Masalimo 75 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 75:1-10

Salimo 75

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe, potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Salimo la Asafu. Nyimbo.

1Tikuthokoza Inu Mulungu,

tikuthokoza, pakuti dzina lanu lili pafupi nafe,

anthutu amafotokoza za ntchito zanu zodabwitsa.

2Mumati, “Ine ndimayika nthawi yoyenera,

ndine amene ndimaweruza mwachilungamo.

3Pamene dziko lapansi ndi anthu ake onse anjenjemera,

ndine amene ndimagwiriziza mizati yake molimba.

Sela

4Kwa odzitama ndikuti, ‘Musadzitamenso,’

ndipo kwa oyipa, ‘Musatukulenso nyanga zanu.

5Musatukule nyanga zanu motsutsana ndi kumwamba;

musayankhule ndi khosi losololoka.’ ”

6Kugamula milandu sikuchokera kummawa kapena kumadzulo

kapena ku chipululu.

7Koma ndi Mulungu amene amaweruza:

Iyeyo amatsitsa wina, nakwezanso wina.

8Mʼdzanja la Yehova muli chikho

chodzaza ndi vinyo wochita thovu, wosakanizidwa ndi zokometsera;

Iye amamutsanulira pansi ndipo onse oyipa a dziko lapansi

amamwa ndi senga zake zonse.

9Kunena za ine, ndidzalengeza izi kwamuyaya;

ndidzayimba matamando kwa Mulungu wa Yakobo.

10Ndidzadula nyanga za onse oyipa

koma nyanga za olungama zidzakwezedwa.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

詩篇 75:1-10

第 75 篇

上帝是審判者

亞薩的詩,交給樂長,調用「休要毀壞」。

1上帝啊,

我們稱謝你,我們稱謝你,

因為你與我們同在。

人們都述說你奇妙的作為。

2你說:「我已定好時間,

我必秉公審判。

3大地震動,世人戰抖的時候,

是我使地的根基穩固。(細拉)

4我警告狂妄人不要再狂傲,

告誡惡人不要再張狂。

5不要再狂妄自大,

不要說話傲氣沖天。」

6人的尊貴不是來自東方,

不是來自西方,

也不是來自曠野。

7決定人尊貴的是上帝:

祂擢升這個,貶抑那個。

8耶和華手中的杯裡盛滿泛著泡沫、精工調製的怒酒。

祂倒出怒酒,讓世上的惡人喝得一滴不剩。

9我要永遠宣揚祂的作為,

我要頌讚雅各的上帝。

10上帝必剷除惡人的勢力,

使義人充滿力量。