Masalimo 7 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 7:1-17

Salimo 7

Sigioni wa Davide, amene anayimbira Yehova zokhudza Kusi, wa fuko la Benjamini.

1Inu Yehova Mulungu wanga, Ine ndikuthawira kwa Inu;

pulumutseni ndi kundilanditsa kwa onse amene akundithamangitsa,

2mwina angandikadzule ngati mkango,

ndi kundingʼamba popanda wondipulumutsa.

3Inu Yehova Mulungu wanga,

ngati ndachita izi ndipo ndapezeka wolakwa,

4ngati ndachita zoyipa kwa iye amene ndili naye pa mtendere,

kapena popanda chifukwa ndalanda mdani wanga,

5pamenepo lolani adani anga andithamangitse ndi kundipitirira,

lolani kuti moyo wanga aupondereze pansi

ndipo mundigoneke pa fumbi.

Sela

6Nyamukani Yehova, mu mkwiyo wanu;

nyamukani kutsutsana ndi mkwiyo wa adani anga.

Dzukani Mulungu wanga, lamulirani chilungamo chanu.

7Lolani gulu la anthu a mitundu ina lisonkhane mokuzungulirani.

Alamulireni muli kumwambako;

8Yehova aweruzeni anthu a mitundu inayo.

Ndiweruzeni Yehova, monga mwa chilungamo changa,

monga mwa moyo wanga wangwiro, Inu Wammwambamwamba.

9Inu Mulungu wolungama,

amene mumasanthula maganizo ndi mitima,

thetsani chiwawa cha anthu oyipa

ndipo wolungama akhale motetezedwa.

10Chishango changa ndi Mulungu Wammwambamwamba,

amene amapulumutsa olungama mtima.

11Mulungu amaweruza molungama,

Mulungu amene amaonetsa ukali wake tsiku ndi tsiku.

12Ngati munthu satembenuka,

Mulungu adzanola lupanga lake,

Iye adzawerama ndi kukoka uta.

13Mulungu wakonza zida zake zoopsa;

Iye wakonzekera mivi yake yoyaka moto.

14Taonani, munthu woyipa amalingalira zoyipa zokhazokha nthawi zonse.

Zochita zake ndi zosokoneza ndi zovutitsa anthu ena.

15Iye amene akumba dzenje ndi kulizamitsa

amagwera mʼdzenje limene wakumbalo.

16Mavuto amene amayambitsa amamubwerera mwini;

chiwawa chake chimatsikira pa mutu wake womwe.

17Ine ndidzayamika Yehova chifukwa cha chilungamo chake;

ndipo ndidzayimba nyimbo zamatamando pa dzina la Yehova Wammwambamwamba.

New Russian Translation

Псалтирь 7:1-18

Псалом 7

1Плачевная песнь7:1 Евр.: «шиггайон». Точное значение этого термина сегодня неизвестно. Возможно, он относится либо к сюжету песни, либо указывает на акцентированный ритм и патетическую манеру исполнения. Давида, которую он воспел Господу из-за вениамитянина Куша.

2Господи, мой Боже, у Тебя я ищу прибежища.

Спаси меня и избавь от всех, кто меня преследует,

3иначе, как лев, меня разорвут,

растерзают – и не будет спасителя.

4Господи, мой Боже, если я это сделал,

если есть несправедливость в моих руках,

5если я сделал зло тому,

кто со мною в мире,

или врага без повода обобрал,

6то пусть враг за мною погонится и настигнет,

пусть он жизнь мою втопчет в землю

и повергнет славу мою в прах. Пауза

7Господи, восстань в гневе Своем,

ополчись на неистовство моих врагов!

Пробудись, заступись за меня на суде,

который Ты заповедал!

8Пусть окружат Тебя собравшиеся народы,

воссядь7:8 Вероятный текст; букв.: «возвратись». над ними на высоте.

9Судит Господь народы.

Оправдай меня, Господи, по праведности моей,

по моей непорочности, Всевышний.

10Праведный Бог, судящий помыслы и сердце,

положи конец беззаконию нечестивых,

но праведного укрепи.

11Щит мой – Бог Высочайший,

спасающий правых сердцем.

12Бог – судья справедливый,

Бог, строго взыскивающий каждый день.

13Если кто7:13 Или: «Если Он». не раскается,

Он наточит Свой меч, согнет лук

и оснастит его тетивой,

14приготовит оружие смертоносное

и огненными сделает стрелы.

15Кто несчастье зачал

и носит под сердцем беду,

тот разрешится от бремени ложью.

16Кто рыл и выкопал яму,

сам в нее упадет.

17Зло его к нему же и вернется,

на него обратится его жестокость.

18Восславлю Господа: праведен Он,

воспою хвалу имени Господа Всевышнего7:18 Евр.: «ЙГВГ Эльон»..