Masalimo 68 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 68:1-35

Salimo 68

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Adzuke Mulungu, adani ake amwazikane;

adani ake athawe pamaso pake.

2Monga momwe mphepo imachotsera utsi; Inu muwawulutsire kutali.

Monga phula limasungunukira pa moto,

oyipa awonongeke pamaso pa Mulungu.

3Koma olungama asangalale

ndi kukondwera pamaso pa Mulungu;

iwo akondwere ndi kusangalala.

4Imbirani Mulungu imbirani dzina lake matamando,

mukwezeni Iye amene amakwera pa mitambo;

dzina lake ndi Yehova ndipo sangalalani pamaso pake.

5Atate wa ana amasiye, mtetezi wa akazi amasiye,

ndiye Mulungu amene amakhala mʼmalo oyera.

6Mulungu amakhazikitsa mtima pansi osungulumwa mʼmabanja,

amatsogolera amʼndende ndi kuyimba;

koma anthu osamvera amakhala ku malo owuma a dziko lapansi.

7Pamene munatuluka kutsogolera anthu anu, Inu Mulungu,

pamene munayenda kudutsa chipululu,

8dziko lapansi linagwedezeka, miyamba inakhuthula pansi mvula,

pamaso pa Mulungu, Mmodzi uja wa ku Sinai.

Pamaso pa Mulungu, Mulungu wa Israeli.

9Munapereka mivumbi yochuluka, Inu Mulungu;

munatsitsimutsa cholowa chanu cholefuka.

10Anthu anu anakhala mʼmenemo

ndipo munapatsa anthu osauka zimene zinkawasowa chifukwa cha ubwino wanu Mulungu.

11Ambuye analengeza mawu,

ndipo gulu linali lalikulu la iwo amene anapita kukawafalitsa;

12“Mafumu ndi ankhondo anathawa mwaliwiro;

mʼmisasa anthu anagawana zolanda pa nkhondo.

13Ngakhale mukugona pakati pa makola a ziweto,

mapiko a nkhunda akutidwa ndi siliva,

nthenga zake ndi golide wonyezimira.”

14Pamene Wamphamvuzonse anabalalitsa mafumu mʼdziko,

zinali ngati matalala akugwa pa Zalimoni.

15Mapiri a Basani ndi mapiri aulemerero;

mapiri a Basani, ndi mapiri a msonga zambiri.

16Muyangʼaniranji mwansanje inu mapiri a msonga zambiri,

pa phiri limene Mulungu analisankha kuti azilamulira,

kumene Yehova mwini adzakhalako kwamuyaya?

17Magaleta a Mulungu ndi osawerengeka,

ndi miyandamiyanda;

Ambuye wabwera kuchokera ku Sinai, walowa mʼmalo ake opatulika.

18Pamene Inu munakwera mmwamba,

munatsogolera a mʼndende ambiri;

munalandira mphatso kuchokera kwa anthu,

ngakhale kuchokera kwa owukira,

kuti Inu Mulungu, mukhale kumeneko.

19Matamando akhale kwa Ambuye, kwa Mulungu Mpulumutsi wathu

amene tsiku ndi tsiku amasenza zolemetsa zathu.

20Mulungu wathu ndi Mulungu amene amapulumutsa;

Ambuye Wamphamvuzonse ndiye amene amatipulumutsa ku imfa.

21Ndithu Mulungu adzaphwanya mitu ya adani ake,

zipewa za ubweya za iwo amene amapitiriza kuchita machimo awo.

22Ambuye akunena kuti, “Ndidzawabweretsa kuchokera ku Basani;

ndidzawabweretsa kuchokera ku nyanja zozama.

23Kuti muviyike mapazi anu mʼmagazi a adani anu,

pamene malilime a agalu anu akudyapo gawo lawo.”

24Mayendedwe aulemu a anthu anu aonekera poyera, Inu Mulungu;

mayendedwe olemekeza Mulungu wanga ndi Mfumu yanga yokalowa mʼmalo opatulika.

25Patsogolo pali oyimba nyimbo pakamwa, pambuyo pawo oyimba nyimbo ndi zipangizo;

pamodzi ndi iwo pali atsikana akuyimba matambolini.

26Tamandani Mulungu mu msonkhano waukulu;

tamandani Yehova mu msonkhano wa Israeli.

27Pali fuko lalingʼono la Benjamini, kuwatsogolera,

pali gulu lalikulu la ana a mafumu a Yuda,

ndiponso pali ana a mafumu a Zebuloni ndi Nafutali.

28Kungani mphamvu zanu Mulungu;

tionetseni nyonga zanu, Inu Mulungu, monga munachitira poyamba.

29Chifukwa cha Nyumba yanu ku Yerusalemu,

mafumu adzabweretsa kwa Inu mphatso.

30Dzudzulani chirombo pakati pa mabango,

gulu la ngʼombe zazimuna pakati pa ana angʼombe a mitundu ya anthu.

Mochititsidwa manyazi, abweretse mitanda ya siliva.

