Masalimo 77 – CCL & NIVUK

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 77:1-20

Salimo 77

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Asafu.

1Ndinafuwulira Mulungu kupempha thandizo;

ndinafuwula mokweza kwa Mulungu kuti anditcherere khutu.

2Pamene ndinali pa masautso ndinafunafuna Ambuye;

usiku ndinatambasula manja mosalekeza

ndipo moyo wanga unakana kutonthozedwa.

3Ndinakumbukira Inu Mulungu, ndipo ndinabuwula;

ndinasinkhasinkha ndipo mzimu wanga unalefuka.

Sela

4Munagwira zikope zanga kuti ndisagone

ndipo ndinavutika kwambiri kuti ndiyankhule.

5Ndinaganizira za masiku akale,

zaka zamakedzana;

6Ndinakumbukira nyimbo zanga usiku.

Mtima wanga unasinkhasinkha ndipo mzimu wanga unafunsa kuti,

7“Kodi Ambuye adzatikana mpaka muyaya?

Kodi Iwo sadzaonetsanso kukoma mtima kwawo?

8Kodi Chikondi chake chosatha chija chatheratu?

Kodi malonjezo ake alephera nthawi yonse?

9Kodi Mulungu wayiwala kukhala wokoma mtima?

Kodi mu mkwiyo wake waleka chifundo chake?”

10Ndipo ndinaganiza, “Pa izi ine ndidzapemphanso:

zaka za dzanja lamanja la Wammwambamwamba.

11Ine ndidzakumbukira ntchito za Yehova;

Ine ndidzakumbukira zodabwitsa zanu za kalekale.

12Ndidzakumbukira ntchito zanu

ndi kulingalira zodabwitsa zanu.”

13Njira zanu Mulungu ndi zoyera.

Kodi ndi mulungu uti ali wamkulu kuposa Mulungu wathu?

14Inu ndinu Mulungu wochita zodabwitsa;

Mumaonetsera mphamvu yanu pakati pa mitundu ya anthu.

15Ndi dzanja lanu lamphamvu munawombola anthu anu,

zidzukulu za Yakobo ndi Yosefe.

Sela

16Madzi anakuonani Mulungu,

madzi anakuonani ndipo anachita mantha;

nyanja yozama inakomoka.

17Mitambo inakhuthula madzi ake pansi,

mu mlengalenga munamveka mabingu;

mivi yanu inawuluka uku ndi uku.

18Bingu lanu linamveka mʼmphepo ya kamvuluvulu,

mphenzi yanu inawalitsa dziko lonse;

dziko lapansi linanjenjemera ndi kugwedezeka.

19Njira yanu inadutsa pa nyanja,

njira yanu inadutsa pa madzi amphamvu,

ngakhale zidindo za mapazi anu sizinaoneke.

20Inu munatsogolera anthu anu ngati gulu la nkhosa

mwa dzanja la Mose ndi Aaroni.

New International Version – UK

Psalms 77:1-20

Psalm 77In Hebrew texts 77:1-20 is numbered 77:2-21.

For the director of music. For Jeduthun. Of Asaph. A psalm.

1I cried out to God for help;

I cried out to God to hear me.

2When I was in distress, I sought the Lord;

at night I stretched out untiring hands,

and I would not be comforted.

3I remembered you, God, and I groaned;

I meditated, and my spirit grew faint.77:3 The Hebrew has Selah (a word of uncertain meaning) here and at the end of verses 9 and 15.

4You kept my eyes from closing;

I was too troubled to speak.

5I thought about the former days,

the years of long ago;

6I remembered my songs in the night.

My heart meditated and my spirit asked:

7‘Will the Lord reject for ever?

Will he never show his favour again?

8Has his unfailing love vanished for ever?

Has his promise failed for all time?

9Has God forgotten to be merciful?

Has he in anger withheld his compassion?’

10Then I thought, ‘To this I will appeal:

the years when the Most High stretched out his right hand.

11I will remember the deeds of the Lord;

yes, I will remember your miracles of long ago.

12I will consider all your works

and meditate on all your mighty deeds.’

13Your ways, God, are holy.

What god is as great as our God?

14You are the God who performs miracles;

you display your power among the peoples.

15With your mighty arm you redeemed your people,

the descendants of Jacob and Joseph.

16The waters saw you, God,

the waters saw you and writhed;

the very depths were convulsed.

17The clouds poured down water,

the heavens resounded with thunder;

your arrows flashed back and forth.

18Your thunder was heard in the whirlwind,

your lightning lit up the world;

the earth trembled and quaked.

19Your path led through the sea,

your way through the mighty waters,

though your footprints were not seen.

20You led your people like a flock

by the hand of Moses and Aaron.