Salimo 65
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Nyimbo.
1Matamando akudikira Inu Mulungu mu Ziyoni;
kwa inu malumbiro athu adzakwaniritsidwa.
2Inu amene mumamva pemphero,
kwa inu anthu onse adzafika.
3Pamene tinathedwa nzeru ndi machimo,
Inu munakhululukira mphulupulu zathu.
4Odala iwo amene inu muwasankha
ndi kuwabweretsa pafupi kukhala mʼmabwalo anu!
Ife tadzazidwa ndi zinthu zabwino za mʼNyumba mwanu,
za mʼNyumba yanu yoyera.
5Mumatiyankha ife ndi ntchito zodabwitsa zachilungamo,
Inu Mulungu Mpulumutsi wathu,
chiyembekezo cha mathero onse a dziko lapansi
ndi cha nyanja zomwe zili kutali kwambiri,
6amene munapanga mapiri ndi mphamvu zanu,
mutadziveka nokha ndi mphamvu.
7Amene munakhalitsa bata nyanja
kukokoma kwa mafunde ake,
ndi phokoso la anthu a mitundu ina.
8Iwo amene akukhala kutali amaopa zizindikiro zozizwitsa zanu;
kumene dzuwa limatulukira ndi kumene dzuwa limalowera.
Inu mumafuna nyimbo zachimwemwe.
9Inu mumasamalira dziko lapansi ndi kulithirira;
Inuyo mumalilemeretsa kwambiri.
Mtsinje wa Mulungu ndi wodzaza ndi madzi
kuti upereke tirigu kwa anthu,
pakuti Inu munakhazikitsa zimenezi.
10Mwadzaza nthaka yake ndi madzi ndi kusalaza migula yake,
mwayifewetsa ndi mvula yamawawa ndi kudalitsa mbewu zake.
11Inu mumaveka chaka ndi zinthu zochuluka,
ndipo ngolo zanu zimasefukira ndi zinthu zochuluka.
12Malo a udzu a mʼchipululu amasefukira;
mapiri avekedwa ndi chisangalalo.
13Madambo akutidwa ndi zoweta
ndi zigwa zavekedwa ndi tirigu;
izo pamodzi zikufuwula ndi kuyimba mwachimwemwe.
Psalmul 65
Pentru dirijor. Un psalm al lui David. O cântare.
1Dumnezeule, pe Tine Te așteaptă lauda1 Sau: Dumnezeule, pentru Tine, tăcere, laudă. în Sion;
față de Tine va fi împlinit jurământul.
2Tu asculți rugăciunea;
la Tine vor veni toți oamenii.
3Poverile nelegiuirilor noastre ne copleșesc,
dar Tu faci ispășire pentru fărădelegile noastre.
4Ferice de cel pe care‑l alegi,
pe care‑l apropii să locuiască în curțile Tale!
Ne vom sătura de lucrurile bune ale Casei Tale,
ale Templului Tău cel sfânt.
5Tu ne răspunzi prin lucrări de temut, cu dreptate,
Dumnezeul mântuirii noastre,
Încrederea tuturor marginilor pământului
și ale mărilor îndepărtate,
6Cel Ce a întemeiat munții cu puterea Sa,
fiind încins cu tărie,
7Cel Ce potolește vuietul mărilor,
vuietul talazurilor lor și tumultul noroadelor.
8Locuitorii de la marginile pământului se tem din cauza minunilor Tale!
Tu faci să răsune de bucurie locurile de unde se ivesc dimineața și seara.
9Tu cercetezi pământul și‑l faci să se reverse;
îl îmbogățești mult.
Râul lui Dumnezeu este plin de apă.
Tu le dai oamenilor grâne, căci așa pregătești Tu pământul:
10îi uzi brazdele, îi sfărâmi bulgării,
îl înmoi cu aversele și îi binecuvântezi răsadul.
11Încununezi anul cu bunătățile Tale,
în urma Ta mustește belșugul;11 Sau: din carele Tale se prelinge belșugul.
12mustesc, de asemenea, și pășunile din pustie,
iar dealurile se încing cu veselie.
13Pășunile sunt îmbrăcate cu turme,
văile se acoperă de grâne;
toate strigă de bucurie și cântă.