

36Komabe ankamuthyasika ndi pakamwa pawo,

kumunamiza ndi malilime awo;

37Mitima yawo sinali yokhazikika pa Iye,

iwo sanakhulupirike ku pangano lake.

38Komabe Iye anali wachifundo;

anakhululukira mphulupulu zawo

ndipo sanawawononge.

Nthawi ndi nthawi Iye anabweza mkwiyo wake

ndipo sanawutse ukali wake wonse.

39Iye anakumbukira kuti iwo anali anthu chabe,

mphepo yopita imene sibwereranso.

40Nthawi zambiri iwo ankamuwukira Iye mʼchipululu

ndi kumumvetsa chisoni mʼdziko lopanda kanthu!

41Kawirikawiri iwo ankamuyesa Mulungu;

ankamuputa Woyera wa Israeli.

42Sanakumbukire mphamvu zake,

tsiku limene Iye anawawombola kwa ozunza,

43tsiku limene Iyeyo anaonetsa poyera zizindikiro zozizwitsa zake mu Igupto,

zozizwitsa zake mʼchigawo cha Zowani.

44Iye anasandutsa mitsinje yawo kukhala magazi;

Iwo sanathe kumwa madzi ochokera mʼmitsinje yawo.

45Iye anawatumizira magulu a ntchentche zimene zinawawononga,

ndiponso achule amene anawasakaza.

46Iye anapereka mbewu zawo kwa ziwala,

zokolola zawo kwa dzombe.

47Iye anawononga mphesa zawo ndi matalala

ndiponso mitengo yawo yankhuyu ndi chisanu.

48Iye anapereka ngʼombe zawo ku matalala,

zoweta zawo ku zingʼaningʼani.

49Anakhuthula moto wa ukali wake pa iwo,

anawapsera mtima nawakwiyira nʼkuwabweretsera masautso.

Zimenezi zinali ngati gulu la angelo osakaza.

50Analolera kukwiya,

sanawapulumutse ku imfa

koma anawapereka ku mliri.

51Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto,

zipatso zoyamba kucha za mphamvu zawo mʼmatenti a Hamu

52Koma Iye anatulutsa anthu ake ngati ziweto;

anawatsogolera ngati nkhosa kudutsa mʼchipululu.

53Anawatsogolera bwinobwino kotero kuti analibe mantha

koma nyanja inamiza adani awo.

54Kotero anawafikitsa ku malire a dziko lake loyera,

ku dziko lamapiri limene dzanja lake lamanja linawatengera.

55Iye anathamangitsa mitundu ya anthu patsogolo pawo

ndipo anapereka mayiko awo kwa Aisraeli kuti akhale awo;

Iye anakhazikitsa mafuko a Israeli mʼnyumba zawo.

56Koma iwo anayesa Mulungu

ndi kuwukira Wammwambamwamba;

sanasunge malamulo ake.

57Anakhala okanika ndi osakhulupirika monga makolo awo,

anapotoka monga uta wosakhulupirika.

58Anakwiyitsa Iyeyo ndi malo awo opembedzera mafano;

anawutsa nsanje yake ndi mafano awo.

59Pamene Mulungu anamva zimenezi, anakwiya kwambiri;

Iye anakana Israeli kwathunthu.

60Anasiya nyumba ya ku Silo,

tenti imene Iyeyo anayimanga pakati pa anthu.

61Anatumiza mphamvu zake ku ukapolo,

ulemerero wake mʼmanja mwa adani.

62Anapereka anthu ake ku lupanga;

anakwiya kwambiri ndi cholowa chake.

63Moto unanyeketsa anyamata awo,

ndipo anamwali awo analibe nyimbo za ukwati;

64ansembe awo anaphedwa ndi lupanga,

ndipo amayi awo amasiye sanathe kulira.

65Kenaka Ambuye anakhala ngati akudzuka kutulo,

ngati munthu wamphamvu wofuwula chifukwa cha vinyo.

66Iye anathamangitsa adani ake;

anawachititsa manyazi ku nthawi zonse.

67Kenaka Iye anakana matenti a Yosefe,

sanasankhe fuko la Efereimu;

68Koma anasankha fuko la Yuda,

phiri la Ziyoni limene analikonda.

