Salimo 72
Salimo la Solomoni.
1Patsani mwana wa mfumu nzeru zanu zoweruzira mwa chilungamo,
Inu Mulungu mupatseni mwana wa mfumu chilungamo chanu.
2Iye adzaweruza anthu anu mwachilungamo,
anthu anu ozunzika mosakondera.
3Mapiri adzabweretsa chuma kwa anthu anu,
timapiri tidzabweretsa zipatso zachilungamo.
4Iye adzateteza ozunzika pakati pa anthu
ndi kupulumutsa ana a anthu osowa;
adzaphwanya ozunza anzawo.
5Adzakhala ndi moyo pa mibado yonse,
nthawi zonse pamene dzuwa ndi mwezi zikuwala.
6Iye adzakhala kugwa kwa mvula pa minda yolimidwa
ngati mivumbi yothirira dziko lapansi.
7Mʼmasiku a munthu wolungama adzakhazikika;
chuma chidzachuluka mpaka mwezi utaleka kuwala.
8Iye adzalamulira kuchokera ku nyanja ina mpaka ku nyanja ina
ndiponso kuchokera ku mtsinje mpaka ku malekezero a dziko lapansi.
9Mafuko a mʼchipululu adzawerama pamaso pake
ndipo adani ake adzanyambita fumbi.
10Mafumu a ku Tarisisi ndi a ku zilumba zakutali
adzabweretsa mitulo kwa iye,
mafumu a ku Seba ndi Seba
adzapereka mphatso kwa iyeyo.
11Mafumu onse adzamuweramira
ndipo mitundu yonse idzamutumikira.
12Pakuti iye adzawombola wosowa amene akulira,
wozunzika amene alibe wina womuthandiza.
13Iye adzachitira chifundo anthu ofowoka ndi anthu osowa
ndi kupulumutsa osowa ku imfa.
14Iye adzalanditsa iwo ku mazunzo ndi chiwawa
pakuti magazi awo ndi amtengo wapatali pamaso pake.
15Iye akhale ndi moyo wautali;
golide ochokera ku Seba apatsidwe kwa iye.
Anthu amupempherere nthawi zonse
ndi kumudalitsa tsiku lonse.
16Mulole kuti tirigu achuluke mʼdziko lonse;
pamwamba pa mapiri pakhale tirigu.
Zipatso zake zichuluke ngati za ku Lebanoni;
zichuluke ngati udzu wakuthengo
17Dzina lake likhazikike kwamuyaya,
lipitirire kukhala monga momwe limakhalira dzuwa.
Mitundu yonse idzadalitsika kudzera mwa iye
ndipo iwo adzamutcha iye wodala.
18Matamando akhale kwa Yehova Mulungu, Mulungu wa Israeli
amene Iye yekha amachita ntchito zodabwitsa.
19Matamando akhale ku dzina lake laulemerero kwamuyaya
dziko lonse lapansi lidzaze ndi ulemerero wake.
Ameni ndi Ameni.
20Uku ndiko kumaliza kwa mapemphero a Davide mwana wa Yese.
왕을 위한 기도
(솔로몬을 위해 지은 시)
1하나님이시여,
왕에게 주의 판단력을
주시고
왕의 아들이
주의 의로운 길을 걷게 하소서.
2그러면 그가 주의 백성을
바르게 판단하며
가난하고 고통당하는 주의 백성을
공정하게 다스릴 것입니다.
3의로운 통치를 하게 될 때
산과 들도 백성들에게
번영을 주리라.
4그가 백성들 가운데
고통당하는 자들을 옹호하고
가난한 자들의 자녀들을 구하며
학대하는 자들을 꺾을 것이다.
5해와 달이 비치는 한
가난하고 고통당하는 자들이
여호와를 두려운
마음으로 섬기리라.
6왕은 풀을 벤 들에 내리는
비와 같고
땅을 적시는 소나기 같아서
7그가 통치하는 동안에
의로운 자들이 번성하고
달이 다할 때까지
72:7 또는 ‘평강의 풍성함이’번영이 지속되기를 바라노라.
8그가 바다에서 바다까지,
유프라테스강에서 땅 끝까지
다스릴 것이니
9광야에 사는 자들이
그 앞에 허리를 굽히고
그의 원수들이
그에게 굴복할 것이다.
10다시스와 섬나라 왕들이
그에게 조공을 바치고
스바와 시바 왕들이 예물을 드리며
11세상의 모든 왕들이
그 앞에 절하고
모든 민족이 그를 섬기리라.
12그는 가난한 자가
부르짖을 때 구하고
도울 자가 없는
고통당하는 자들을 건질 것이다.
13그는 약하고 가난한 자들을
불쌍히 여겨
그들의 생명을 구하고
14그들을 압박과 폭력에서
건질 것이니
그에게는 그들의 생명이
소중함이라.
15그가 장수하기를 바라노라.
사람들이 그에게
스바의 금을 드리며
그를 위해 항상 기도하고
종일 찬송하기를 바라노라.
16산꼭대기까지
온 땅에 곡식이 풍성하고
그 열매가 레바논의 열매 같으며
백성들은
들의 풀같이 번성하리라.
17그의 이름이 영원히 남고
그의 명성이 해처럼
지속되기를 바라노라.
모든 민족이 그를 통해
복을 받을 것이니
그들이 그를
복되다 하리라.
18이스라엘의 하나님
여호와를 찬양하라.
그분만이
놀라운 일을 행하신다.
19그의 영광스러운 이름을
영원히 찬양하라.
온 땅에 그의 영광이
충만하기를 원하노라.
아멘! 아멘!
20이것으로 이새의 아들
다윗의 기도가 끝난다.