Masalimo 73 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 73:1-28

BUKU LACHITATU

Masalimo 73–89

Salimo 73

Salimo la Asafu.

1Mulungu ndi wabwino ndithu kwa Israeli,

kwa iwo amene ndi oyera mtima.

2Koma kunena za ine, mapazi anga anali pafupi kuterereka;

ndinatsala pangʼono kugwa.

3Pakuti ndinkachitira nsanje odzitamandira,

pamene ndinaona mtendere wa anthu oyipa.

4Iwo alibe zosautsa;

matupi awo ndi athanzi ndi amphamvu.

5Saona mavuto monga anthu ena;

sazunzika ngati anthu ena onse.

6Nʼchifukwa chake kunyada kuli monga mkanda wa mʼkhosi mwawo;

amadziveka chiwawa.

7Mʼmitima yawo yokhota mumachokera zolakwa;

zoyipa zochokera mʼmaganizo awo sizidziwa malire.

8Iwowo amanyogodola ndi kumayankhula zoyipa;

mwa kudzikuza kwawo amaopseza ena nʼkumati, “Tikuponderezani.”

9Pakamwa pawo pamayankhula monyoza Mulungu kumwamba

ndipo lilime lawo limayenda pa dziko lapansi.

10Nʼchifukwa chake anthu awo amapita kwa iwowo

ndi kumwa madzi mochuluka.

11Iwo amati, “Kodi Mulungu angadziwe bwanji?

Kodi Wammwambamwamba angadziwe kalikonse?”

12Umu ndi mmene oyipa alili;

nthawi zonse ali pabwino ndipo chuma chawo chimachulukirachulukira.

13Ndithudi ine ndawusunga pachabe mtima wanga woyera;

pachabe ndasamba mʼmanja mwanga mwa kusalakwa kwanga.

14Tsiku lonse ndapeza mavuto;

ndakhala ndi kulangidwa mmawa uliwonse.

15Ndikanati, “Ndidzayankhula motere,”

ndikanachita chosakhulupirika kwa ana anu.

16Pamene ndinayesa kuti ndimvetse zonsezi,

zinandisautsa kwambiri

17kufikira nditalowa mʼmalo opatulika a Mulungu;

pamenepo ndinamvetsa mathero awo.

18Zoonadi Inu munawayika pa malo woterera;

Mumawagwetsa pansi kuti awonongeke.

19Mwamsangamsanga iwo amawonongedwa,

amasesedwa kwathunthu ndi mantha!

20Monga loto pamene wina adzuka,

kotero pamene Inu muuka, Inu Ambuye,

mudzawanyoza ngati maloto chabe.

21Pamene mtima wanga unasautsidwa

ndi kuwawidwa mu mzimu mwanga,

22ndinali wopusa ndi wosadziwa;

ndinali chirombo chopanda nzeru pamaso panu.

23Komabe ineyo ndili ndi Inu nthawi zonse;

mumandigwira dzanja langa lamanja.

24Inu mumanditsogolera ndi malangizo anu

ndipo pambuyo pake mudzanditenga ku ulemerero.

25Kodi kumwamba ndili ndi yani kupatula Inu?

Ndipo dziko lapansi lilibe chilichonse chimene ndimachilakalaka koposa Inuyo.

26Thupi ndi mtima wanga zitha kufowoka,

koma Mulungu ndiye mphamvu ya mtima wanga

ndi cholandira changa kwamuyaya.

27Iwo amene ali kutali ndi Inu adzawonongeka;

Inu mumawononga onse osakhulupirika pamaso panu.

28Koma kunena za Ine ndi kwabwino kukhala pafupi ndi Mulungu.

Ndatsimikiza kuti Ambuye Yehova ndiwo pothawirapo panga

ndipo ndidzalalika ntchito zanu zonse.

New Russian Translation

Псалтирь 73:1-23

Псалом 73

1Наставление Асафа.

О Боже, зачем Ты навсегда отверг нас?

Почему гнев Твой возгорелся на овец пастбищ Твоих?

2Вспомни народ, который Ты приобрел с давних времен,

который Ты искупил, чтобы он был Твоим наследием;

вспомни гору Сион, на которой Ты обитаешь.

3Направь Свои шаги к вековым развалинам –

все разрушил враг во святилище!

4Враги Твои рычали посреди собрания Твоего,

установили там свои знамена.

5Они размахивали своими топорами,

как дровосеки в густом лесу,

6без остатка разрушили резные стены

их секиры и бердыши.

7Они сожгли святилище Твое дотла,

осквернили они жилище имени Твоего.

8Решили они в сердце своем: «Уничтожим их полностью» –

и по всей стране сожгли все места,

где поклонялись мы Тебе.

9Знамений не видят наши глаза,

и не осталось пророков,

нет никого, кто знал бы,

когда этому наступит конец.

10О Боже, как долго еще будет враг глумиться,

и вечно ли будет противник оскорблять Твое имя?

11Почему Ты убираешь назад Свою руку, Свою правую руку?

Извлеки ее на них и порази их!

12Бог, мой Царь от начала,

Ты принес спасение на землю.

13Ты разделил Своей силою море,

Ты сокрушил головы морских чудовищ.

14Ты сокрушил головы Левиафана73:14 Левиафан – морское чудовище, символ враждебных Богу сил. См. Иов 40:20–41:26.,

жителям пустынь отдав его в пищу.

15Ты иссек источник и поток,

Ты иссушил бегущие реки.

16День и ночь – Твои; Ты создал солнце и луну.

17Ты определил границы земли,

сотворил лето и зиму.

18Вспомни, Господи, как глумится враг

и как безумный народ оскорбляет Твое имя.

19Не отдавай зверям душу Твоей горлицы;

жизней Твоих страдальцев не забудь никогда.

20Взгляни на Свой завет,

потому что насилие во всех темных уголках земли.

21Да не возвратится угнетенный с позором;

пусть бедный и нищий восхвалят Твое имя.

22Восстань, Боже, и защити Свое дело;

вспомни, как глупец оскорбляет Тебя целый день.

23Не забудь крика Своих врагов,

шума, который непрестанно поднимают противники Твои.