Salimo 67
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo.
1Yehova atikomere mtima ndi kutidalitsa,
achititse kuti nkhope yake itiwalire.
2Kuti njira zanu zidziwike pa dziko lapansi,
chipulumutso chanu pakati pa mitundu yonse.
3Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu;
mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
4Mitundu yonse ya anthu isangalale ndi kuyimba mwachimwemwe,
pakuti inu mumaweruza mitundu ya anthu mwachilungamo
ndi kutsogolera mitundu ya anthu a dziko lapansi.
5Mitundu ya anthu ikutamandeni Inu Mulungu;
mitundu yonse ya anthu ikutamandeni.
6Nthaka yabereka zokolola zake;
tidalitseni Mulungu wathu.
7Mulungu atidalitse
kuti pamenepo malekezero onse a dziko lapansi apembedze Iyeyo.
Psalm 67In Hebrew texts 67:1-7 is numbered 67:2-8.
For the director of music. With stringed instruments. A psalm. A song.
1May God be gracious to us and bless us
and make his face shine on us—67:1 The Hebrew has Selah (a word of uncertain meaning) here and at the end of verse 4.
2so that your ways may be known on earth,
your salvation among all nations.
3May the peoples praise you, God;
may all the peoples praise you.
4May the nations be glad and sing for joy,
for you rule the peoples with equity
and guide the nations of the earth.
5May the peoples praise you, God;
may all the peoples praise you.
6The land yields its harvest;
God, our God, blesses us.
7May God bless us still,
so that all the ends of the earth will fear him.