Masalimo 71 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 71:1-24

Salimo 71

1Mwa Inu Yehova ine ndathawiramo;

musalole kuti ndichititsidwe manyazi.

2Mundilanditse ndi kundipulumutsa mwa chilungamo chanu,

mutchere khutu lanu ndi kundipulumutsa.

3Mukhale thanthwe langa lothawirapo,

kumene ine nditha kupita nthawi zonse;

lamulani kuti ndipulumuke,

pakuti Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa.

4Landitseni Inu Mulungu wanga, kuchoka mʼdzanja la oyipa,

kuchoka mʼdzanja la oyipa ndi anthu ankhanza.

5Pakuti Inu mwakhala chiyembekezo changa, Inu Ambuye Wamphamvuzonse,

chilimbikitso changa kuyambira ndili mwana.

6Kuyambira pamene ndinabadwa, ndakhala ndikudalira Inu;

Inu munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga,

ndipo ndidzakupembedzani nthawi zonse.

7Ine ndakhala chinthu chodabwitsa kwa anthu ambiri

koma Inu ndinu wonditchinjiriza wamphamvu.

8Pakamwa panga padzaza ndi matamando anu,

kulengeza ulemerero wanu tsiku lonse.

9Musanditaye pamene ndakalamba;

musandisiye pamene mphamvu zanga zatha.

10Pakuti adani anga ayankhula motsutsana nane;

iwo amene amadikira kuti andiphe amapangana pamodzi.

11Iwo amati, “Mulungu wamusiya;

mutsatireni ndi kumugwira,

pakuti palibe amene adzamupulumutse.”

12Musakhale kutali ndi ine Inu Mulungu,

bwerani msanga, Inu Mulungu wanga; thandizeni.

13Ondineneza anga awonongeke mwa manyazi,

iwo amene akufuna kundipweteka

avale chitonzo ndi manyazi.

14Koma ine ndidzakhala ndi chiyembekezo mwa Inu nthawi zonse,

ndidzakutamandani mowirikizawirikiza.

15Pakamwa panga padzafotokoza za chilungamo chanu,

za chipulumutso chanu tsiku lonse,

ngakhale sindikudziwa muyeso wake.

16Ndidzabwera ndi kulengeza za machitidwe amphamvu zanu Inu Ambuye Wamphamvuzonse.

Ndidzalengeza chilungamo chanu, chanu chokha.

17Kuyambira ubwana wanga, Inu Mulungu mwakhala mukundiphunzitsa,

ndipo mpaka lero ine ndikulengeza za ntchito zanu zodabwitsa

18Ngakhale pamene ndakalamba ndipo imvi zili mbuu

musanditaye Inu Mulungu,

mpaka nditalengeza mphamvu zanu

kwa mibado yonse yakutsogolo.

19Mphamvu zanu ndi kulungama kwanu zimafika mpaka kumwambamwamba.

Ndani wofanana nanu Inu Mulungu,

amene mwachita zazikulu?

20Ngakhale mwandionetsa mavuto

ambiri owawa,

mudzabwezeretsanso moyo wanga;

kuchokera kunsi kwa dziko lapansi,

mudzandiukitsanso.

21Inu mudzachulukitsa ulemu wanga

ndi kunditonthozanso.

22Ndidzakutamandani ndi zeze

chifukwa cha kukhulupirika kwanu Mulungu,

ndidzayimba matamando kwa Inu ndi pangwe,

Inu Woyera wa Israeli.

23Milomo yanga idzafuwula ndi chimwemwe

pamene ndidzayimba matamando kwa Inu

amene mwandiwombola.

24Lilime langa lidzafotokoza za ntchito zanu zachilungamo

tsiku lonse,

pakuti iwo amene amafuna kundipweteka

achititsidwa manyazi ndi kusokonezedwa.

New Serbian Translation

Псалми 71:1-24

Псалам 71

1У теби је уточиште моје, Господе;

о, да се никад не постидим.

2Ослободи ме по својој праведности и избави ме,

пригни ухо своје к мени и спаси ме.

3Буди ми стена пребивалишта

којој увек долазим;

спасење моје ти си заповедио,

јер си моја стена и тврђава.

4Избави ме, Боже мој, из руке зликовачке,

од руке преступника и окрутнога.

5Јер, ти си моја нада, о, Боже Господе,

поуздање си ми од младости моје.

6На тебе се ослањам од утробе,

из крила мајке моје си ме извукао;

славићу те непрестано.

7Попут знака постао сам многима,

а ти си ми уточиште јако.

8Уста си ми славом својом испунио

и красотом својом од јутра до сутра.

9Не одбаци ме у доба старости,

кад ми снага клоне не заборави ме.

10Јер о мени говоре противници моји,

они што ми живот вребају

заједно се саветују.

11Кажу: „Бог је њега оставио!

Гоните га, ухватите,

јер избавитеља нема!“

12Боже, од мене се не удаљуј!

О, мој Боже, пожури ми у помоћ!

13Нека се постиде и нека пропадну

тужитељи моје душе;

и презир и брука нек покрију

оне који ми о глави раде.

14А ја ћу увек да се надам,

све више и више славићу те.

15Уста ће моја о праведности твојој да говоре,

о делима твог спасења од јутра до сутра,

јер им броја не знам.

16У моћним делима Бога Господа ја ћу доћи,

твоју праведност ћу спомињати, само твоју.

17Од младости моје, Боже, ти си ме учио;

и чудеса твоја досад јављао сам.

18Чак и када остарим и оседим,

Боже, не остављај ме,

док ти силу не објавим нараштају новом;

силу твоју сваком што долази.

19Праведност је твоја, Боже, до висина,

велика си дела учинио;

ко је попут тебе, Боже?

20Ти – дао си да гледам многе невоље и муке –

ти ћеш ми опет обновити живот;

из дубина земље подићеш ме опет.

21Ти ојачај достојанство моје

и поново утеши ме.

22И ја ћу харфом да те хвалим

због верности твоје;

Боже мој, свираћу ти на лири,

Светитељу Израиљев.

23Клицаће радосно усне моје,

јер ћу ти свирати,

и душа моја што си је откупио.

24И мој ће језик од јутра до сутра

причати о твојој праведности;

јер ће се постидети, јер ће се осрамотити

ти што ми о глави раде.