69Iye anamanga malo ake opatulika ngati zitunda,

dziko limene analikhazikitsa kwamuyaya.

70Anasankha Davide mtumiki wake

ndi kumuchotsa pakati pa makola ankhosa;

71kuchokera koyangʼanira nkhosa anamubweretsa

kuti akhale mʼbusa wa anthu ake, Yakobo,

wa Israeli cholowa chake.

72Ndipo Davide anawaweta ndi mtima wolungama;

ndi manja aluso anawatsogolera.

La Bible du Semeur

Psaumes 78:1-72

La main de Dieu dans l’histoire

1Méditation78.1 Signification incertaine. d’Asaph78.1 Voir note 50.1..

Mon peuple, écoute mon enseignement,

sois attentif à ce que je vais dire.

2J’énoncerai des propos instructifs,

j’évoquerai des secrets du passé78.2 Cité en Mt 13.35 d’après l’ancienne version grecque..

3Nous avons entendu et nous savons

ce que nos pères nous ont raconté,

4nous n’allons pas le cacher à leurs descendants.

Nous redirons à la génération suivante, ╵les œuvres glorieuses de l’Eternel,

les puissants actes ╵et les prodiges qu’il a accomplis.

5Il a fixé une règle en Jacob,

établi une loi en Israël,

et il a ordonné à nos ancêtres ╵d’enseigner tout cela à leurs enfants,

6afin que la génération suivante ╵puisse l’apprendre

et que les enfants qui viendront à naître,

se lèvent à leur tour ╵pour l’enseigner à leurs propres enfants,

7afin qu’ils placent leur confiance en Dieu,

qu’ils n’oublient pas comment Dieu a agi

et qu’ils observent ses commandements,

8qu’ils ne ressemblent pas à leurs ancêtres,

génération indocile et rebelle,

génération au cœur trop inconstant,

dont l’esprit n’était pas fidèle à Dieu.

9Les hommes d’Ephraïm, armés de l’arc,

ont tourné le dos, au jour du combat.

10Ils n’ont pas respecté ╵l’alliance de Dieu,

ils ont refusé de suivre sa Loi78.10 Allusion aux désobéissances d’Ephraïm (voir Jg 1.29 ; 2.2 ; 8.1 ; 9.1-5 ; 12.2)..

11Ils ont oublié ses exploits

et les hauts faits opérés sous leurs yeux.

12Devant leurs pères, Dieu avait fait des prodiges

aux champs de Tsoân78.12 Ancienne ville de la Basse-Egypte appelée aussi Tanis, située à l’est du delta du Nil, sur le chemin de l’Exode (Nb 13.22)., au pays d’Egypte.

13Il a fendu la mer, et il les a fait traverser,

il a dressé les eaux tout comme un mur78.13 Voir Ex 14.1 à 15.21..

14Il les guidait, le jour par la nuée,

et la nuit, par la lumière d’un feu78.14 Voir Ex 13.21-22..

15Il a fendu des rochers au désert,

et les a abreuvés de torrents d’eau78.15 Pour les v. 15-16, voir Ex 17.1-7 ; Nb 20.2-13..

16Du roc, il a fait jaillir des rivières,

il en a fait sortir l’eau comme un fleuve.

17Mais ils péchaient contre lui sans arrêt,

ils bravaient le Très-Haut dans le désert78.17 Par les murmures contre lui, par exemple à Mara (Ex 15.24)..

18Dans leur cœur, ils ont mis Dieu au défi

en réclamant à manger à leur goût78.18 Pour les v. 18-31, voir Ex 16.2-15 ; Nb 11.4-23, 31-34..

19Ils ont tenu des propos contre lui,

disant : « Dieu pourrait-il

dresser une table dans le désert78.19 Voir Nb 21.5. ? »

20C’est ainsi qu’il a frappé le rocher,

l’eau a coulé, des torrents ont jailli.

« Pourrait-il aussi nous donner du pain

ou procurer de la viande à son peuple ? »

21L’Eternel entendit, il s’emporta,

et un feu s’alluma contre Jacob :

sa colère éclata contre Israël,

22car ils n’avaient pas fait confiance à Dieu,

ils n’avaient pas compté sur son secours.

