Masalimo 65 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 65:1-13

Salimo 65

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Nyimbo.

1Matamando akudikira Inu Mulungu mu Ziyoni;

kwa inu malumbiro athu adzakwaniritsidwa.

2Inu amene mumamva pemphero,

kwa inu anthu onse adzafika.

3Pamene tinathedwa nzeru ndi machimo,

Inu munakhululukira mphulupulu zathu.

4Odala iwo amene inu muwasankha

ndi kuwabweretsa pafupi kukhala mʼmabwalo anu!

Ife tadzazidwa ndi zinthu zabwino za mʼNyumba mwanu,

za mʼNyumba yanu yoyera.

5Mumatiyankha ife ndi ntchito zodabwitsa zachilungamo,

Inu Mulungu Mpulumutsi wathu,

chiyembekezo cha mathero onse a dziko lapansi

ndi cha nyanja zomwe zili kutali kwambiri,

6amene munapanga mapiri ndi mphamvu zanu,

mutadziveka nokha ndi mphamvu.

7Amene munakhalitsa bata nyanja

kukokoma kwa mafunde ake,

ndi phokoso la anthu a mitundu ina.

8Iwo amene akukhala kutali amaopa zizindikiro zozizwitsa zanu;

kumene dzuwa limatulukira ndi kumene dzuwa limalowera.

Inu mumafuna nyimbo zachimwemwe.

9Inu mumasamalira dziko lapansi ndi kulithirira;

Inuyo mumalilemeretsa kwambiri.

Mtsinje wa Mulungu ndi wodzaza ndi madzi

kuti upereke tirigu kwa anthu,

pakuti Inu munakhazikitsa zimenezi.

10Mwadzaza nthaka yake ndi madzi ndi kusalaza migula yake,

mwayifewetsa ndi mvula yamawawa ndi kudalitsa mbewu zake.

11Inu mumaveka chaka ndi zinthu zochuluka,

ndipo ngolo zanu zimasefukira ndi zinthu zochuluka.

12Malo a udzu a mʼchipululu amasefukira;

mapiri avekedwa ndi chisangalalo.

13Madambo akutidwa ndi zoweta

ndi zigwa zavekedwa ndi tirigu;

izo pamodzi zikufuwula ndi kuyimba mwachimwemwe.

New Russian Translation

Псалтирь 65:1-20

Псалом 65

1Дирижеру хора. Песнь. Псалом.

Восклицай Богу от радости, вся земля!

2Пойте славу Его имени,

воздайте Ему хвалу.

3Скажите Богу: «Как устрашающи Твои дела!

Столь велика сила Твоя,

что враги Твои раболепствуют пред Тобою.

4Тебе поклоняется вся земля,

Тебе воспевает славу,

воспевает славу имени Твоему». Пауза

5Придите, смотрите на Божьи дела;

как устрашающи Его дела для сынов человеческих!

6Сушей Он сделал море65:6 См. Исх. 14.,

реку они перешли по суше65:6 См. Нав. 3.,

и там мы возрадовались о Нем.

7Силой Своей Он властвует вовек,

не спускает с народов глаз,

чтобы мятежники против Него не восстали. Пауза

8Славьте нашего Бога, народы,

громко воздайте хвалу Ему.

9Он сохранил нам жизнь

и не дал нашим ногам споткнуться.

10Боже, Ты испытал нас,

очистил, как серебро.

11Ты заключил нас в неволю,

возложил нам на спину бремя

12и позволил конникам попирать нас.

Мы прошли сквозь огонь и воду,

но Ты нас вывел к месту изобилия.

13Я приду в Твой храм со всесожжениями

и исполню свои обеты Тебе –

14обеты, что дали мои уста,

и язык мой произнес, когда я был в беде.

15Я вознесу Тебе всесожжения –

дым от лучших баранов;

я принесу Тебе в жертву быков и козлов. Пауза

16Придите и слушайте, все боящиеся Бога,

я расскажу о том, что Он для меня совершил.

17Я взывал к Нему устами своими,

превозносил его языком моим.

18Если бы в сердце своем видел я грех,

то Владыка не слушал бы меня.

19Но Бог поистине услышал меня

и внял мольбе моей.

20Благословен будь, Бог,

не отвергший мою молитву

и милости меня не лишивший!