Masalimo 73 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 73:1-28

BUKU LACHITATU

Masalimo 73–89

Salimo 73

Salimo la Asafu.

1Mulungu ndi wabwino ndithu kwa Israeli,

kwa iwo amene ndi oyera mtima.

2Koma kunena za ine, mapazi anga anali pafupi kuterereka;

ndinatsala pangʼono kugwa.

3Pakuti ndinkachitira nsanje odzitamandira,

pamene ndinaona mtendere wa anthu oyipa.

4Iwo alibe zosautsa;

matupi awo ndi athanzi ndi amphamvu.

5Saona mavuto monga anthu ena;

sazunzika ngati anthu ena onse.

6Nʼchifukwa chake kunyada kuli monga mkanda wa mʼkhosi mwawo;

amadziveka chiwawa.

7Mʼmitima yawo yokhota mumachokera zolakwa;

zoyipa zochokera mʼmaganizo awo sizidziwa malire.

8Iwowo amanyogodola ndi kumayankhula zoyipa;

mwa kudzikuza kwawo amaopseza ena nʼkumati, “Tikuponderezani.”

9Pakamwa pawo pamayankhula monyoza Mulungu kumwamba

ndipo lilime lawo limayenda pa dziko lapansi.

10Nʼchifukwa chake anthu awo amapita kwa iwowo

ndi kumwa madzi mochuluka.

11Iwo amati, “Kodi Mulungu angadziwe bwanji?

Kodi Wammwambamwamba angadziwe kalikonse?”

12Umu ndi mmene oyipa alili;

nthawi zonse ali pabwino ndipo chuma chawo chimachulukirachulukira.

13Ndithudi ine ndawusunga pachabe mtima wanga woyera;

pachabe ndasamba mʼmanja mwanga mwa kusalakwa kwanga.

14Tsiku lonse ndapeza mavuto;

ndakhala ndi kulangidwa mmawa uliwonse.

15Ndikanati, “Ndidzayankhula motere,”

ndikanachita chosakhulupirika kwa ana anu.

16Pamene ndinayesa kuti ndimvetse zonsezi,

zinandisautsa kwambiri

17kufikira nditalowa mʼmalo opatulika a Mulungu;

pamenepo ndinamvetsa mathero awo.

18Zoonadi Inu munawayika pa malo woterera;

Mumawagwetsa pansi kuti awonongeke.

19Mwamsangamsanga iwo amawonongedwa,

amasesedwa kwathunthu ndi mantha!

20Monga loto pamene wina adzuka,

kotero pamene Inu muuka, Inu Ambuye,

mudzawanyoza ngati maloto chabe.

21Pamene mtima wanga unasautsidwa

ndi kuwawidwa mu mzimu mwanga,

22ndinali wopusa ndi wosadziwa;

ndinali chirombo chopanda nzeru pamaso panu.

23Komabe ineyo ndili ndi Inu nthawi zonse;

mumandigwira dzanja langa lamanja.

24Inu mumanditsogolera ndi malangizo anu

ndipo pambuyo pake mudzanditenga ku ulemerero.

25Kodi kumwamba ndili ndi yani kupatula Inu?

Ndipo dziko lapansi lilibe chilichonse chimene ndimachilakalaka koposa Inuyo.

26Thupi ndi mtima wanga zitha kufowoka,

koma Mulungu ndiye mphamvu ya mtima wanga

ndi cholandira changa kwamuyaya.

27Iwo amene ali kutali ndi Inu adzawonongeka;

Inu mumawononga onse osakhulupirika pamaso panu.

28Koma kunena za Ine ndi kwabwino kukhala pafupi ndi Mulungu.

Ndatsimikiza kuti Ambuye Yehova ndiwo pothawirapo panga

ndipo ndidzalalika ntchito zanu zonse.

New International Reader’s Version

Psalm 73:1-28

Book III

Psalms 73–89

Psalm 73

A psalm of Asaph.

1God is truly good to Israel.

He is good to those who have pure hearts.

2But my feet had almost slipped.

I had almost tripped and fallen.

3I saw that proud and sinful people were doing well.

And I began to long for what they had.

4They don’t have any troubles.

Their bodies are healthy and strong.

5They don’t have the problems most people have.

They don’t suffer as other people do.

6Their pride is like a necklace.

They put on meanness as if it were their clothes.

7Many sins come out of their hard and stubborn hearts.

There is no limit to the evil things they can think up.

8They laugh at others and speak words of hatred.

They are proud. They warn others about the harm they can do to them.

9They brag as if they owned heaven itself.

They talk as if they controlled the earth.

10So people listen to them.

They lap up their words like water.

11They say, “How would God know what we’re doing?

Does the Most High God know anything?”

12Here is what sinful people are like.

They don’t have a care in the world.

They keep getting richer and richer.

13It seems as if I have kept my heart pure for no reason.

It didn’t do me any good to wash my hands

to show that I wasn’t guilty of doing anything wrong.

14Day after day I’ve been in pain.

God has punished me in a new way every morning.

15What if I had talked like that?

Then I wouldn’t have been faithful to God’s children.

16I tried to understand it all.

But it was more than I could handle.

17It troubled me until I entered God’s temple.

Then I understood what will finally happen to bad people.

18God, I’m sure you will make them slip and fall.

You will throw them down and destroy them.

19It will happen very suddenly.

A terrible death will take them away completely.

20A dream goes away when a person wakes up.

Lord, it will be like that when you rise up.

It will be as if those people were only a dream.

21At one time my heart was sad

and my spirit was bitter.

22I didn’t have any sense. I didn’t know anything.

I acted like a wild animal toward you.

23But I am always with you.

You hold me by my right hand.

24You give me wise advice to guide me.

And when I die, you will take me away

into the glory of heaven.

25I don’t have anyone in heaven but you.

I don’t want anything on earth besides you.

26My body and my heart may grow weak.

God, you give strength to my heart.

You are everything I will ever need.

27Those who don’t want anything to do with you will die.

You destroy all those who aren’t faithful to you.

28But I am close to you. And that’s good.

Lord and King, I have made you my place of safety.

I will talk about everything you have done.