23Il donna ordre aux nuages d’en haut

et il ouvrit les écluses du ciel.

24Pour les nourrir, il fit pleuvoir sur eux la manne

et il leur donna le froment du ciel.

25Chacun mangea de ce pain des puissants78.25 L’ancienne version grecque a traduit : pain des anges.,

Dieu leur fournit à satiété des vivres.

26Il fit souffler le vent d’est dans le ciel,

et par sa force, il fit venir le vent du sud.

27Il fit pleuvoir de la viande sur eux, ╵aussi abondante que la poussière.

Il fit tomber une nuée d’oiseaux ╵aussi nombreux que le sable des mers.

28Il les fit tomber au milieu du camp,

autour du lieu où se dressaient leurs tentes.

29Ils en mangèrent jusqu’à satiété.

Dieu leur avait servi ce qu’ils voulaient.

30Mais leur envie n’était pas assouvie,

ils avaient encore la viande à la bouche

31que la colère de Dieu éclata contre eux.

Alors il frappa les plus vigoureux,

abattant les jeunes gens d’Israël.

32Malgré cela, ils ont péché encore,

ils n’ont pas eu foi, malgré ses prodiges78.32 Ils n’ont pas cru, en particulier, que Dieu pourrait leur donner la victoire sur les Cananéens (Nb 14). Comme au v. 22, l’incrédulité est le péché majeur des Israélites..

33Il fit s’évanouir leurs jours ╵de façon lamentable,

et terminer leurs années dans l’angoisse78.33 La génération de l’Exode fut condamnée à mourir dans le désert (Nb 14.22-23, 28-35)..

34Dieu les frappait, ils se tournaient vers lui,

ils revenaient à lui, ╵en le suppliant instamment,

35se souvenant qu’il était leur rocher,

que le Dieu très-haut était leur libérateur.

36Mais s’ils priaient, c’était pour le tromper :

les propos qu’ils lui tenaient n’étaient pas sincères,

37car leur cœur n’était pas droit envers lui,

à son alliance, ils n’étaient pas fidèles.

38Lui, cependant, rempli de compassion,

leur pardonnait au lieu de les détruire,

et, bien souvent, détournait sa colère,

ne voulant pas déchaîner toute sa fureur.

39Il considérait qu’ils étaient fragiles :

un souffle qui passe et ne revient plus.

40Que de fois ils se sont rebellés contre lui ╵dans le désert

et l’ont offensé dans les lieux arides78.40 Dans ce second cycle (v. 40-64), le psalmiste reprend les faits mentionnés dans le premier (v. 17-39). !

41A nouveau, ils mettaient Dieu au défi

et ils attristaient le Saint d’Israël.

42Car ils oubliaient son œuvre puissante :

comment il les avait sauvés de l’oppresseur,

43en Egypte, il avait fait des miracles,

et, au pays de Tsoân, des prodiges78.43 Voir note v. 12. Les v. 44-51 reprennent partiellement le thème des plaies d’Egypte.,

44canaux et rivières changés en sang,

nul ne pouvait plus s’y désaltérer78.44 Voir Ex 7.14-25.,

45mouches venimeuses qui les piquaient78.45 Voir Ex 8.16-28.,

grenouilles qui causaient leur ruine78.45 Voir Ex 7.26 à 8.11. Pour les v. 45-48, voir Ex 9.13-35.,

46leurs récoltes livrées aux sauterelles

et le fruit de leur labeur aux criquets78.46 Voir Ex 10.1-20.,

47leurs vignes ravagées par des grêlons

et leurs figuiers sous les effets du gel,

48leurs troupeaux abandonnés à la grêle

et leur bétail décimé par la foudre.

49Il déchaîna contre eux son ardente colère,

son courroux, sa fureur, et les mit en détresse,

en envoyant une armée d’anges de malheur.

50Il donna libre cours à sa colère,

et il ne leur épargna pas la mort.

Au contraire, il les livra à la peste.

51Il frappa tous les fils aînés d’Egypte,

les premiers fruits de leur virilité78.51 Autre traduction : de leur vigueur. ╵dans les logis de Cham78.51 Voir Gn 7.13 ; 10.6-20. Selon Gn 10.6, les Egyptiens étaient les descendants de Cham, l’un des fils de Noé (cf. Ps 105.23, 27 ; 106.21-22)..