Balalitsani anthu a mitundu ina amene amasangalatsidwa ndi nkhondo.

31Nthumwi zidzachokera ku Igupto;

Kusi adzadzipereka yekha kwa Mulungu.

32Imbirani Mulungu Inu mafumu a dziko lapansi

imbirani Ambuye matamando.

Sela

33Kwa Iye amene amakwera pa mitambo yakalekale ya mmwamba

amene amabangula ndi mawu amphamvu.

34Lengezani za mphamvu za Mulungu,

amene ulemerero wake uli pa Israeli

amene mphamvu zake zili mʼmitambo.

35Ndinu woopsa, Inu Mulungu mʼmalo anu opatulika;

Mulungu wa Israeli amapereka mphamvu ndi nyonga kwa anthu ake.

Matamando akhale kwa Mulungu!

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Забур 68:1-37

Песнь 68

1Дирижёру хора. На мотив «Лилии». Песнь Довуда.

2Спаси меня, Всевышний,

потому что воды поднялись до шеи моей!

3Я погряз в глубоком иле, и нет опоры;

вошёл в глубокие воды, и потоком накрыло меня.

4Устал я, взывая о помощи;

иссушено моё горло.

Я выплакал глаза свои

в ожидании моего Бога.

5Ненавидящих меня без всякой причины

стало больше, чем волос на моей голове.

Умножились враги мои,

несправедливо меня преследующие.

То, чего не отнимал,

я должен отдать.

6Всевышний, Ты знаешь глупость мою,

и грехи мои от Тебя не сокрыты.

7Да не смущу я тех, кто надеется на Тебя,

Владыка Вечный, Повелитель Сил.

Пусть не будут опозорены из-за меня те,

кто ищет Тебя, Бог Исроила.

8Ведь ради Тебя сношу я упрёки,

и позор покрыл моё лицо.

9Изгоем я стал для братьев моих,

чужим для сыновей матери моей,

10потому что ревность о доме Твоём снедает меня,

и оскорбления тех, кто злословит Тебя, пали на меня.

11Когда я плакал и постился,

это ставили мне в упрёк.

12Когда я одевался в рубище,

я был посмешищем для них.

13Беседуют обо мне старейшины, сидящие у ворот68:13 Ворота города были центром всей общественной жизни, около них проходили и судебные разбирательства.,

и поют обо мне пьяницы.

14А я молюсь Тебе, Вечный,

во время Твоего благоволения.

По Своей великой милости ответь мне, Всевышний,

и в верности Твоей спаси меня.

15Вытащи меня из тины

и не дай погрязнуть мне!

Дай избавиться от ненавистников моих,

от вод глубоких!

16Да не накроет меня потоком вод,

и да не поглотит меня глубина,

и да не сомкнёт надо мной яма пасть свою.

17Ответь мне, Вечный, потому что благостна милость Твоя;

по Своей великой милости посмотри на меня.

18Не скрывай Своего лица от раба Твоего,

ведь я в беде.

Поспеши, ответь мне!

19Приблизься и избавь меня,

от моих врагов спаси!

20Ты знаешь, как меня презирают,

как бесчестят и позорят меня;

все враги мои пред Тобой.

21Поругание разбило моё сердце, и я сокрушён.

Рассчитывал на сострадание, но нет его,

на утешителей, но не нашёл их.

22Дали мне в пищу желчь;

при жажде моей уксусом меня напоили68:22 См. Мат. 27:34, 48; Мк. 15:36; Лк. 23:36; Ин. 19:29..

23Пусть их праздничные застолья станут для них ловушкой,

а священные праздники – западнёй68:23 Или: «ловушкой, возмездием и западнёй»..

24Пусть их глаза померкнут, чтобы они не видели,

и пусть их спины согнутся навсегда.

25Пролей на них Своё негодование,

и пусть пылающий гнев Твой настигнет их.

26Пусть их жилище будет в запустении;

пусть никто в шатрах их больше не живёт,

27потому что они преследуют тех, кого Ты и без того поразил,

и говорят о страданиях поверженных Тобою.

28Прибавь грех этот к грехам их,

и оправдания пусть не найдут они.

29Пусть будут вычеркнуты они из книги жизни

и да не будут записаны там вместе с праведниками.

30Я же угнетён и страдаю.

Спасение Твоё, Всевышний, пусть возвысит меня!

31Буду славить имя Всевышнего в песне,

буду превозносить Его с благодарностью.

32Это будет приятней Вечному, нежели вол,

приятнее, чем молодой бык с рогами и копытами.

33Когда увидят угнетённые, обрадуются.

Ищущие Всевышнего, пусть оживут ваши сердца!

34Вечный слышит нуждающихся

и узниками Своими не пренебрегает.

35Да восхвалят Его небеса и земля,

моря и всё, что живёт в них,

36потому что Всевышний освободит Иерусалим68:36 Букв.: «Сион».

и восстановит города Иудеи.

Его народ будет жить там и владеть ими,

37потомки Его рабов унаследуют их,

и любящие Его имя будут проживать в них.