Masalimo 72 – CCL & HTB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 72:1-20

Salimo 72

Salimo la Solomoni.

1Patsani mwana wa mfumu nzeru zanu zoweruzira mwa chilungamo,

Inu Mulungu mupatseni mwana wa mfumu chilungamo chanu.

2Iye adzaweruza anthu anu mwachilungamo,

anthu anu ozunzika mosakondera.

3Mapiri adzabweretsa chuma kwa anthu anu,

timapiri tidzabweretsa zipatso zachilungamo.

4Iye adzateteza ozunzika pakati pa anthu

ndi kupulumutsa ana a anthu osowa;

adzaphwanya ozunza anzawo.

5Adzakhala ndi moyo pa mibado yonse,

nthawi zonse pamene dzuwa ndi mwezi zikuwala.

6Iye adzakhala kugwa kwa mvula pa minda yolimidwa

ngati mivumbi yothirira dziko lapansi.

7Mʼmasiku a munthu wolungama adzakhazikika;

chuma chidzachuluka mpaka mwezi utaleka kuwala.

8Iye adzalamulira kuchokera ku nyanja ina mpaka ku nyanja ina

ndiponso kuchokera ku mtsinje mpaka ku malekezero a dziko lapansi.

9Mafuko a mʼchipululu adzawerama pamaso pake

ndipo adani ake adzanyambita fumbi.

10Mafumu a ku Tarisisi ndi a ku zilumba zakutali

adzabweretsa mitulo kwa iye,

mafumu a ku Seba ndi Seba

adzapereka mphatso kwa iyeyo.

11Mafumu onse adzamuweramira

ndipo mitundu yonse idzamutumikira.

12Pakuti iye adzawombola wosowa amene akulira,

wozunzika amene alibe wina womuthandiza.

13Iye adzachitira chifundo anthu ofowoka ndi anthu osowa

ndi kupulumutsa osowa ku imfa.

14Iye adzalanditsa iwo ku mazunzo ndi chiwawa

pakuti magazi awo ndi amtengo wapatali pamaso pake.

15Iye akhale ndi moyo wautali;

golide ochokera ku Seba apatsidwe kwa iye.

Anthu amupempherere nthawi zonse

ndi kumudalitsa tsiku lonse.

16Mulole kuti tirigu achuluke mʼdziko lonse;

pamwamba pa mapiri pakhale tirigu.

Zipatso zake zichuluke ngati za ku Lebanoni;

zichuluke ngati udzu wakuthengo

17Dzina lake likhazikike kwamuyaya,

lipitirire kukhala monga momwe limakhalira dzuwa.

Mitundu yonse idzadalitsika kudzera mwa iye

ndipo iwo adzamutcha iye wodala.

18Matamando akhale kwa Yehova Mulungu, Mulungu wa Israeli

amene Iye yekha amachita ntchito zodabwitsa.

19Matamando akhale ku dzina lake laulemerero kwamuyaya

dziko lonse lapansi lidzaze ndi ulemerero wake.

Ameni ndi Ameni.

20Uku ndiko kumaliza kwa mapemphero a Davide mwana wa Yese.

Het Boek

Psalmen 72:1-20

1Een psalm van Salomo.

O God, doe recht aan de koning

en toon uw rechtvaardigheid aan zijn zoon.

2Laat hij rechtvaardig over uw volk regeren

en zuiver rechtspreken, ook over de armen.

3Laten de bergen de vrede voor het volk aandragen

en de heuvels spreken over de zuivere rechtspraak.

4Laat de koning de armsten uit de samenleving

hun rechten geven en hen werkelijk helpen.

Maar laat hij de onderdrukker veroordelen.

5Laat ieder,

zolang de zon schijnt

en de maan ʼs nachts aan de hemel staat,

ontzag voor U hebben.

Van generatie op generatie.

6Laat de koning zijn als een milde regenbui

die neerdaalt op de akkers en de aarde bevochtigt.

7Laat onder zijn regering

de oprechte mens tot bloei komen

en laat er altijd vrede zijn.

8Laat hem heersen van oost tot west

en van noord tot zuid.

9Laten de nomaden in de woestijn

zich voor hem buigen

en zijn tegenstanders

voorover in het stof vallen.

10Laten de koningen uit Tarsis en de andere buurlanden

hem geschenken brengen.

De koningen van Seba en Saba

moeten hem belasting betalen.

11Laten alle koningen

zich voor hem buigen

en alle volken

aan hem onderworpen zijn.

12De koning zal zeker

de arme die om hulp roept, bevrijden

en ook de armzalige

die door niemand wordt geholpen.

13Hij zal zich ontfermen

over ieder die klein en arm is,

hen allen nabij zijn en bevrijden.

14Elke vorm van onderdrukking en geweld

zal hij voor hen wegnemen.

Zij zullen kostbaar zijn in zijn ogen.

15De koning zal grote voorspoed kennen.

Men zal hem goud uit Seba brengen.

Ook zal men voor hem bidden, dag in, dag uit.

De hele dag door zal men hem het goede toewensen.

16Het land zal overvloedige graanoogsten kennen.

Op de bergen bloeien de gewassen met rijke vruchten,

net als op de Libanon.

De mensen in de stad bloeien

als de gewassen op aarde.

17De naam van de koning zal niet worden vergeten.

Zolang de zon haar licht op aarde geeft,

zal men zijn naam kennen.

Laten alle volken

elkaar het beste wensen met zijn naam en hem eren.

18Alle lof en eer is voor de Here God,

de God van Israël, tot in eeuwigheid.

Alleen Hij doet wonderen.

19Voor eeuwig zal zijn heerlijke naam

worden geloofd en geprezen.

Laat de hele aarde vol zijn met zijn aanwezigheid.

Ja, laat het zo zijn. Amen.

20Hier eindigen de gebeden van David, de zoon van Isaï.