52Comme un troupeau, il fit sortir son peuple

et il les conduisit dans le désert, ╵tout comme un berger conduit ses brebis78.52 Voir Ex 13.17-22..

53Il les conduisit en sécurité, ╵les préservant de tout sujet de crainte,

et la mer engloutit leurs ennemis78.53 Voir Ex 14.26-28..

54Il les fit ensuite venir ╵sur son territoire sacré,

il les conduisit jusqu’à la montagne78.54 Le mont Sion où devait être érigé le Temple (v. 68-69). ╵qu’il s’était par lui-même acquise78.54 Voir Ex 15.17..

55Il chassa devant eux des peuples étrangers,

et il attribua à chacun par le sort, ╵une part du pays en patrimoine.

Il installa les tribus d’Israël ╵dans les demeures des Cananéens.

56Mais ils ont voulu forcer la main ╵au Dieu très-haut

et ils se sont rebellés contre lui.

Ils n’ont pas respecté ses lois78.56 Voir Jg 2.11-15..

57Ils se sont dérobés ╵et se sont montrés traîtres ╵tout comme leurs ancêtres.

On ne pouvait pas leur faire confiance ╵pas plus qu’à l’arc dont la flèche dévie.

58Ils l’ont irrité avec leurs hauts lieux78.58 Lieux consacrés à des cultes idolâtres.,

par leurs idoles, ils ont provoqué ╵sa vive indignation.

59Dieu l’entendit : il se mit en colère

et il prit Israël en aversion.

60Il délaissa sa maison de Silo78.60 Ancien sanctuaire des Israélites au temps de Josué (Jos 18.1, 8 ; 21.1-2 ; Jg 18.31 ; 1 S 1.3 ; Jr 7.12) situé dans le territoire d’Ephraïm entre Béthel et Sichem (Jg 21.12), à une quarantaine de kilomètres au nord de Jérusalem. Le coffre sacré y fut déposé jusqu’au temps du jeune Samuel (1 S 4.3). La ville fut sans doute détruite par les Philistins (d’après les fouilles archéologiques : vers 1050 av. J.-C.).,

le tabernacle, ╵où il résidait parmi les humains.

61Il laissa partir en captivité ╵le coffre sacré, trône de sa force,

et livra aux ennemis sa splendeur78.61 Voir 1 S 4.4-22..

62En colère contre les siens,

il abandonna son peuple à l’épée.

63Le feu consuma ses adolescents,

et l’on ne chanta plus l’éloge ╵de ses jeunes mariées78.63 Il s’agit des chants nuptiaux où les jeunes filles étaient célébrées. Cela signifie qu’elles n’eurent plus l’occasion de se marier parce que les jeunes gens avaient été tués dans les batailles (cf. Es 3.25 à 4.1)..

64Ses prêtres périrent sous les coups de l’épée,

ses veuves n’eurent pas droit à des larmes78.64 Obligées de fuir, elles ne purent pas pleurer leurs morts dans des cérémonies funèbres traditionnelles (voir Jb 27.15)..

65Mais, tout à coup, l’Eternel intervint,

tel un dormeur sortant de sa torpeur,

tel un guerrier exalté par le vin.

66Il frappa ses ennemis à revers,

il les couvrit d’une honte éternelle.

67Il écarta la maison de Joseph78.67 Elle est constituée par les tribus d’Ephraïm et de Manassé (Gn 48.1) auxquelles Jacob a conféré le droit d’aînesse, mais que Dieu a écartées de cette position.,

ne choisit pas la tribu d’Ephraïm.

68Mais il choisit la tribu de Juda,

le mont Sion qu’il prit en affection.

69C’est là qu’il édifia son sanctuaire ╵tels les lieux élevés

comme la terre établie pour toujours.

70Il a choisi son serviteur David

et il l’a tiré de ses bergeries78.70 Pour les v. 70-71, voir 1 S 16.11-13 ; 25.7-8 ; 1 Ch 17.7..

71Il l’a pris du milieu de ses brebis

pour qu’il soit berger de Jacob, son peuple,

et d’Israël qui est sa possession.

72David fut pour eux un berger intègre

qui les guida d’une main avisée.