Masalimo 71 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 71:1-24

Salimo 71

1Mwa Inu Yehova ine ndathawiramo;

musalole kuti ndichititsidwe manyazi.

2Mundilanditse ndi kundipulumutsa mwa chilungamo chanu,

mutchere khutu lanu ndi kundipulumutsa.

3Mukhale thanthwe langa lothawirapo,

kumene ine nditha kupita nthawi zonse;

lamulani kuti ndipulumuke,

pakuti Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa.

4Landitseni Inu Mulungu wanga, kuchoka mʼdzanja la oyipa,

kuchoka mʼdzanja la oyipa ndi anthu ankhanza.

5Pakuti Inu mwakhala chiyembekezo changa, Inu Ambuye Wamphamvuzonse,

chilimbikitso changa kuyambira ndili mwana.

6Kuyambira pamene ndinabadwa, ndakhala ndikudalira Inu;

Inu munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga,

ndipo ndidzakupembedzani nthawi zonse.

7Ine ndakhala chinthu chodabwitsa kwa anthu ambiri

koma Inu ndinu wonditchinjiriza wamphamvu.

8Pakamwa panga padzaza ndi matamando anu,

kulengeza ulemerero wanu tsiku lonse.

9Musanditaye pamene ndakalamba;

musandisiye pamene mphamvu zanga zatha.

10Pakuti adani anga ayankhula motsutsana nane;

iwo amene amadikira kuti andiphe amapangana pamodzi.

11Iwo amati, “Mulungu wamusiya;

mutsatireni ndi kumugwira,

pakuti palibe amene adzamupulumutse.”

12Musakhale kutali ndi ine Inu Mulungu,

bwerani msanga, Inu Mulungu wanga; thandizeni.

13Ondineneza anga awonongeke mwa manyazi,

iwo amene akufuna kundipweteka

avale chitonzo ndi manyazi.

14Koma ine ndidzakhala ndi chiyembekezo mwa Inu nthawi zonse,

ndidzakutamandani mowirikizawirikiza.

15Pakamwa panga padzafotokoza za chilungamo chanu,

za chipulumutso chanu tsiku lonse,

ngakhale sindikudziwa muyeso wake.

16Ndidzabwera ndi kulengeza za machitidwe amphamvu zanu Inu Ambuye Wamphamvuzonse.

Ndidzalengeza chilungamo chanu, chanu chokha.

17Kuyambira ubwana wanga, Inu Mulungu mwakhala mukundiphunzitsa,

ndipo mpaka lero ine ndikulengeza za ntchito zanu zodabwitsa

18Ngakhale pamene ndakalamba ndipo imvi zili mbuu

musanditaye Inu Mulungu,

mpaka nditalengeza mphamvu zanu

kwa mibado yonse yakutsogolo.

19Mphamvu zanu ndi kulungama kwanu zimafika mpaka kumwambamwamba.

Ndani wofanana nanu Inu Mulungu,

amene mwachita zazikulu?

20Ngakhale mwandionetsa mavuto

ambiri owawa,

mudzabwezeretsanso moyo wanga;

kuchokera kunsi kwa dziko lapansi,

mudzandiukitsanso.

21Inu mudzachulukitsa ulemu wanga

ndi kunditonthozanso.

22Ndidzakutamandani ndi zeze

chifukwa cha kukhulupirika kwanu Mulungu,

ndidzayimba matamando kwa Inu ndi pangwe,

Inu Woyera wa Israeli.

23Milomo yanga idzafuwula ndi chimwemwe

pamene ndidzayimba matamando kwa Inu

amene mwandiwombola.

24Lilime langa lidzafotokoza za ntchito zanu zachilungamo

tsiku lonse,

pakuti iwo amene amafuna kundipweteka

achititsidwa manyazi ndi kusokonezedwa.

New International Reader’s Version

Psalm 71:1-24

Psalm 71

1Lord, I have gone to you for safety.

Let me never be put to shame.

2You do what is right, so save me and help me.

Pay attention to me and save me.

3Be my rock of safety

that I can always go to.

Give the command to save me.

You are my rock and my fort.

4My God, save me from the power of sinners.

Save me from the hands of those who are mean and evil.

5You are the King and the Lord. You have always been my hope.

I have trusted in you ever since I was young.

6From the time I was born I have depended on you.

You brought me out of my mother’s body.

I will praise you forever.

7To many people I am an example of how much you care.

You are my strong place of safety.

8My mouth is filled with praise for you.

All day long I will talk about your glory.

9Don’t push me away when I’m old.

Don’t desert me when my strength is gone.

10My enemies speak against me.

Those who want to kill me get together and make evil plans.

11They say, “God has deserted him.

Go after him and grab him.

No one will save him.”

12God, don’t be far away from me.

My God, come quickly and help me.

13May those who bring charges against me die in shame.

May those who want to harm me

be covered with shame and dishonor.

14But I will always have hope.

I will praise you more and more.

15I will tell other people about all the good things you have done.

All day long I will talk about how you have saved your people.

But there’s no way I could say how many times you’ve done this.

16Lord and King, I will come and announce your mighty acts.

I will announce all the good things that you alone do.

17God, ever since I was young you have taught me.

To this very day I tell about your wonderful acts.

18God, don’t leave me

even when I’m old and have gray hair.

Let me live to tell my children about your power.

Let me tell all of them about your mighty acts.

19God, your saving acts reach to the skies.

You have done great things.

God, who is like you?

20You have sent many bitter troubles my way.

But you will give me new life.

Even if I’m almost in the grave,

you will bring me back.

21You will honor me more and more.

You will comfort me once again.

22My God, I will use the harp to praise you

because you are always faithful.

Holy One of Israel,

I will use the lyre to sing praise to you.

23My lips will shout with joy

when I sing praise to you.

You have saved me.

24All day long my tongue will say

that you have done what is right.

Those who wanted to harm me have been put to shame.

They have not been honored.